< Jérémie 16 >

1 La parole de l’Eternel me fut adressée en ces termes:
Kenaka Yehova anandiwuza kuti,
2 "Tu n’épouseras pas de femmes et n’auras ni fils ni fille en ces lieux.
“Usadzakwatire ndi kubereka ana aamuna kapena aakazi malo ano
3 Car voici ce que décrète l’Eternel contre les fils et les filles qui naissent en ces lieux, contre leurs mères qui les mettent au jour et contre les pères qui leur donnent la vie en ce pays:
pakuti ana aamuna ndi ana aakazi obadwira mʼdziko muno, komanso amayi awo ndi abambo awo amene anabereka anawo mʼdziko muno,
4 Ils mourront atteints de maladies virulentes et ne seront ni pleurés ni ensevelis; ils serviront de fumier, sur la surface du sol. Et aussi par le glaive et par la famine ils périront, et leur cadavre servira de pâture aux oiseaux du ciel et aux animaux de la terre."
adzafa ndi nthenda zoopsa. Sadzawalira maliro kapena kuyikidwa mʼmanda koma adzakhala ngati ndowe zotayikira pansi. Ena adzaphedwa ku nkhondo ndipo ena adzafa ndi njala. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo zakuthengo.”
5 En vérité, ainsi parle l’Eternel: "N’Entre pas dans une maison de deuil, n’y va point porter des paroles de regret ni des paroles de compassion, car j’ai retiré mon amitié à ce peuple, dit l’Eternel, la bienveillance et la miséricorde.
Yehova akuti, “Usalowe mʼnyumba ya maliro; usapite kukalira maliro kapena kukapepesa, chifukwa Ine ndawachotsera madalitso anga, chikondi changa ndi chifundo changa.”
6 Grands et petits mourront en ce pays et ne recevront pas de sépulture; on ne les plaindra pas, et pour eux on ne se fera pas d’incision ni on ne se rasera les cheveux.
Akuluakulu ndi angʼonoangʼono omwe adzafa mʼdziko muno. Sadzayikidwa mʼmanda kapena kuliridwa, ndipo palibe amene adzaonetse chisoni podzichekacheka kapena kumeta tsitsi lake chifukwa cha iwo.
7 A cause d’eux, on ne rompra pas le pain de deuil pour consoler ceux qui pleurent un mort, et on ne leur présentera pas à boire la coupe de consolation pour un père et pour une mère.
Palibe amene adzapereka chakudya kutonthoza amene akulira maliro, ngakhale kuti womwalirayo ndi abambo ake kapena amayi ake.
8 Tu éviteras de même d’entrer dans une salle de festin pour manger et boire en leur société."
“Ndipo usalowe mʼnyumba mmene muli madyerero, nʼkukhala pansi ndi kudya ndi kumwa nawo.
9 Car voici ce que dit l’Eternel-Cebaot, Dieu d’Israël: "Sous vos yeux et de votre temps, je vais supprimer de ces lieux les accents d’allégresse et les chants joyeux, la voix du fiancé et la voix de la fiancée.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Pa nthawi yanu, inu mukuona ndidzathetsa mawu achimwemwe ndi achisangalalo ndiponso mawu a mkwati ndi mkwatibwi pa malo ano.’
10 Et lorsque tu communiqueras à ce peuple toutes ces paroles et qu’ils te demanderont: Pourquoi Dieu menace-t-il de cette grande calamité? Quels sont donc nos péchés et nos fautes que nous aurions commis contre l’Eternel, notre Dieu?
“Ukawawuza anthu awa zinthu zonsezi akakufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wanena kuti tsoka lalikulu lotere lidzatigwere? Kodi talakwa chiyani? Kodi tamuchimwira tchimo lotani Yehova Mulungu wathu?’
11 Tu leur répondras: C’Est que vos pères m’ont abandonné, dit l’Eternel, pour suivre d’autres dieux, les adorer et se courber devant eux, tandis que, moi, ils m’ont abandonné, se refusant d’observer ma loi.
Pamenepo ukawawuze kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti makolo anu anandisiya Ine,’ akutero Yehova, ‘ndi kutsatira milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Iwo anandisiya Ine ndipo sanasunge lamulo langa.
12 Et vous avez fait pis encore que vos pères, car vous voici chacun en train de vous abandonner aux mauvais instincts de votre coeur pour ne pas m’écouter.
Komanso inu munachimwa kwambiri kupambana makolo anu. Aliyense wa inu akutsatira zoyipa ndi mtima wake wokanikawo mʼmalo mondimvera Ine.
13 Aussi vous rejetterai-je de ce pays dans un pays inconnu à vous et à vos pères, et là vous servirez, jour et nuit, d’autres dieux, car je ne vous ferai rencontrer aucune pitié."
Choncho Ine ndidzakubalalitsani mʼdziko muno ndi kukulowetsani mʼdziko limene inu ndi makolo anu simunalidziwe. Kumeneko mukatumikira milungu ina usana ndi usiku, ndipo sadzakuchitirani chifundo.’”
14 En vérité, des jours viendront, dit l’Eternel, où l’on ne dira plus: "Vive l’Eternel qui a fait monter les enfants d’Israël du pays d’Egypte!"
Yehova akuti, “Komabe masiku akubwera pamene anthu polumbira sadzatinso, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto,’
15 mais "Vive l’Eternel qui a fait monter les enfants d’Israël du pays du Nord et de toutes les contrées où il les avait exilés! "Car je les aurai ramenés sur leur territoire, que j’avais donné à leurs ancêtres.
koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku dziko lakumpoto, ndi ku mayiko onse kumene anawabalalitsirako.’ Pakuti ndidzawabwezera ku dziko limene ndinalipereka kwa makolo awo.”
16 Voici, je vais convoquer de nombreux pêcheurs, dit l’Eternel, qui les pêcheront; puis, je convoquerai de nombreux chasseurs qui les pourchasseront sur toute montagne, sur toute colline et dans les fentes des rochers;
Yehova akuti, “Koma tsopano ndidzayitana adani okhala ngati asodzi ambiri, ndipo adzawagwira ngati nsomba. Izi zitatha adani enanso okhala ngati alenje ambiri, adzawasaka pa phiri lililonse, pa chitunda chilichonse ndiponso mʼmapanga onse a mʼmatanthwe.
17 car mes yeux sont fixés sur toutes leurs voies; aucune ne me reste cachée, leur iniquité n’échappe point à mes regards.
Maso anga akuona makhalidwe awo onse; sanabisike pamaso panga. Palibe tchimo limene sindikulidziwa.
18 Et d’abord je paierai en double leurs méfaits et leurs fautes, puisqu’ils ont déshonore mon pays et rempli mon domaine de l’infamie de leurs abominations et de leurs horreurs.
Ndidzawalanga mowirikiza chifukwa cha kuyipa kwawo ndi tchimo lawo. Ndidzatero chifukwa ayipitsa dziko langa ndi mafano awo amene ali ngati mitembo, ndiponso adzaza cholowa changa ndi mafano awo onyansa.”
19 Eternel, ô ma force, mon appui et mon refuge au jour du malheur! Des peuples viendront à toi des confins de la terre et diront: "Nos ancêtres n’ont reçu pour héritage que le mensonge, que de vaines idoles, toutes également impuissantes.
Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga ndi linga langa, pothawirapo panga nthawi ya masautso, anthu a mitundu yonse adzabwera kwa Inu kuchokera ku mathero onse a dziko lapansi ndipo adzanena kuti, “Makolo anthu anali ndi milungu yonama, anali ndi mafano achabechabe amene sanawathandize.
20 Les hommes pourraient-ils se créer des dieux? Non, certes, ce ne sont pas des dieux!
Kodi anthu nʼkudzipangira milungu? Atati atero ndiye kuti imeneyo ikhala milungu yachabechabe.”
21 Aussi, vais-je le leur faire sentir; pour le coup, je leur ferai sentir mon bras et ma puissance, et ils apprendront que je me nomme l’Eternel.
“Choncho Ine ndidzawaphunzitsa, kokha kano kuti adziwe za mphamvu yanga ndi za nyonga zanga. Pamenepo adzadziwa kuti dzina langa ndi Yehova.

< Jérémie 16 >