< Isaïe 40 >

1 Consolez, consolez mon peuple, dit votre Dieu.
Atonthozeni, atonthozeni anthu anga, akutero Mulungu wanu.
2 Parlez au cœur de Jérusalem, et criez-lui: Que sa servitude est finie, que son iniquité est expiée, qu’elle a reçu de la main de Yahweh le double pour ses péchés.
Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu ndipo muwawuzitse kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha, tchimo lawo lakhululukidwa. Ndawalanga mokwanira chifukwa cha machimo awo onse.
3 Une voix crie: Frayez dans le désert le chemin de Yahweh, aplanissez dans la steppe une route pour notre Dieu!
Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti, “Konzani njira ya Yehova mʼchipululu; wongolani njira zake; msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
4 Que toute vallée soit relevée, toute montagne et toute colline abaissées; que la hauteur devienne une plaine, et les roches escarpées un vallon!
Chigwa chilichonse achidzaze. Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse; Dziko lokumbikakumbika alisalaze, malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
5 Alors la gloire de Yahweh apparaîtra, et toute chair sans exception la verra; car la bouche de Yahweh a parlé.
Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera, ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona, pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
6 Une voix dit: « Crie! » et on répond: « Que crierai-je? » — « Toute chair est comme l’herbe, et toute sa grâce comme la fleur des champs:
Wina ananena kuti, “Lengeza.” Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani? “Pakuti anthu onse ali ngati udzu ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
7 L’herbe se dessèche, la fleur se flétrit, quand le souffle de Yahweh passe sur elle. Oui, l’homme est comme l’herbe!
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.” Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
8 L’herbe se dessèche, la fleur se flétrit; mais la parole de Dieu subsiste à jamais! »
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota, koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
9 Monte sur une haute montagne, toi qui portes à Sion la bonne nouvelle; élève la voix avec force, toi qui portes à Jérusalem la bonne nouvelle; élève-la, ne crains point; dis aux villes de Juda: « Voici votre Dieu! »
Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni, kwera pa phiri lalitali. Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu, fuwula kwambiri, kweza mawu, usachite mantha; uza mizinda ya ku Yuda kuti, “Mulungu wanu akubwera!”
10 Voici que le Seigneur Yahweh vient avec puissance; son bras exerce la domination; Voici que sa récompense est avec lui, et son salaire est devant lui.
Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu, ndipo dzanja lake likulamulira, taonani akubwera ndi mphotho yake watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
11 Comme un berger, il fera paître son troupeau; il recueillera les agneaux dans ses bras, et les portera dans son sein; il conduira doucement celles qui allaitent.
Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa: Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
12 Qui a mesuré les eaux dans le creux de sa main, estimé l’ étendue des cieux à l’empan, jaugé au boisseau toute la poussière de la terre, pesé les montagnes au crochet, et les collines à la balance?
Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu, kapena kuyeza kulemera kwa mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
13 Qui a dirigé l’esprit de Yahweh, et quel a été son conseiller pour l’instruire?
Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
14 Avec qui a-t-il tenu conseil, pour qu’il l’éclaire, pour qu’il lui enseigne le sentier de la justice, pour qu’il lui enseigne la sagesse, et lui montre le chemin de l’intelligence?
Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya, kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru? Iye anapempha nzeru kwa yani ndi njira ya kumvetsa zinthu?
15 Voici que les nations sont comme la goutte suspendue à un seau, elles sont réputées comme la poussière dans la balance; voici que les îles sont la poudre menue qui s’envole.
Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko. Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo; mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
16 Le Liban ne suffit pas pour le feu, et ses animaux ne suffisent pas pour l’holocauste.
Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe, ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
17 Toutes les nations sont devant lui comme rien; il les compte pour néant et vanité.
Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake; Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu ndi cha chabechabe.
18 À qui donc comparerez-vous Dieu, et quelle image lui préparerez-vous?
Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani? Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
19 Quand l’ouvrier a coulé une idole, l’orfèvre la recouvre d’or, et il lui fond des chaînettes d’argent.
Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide naliveka mkanda wasiliva.
20 Le pauvre, qui ne peut offrir beaucoup, choisit un bois qui ne pourrisse point; et il va chercher un ouvrier habile, pour faire une idole qui ne branle point.
Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere amasankha mtengo umene sudzawola, nafunafuna mʼmisiri waluso woti amupangire fano limene silingasunthike.
21 Ne savez-vous pas? N’avez-vous pas entendu dire? Ne vous a-t-on pas annoncé dès le commencement? N’avez-vous pas appris qui a posé les fondements de la terre?
Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe? Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
22 Il trône par dessus la voûte de la terre, — et ses habitants sont comme des sauterelles; — il étend les cieux comme un voile, et les déploie comme une tente pour y habiter;
Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi, Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala. Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga, nayikunga ngati tenti yokhalamo.
23 Il livre au néant les puissants, et réduit à rien les juges de la terre:
Amatsitsa pansi mafumu amphamvu nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
24 à peine sont-ils plantés, à peine sont-ils semés, à peine leur tronc a-t-il pris racine en terre, il souffle sur eux, et ils sèchent, et l’ouragan les emporte comme le chaume.
Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene kapena kufesedwa chapompano, ndi kungoyamba kuzika mizu kumene ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.
25 À qui donc me comparerez-vous, que je lui sois pareil, dit le Saint?
Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani? Kapena kodi alipo wofanana nane?”
26 Levez les yeux en haut et regardez: qui a créé ces choses? Celui qui fait marcher en ordre leur armée, et qui les appelle toutes par leur nom; et, à cause de la grandeur de sa puissance et de l’énergie de sa force, pas une ne fait défaut.
Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani. Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi? Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo, nayitana iliyonse ndi dzina lake. Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri, palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.
27 Pourquoi dis-tu, ô Jacob, et parles-tu ainsi, ô Israël: « Ma voie est cachée à Yahweh, et mon droit passe inaperçu devant mon Dieu? »
Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti, “Yehova sakudziwa mavuto anga, Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
28 Ne sais-tu pas, n’as-tu pas entendu? Yahweh est un Dieu éternel, qui a créé les extrémités de la terre, qui ne se fatigue ni ne se lasse, et dont la sagesse est insondable.
Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Yehova ndiye Mulungu wamuyaya, ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi. Iye sadzatopa kapena kufowoka ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
29 Il donne de la force à celui qui est fatigué et redouble la vigueur de celui qui est défaillant.
Iye amalimbitsa ofowoka ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
30 Les jeunes gens se fatiguent et se lassent, et les jeunes gens chancellent,
Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka, ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
31 Mais ceux qui se confient en Yahweh renouvellent leurs forces; ils élèveront leur vol comme les aigles; ils courront et ne se fatigueront point; ils marcheront et ne se lasseront point.
koma iwo amene amakhulupirira Yehova adzalandira mphamvu zatsopano. Adzawuluka ngati chiwombankhanga; adzathamanga koma sadzalefuka, adzayenda koma sadzatopa konse.

< Isaïe 40 >