< Psalmaro 103 >
1 De David. Benu, ho mia animo, la Eternulon, Kaj mia tuta internaĵo Lian sanktan nomon.
Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
2 Benu, ho mia animo, la Eternulon, Kaj ne forgesu ĉiujn Liajn bonfarojn.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
3 Li pardonas ĉiujn viajn pekojn, Li sanigas ĉiujn viajn malsanojn;
Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
4 Li savas de la tombo vian vivon, Li kronas vin per boneco kaj favorkoreco;
amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
5 Li satigas per bonaĵoj vian maljunan aĝon, Ke via juneco renoviĝas kiel ĉe aglo.
amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
6 La Eternulo faras justecon kaj juĝon al ĉiuj prematoj.
Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
7 Li sciigis Siajn vojojn al Moseo, Siajn farojn al la Izraelidoj.
Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
8 Favorkora kaj kompatema estas la Eternulo, Longetolerema kaj tre bona.
Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
9 Ne eterne Li indignas, Kaj ne por ĉiam Li koleras.
Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
10 Ne laŭ niaj pekoj Li agis kun ni, Kaj ne laŭ niaj krimoj Li redonis al ni.
satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
11 Ĉar kiel alte estas la ĉielo super la tero, Tiel granda estas Lia boneco por tiuj, kiuj Lin timas.
Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
12 Kiel malproksime estas la oriento de la okcidento, Tiel Li malproksimigis de ni niajn pekojn.
monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
13 Kiel patro korfavoras filojn, Tiel la Eternulo korfavoras tiujn, kiuj Lin timas.
Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
14 Ĉar Li scias nian esencon; Li memoras, ke ni estas polvo.
pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
15 La tagoj de homo estas kiel herbo; Kiel floro de kampo, tiel li floras.
Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
16 Pasas super ĝi vento, kaj ĝi jam ne ekzistas; Kaj ĝia loko ĝin jam ne rekonas.
koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
17 Sed la boneco de la Eternulo daŭras eterne al tiuj, kiuj Lin timas, Kaj Lia bonfaremeco iras ĝis la pranepoj,
Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
18 Kiuj observas Lian interligon Kaj memoras Liajn ordonojn por ilin plenumi.
iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
19 La Eternulo starigis en la ĉielo Sian tronon; Kaj Lia reĝeco regas ĉion.
Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
20 Benu la Eternulon Liaj anĝeloj, potencaj per sia forto, Kiuj plenumas Lian vorton, Por ke oni obeu la voĉon de Lia vorto.
Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
21 Benu la Eternulon ĉiuj Liaj ĉirkaŭantoj, Liaj servantoj, kiuj plenumas Lian volon.
Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
22 Benu la Eternulon ĉiuj Liaj kreitaĵoj, En ĉiuj lokoj de Lia regado. Benu, ho mia animo, la Eternulon.
Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.