< Job 36 >

1 Élihu continua et dit:
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 Attends un peu, et je vais poursuivre, Car j’ai des paroles encore pour la cause de Dieu.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 Je prendrai mes raisons de haut, Et je prouverai la justice de mon créateur.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 Sois-en sûr, mes discours ne sont pas des mensonges, Mes sentiments devant toi sont sincères.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 Dieu est puissant, mais il ne rejette personne; Il est puissant par la force de son intelligence.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 Il ne laisse pas vivre le méchant, Et il fait droit aux malheureux.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 Il ne détourne pas les yeux de dessus les justes, Il les place sur le trône avec les rois, Il les y fait asseoir pour toujours, afin qu’ils soient élevés.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 Viennent-ils à tomber dans les chaînes, Sont-ils pris dans les liens de l’adversité,
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 Il leur dénonce leurs œuvres, Leurs transgressions, leur orgueil;
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 Il les avertit pour leur instruction, Il les exhorte à se détourner de l’iniquité.
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 S’ils écoutent et se soumettent, Ils achèvent leurs jours dans le bonheur, Leurs années dans la joie.
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 S’ils n’écoutent pas, ils périssent par le glaive, Ils expirent dans leur aveuglement.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 Les impies se livrent à la colère, Ils ne crient pas à Dieu quand il les enchaîne;
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Ils perdent la vie dans leur jeunesse, Ils meurent comme les débauchés.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 Mais Dieu sauve le malheureux dans sa misère, Et c’est par la souffrance qu’il l’avertit.
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 Il te retirera aussi de la détresse, Pour te mettre au large, en pleine liberté, Et ta table sera chargée de mets succulents.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Mais si tu défends ta cause comme un impie, Le châtiment est inséparable de ta cause.
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Que l’irritation ne t’entraîne pas à la moquerie, Et que la grandeur de la rançon ne te fasse pas dévier!
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Tes cris suffiraient-ils pour te sortir d’angoisse, Et même toutes les forces que tu pourrais déployer?
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Ne soupire pas après la nuit, Qui enlève les peuples de leur place.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Garde-toi de te livrer au mal, Car la souffrance t’y dispose.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 Dieu est grand par sa puissance; Qui saurait enseigner comme lui?
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Qui lui prescrit ses voies? Qui ose dire: Tu fais mal?
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Souviens-toi d’exalter ses œuvres, Que célèbrent tous les hommes.
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 Tout homme les contemple, Chacun les voit de loin.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 Dieu est grand, mais sa grandeur nous échappe, Le nombre de ses années est impénétrable.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 Il attire à lui les gouttes d’eau, Il les réduit en vapeur et forme la pluie;
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 Les nuages la laissent couler, Ils la répandent sur la foule des hommes.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 Et qui comprendra le déchirement de la nuée, Le fracas de sa tente?
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 Voici, il étend autour de lui sa lumière, Et il se cache jusque dans les profondeurs de la mer.
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 Par ces moyens il juge les peuples, Et il donne la nourriture avec abondance.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 Il prend la lumière dans sa main, Il la dirige sur ses adversaires.
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 Il s’annonce par un grondement; Les troupeaux pressentent son approche.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

< Job 36 >