< Psalms 85 >

1 Of the sones of Chore. Lord, thou hast blessid thi lond; thou hast turned awei the caitifte of Jacob.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
2 Thou hast foryoue the wickidnesse of thi puple; thou hast hilid alle the synnes of hem.
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
3 Thou hast aswagid al thin ire; thou hast turned awei fro the ire of thin indignacioun.
Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
4 God, oure helthe, conuerte thou vs; and turne awei thin ire fro vs.
Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
5 Whether thou schalt be wrooth to vs withouten ende; ether schalt thou holde forth thin ire fro generacioun in to generacioun?
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
6 God, thou conuertid schalt quykene vs; and thi puple schal be glad in thee.
Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
7 Lord, schewe thi merci to vs; and yyue thin helthe to vs.
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
8 I schal here what the Lord God schal speke in me; for he schal speke pees on his puple. And on hise hooli men; and on hem that ben turned to herte.
Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
9 Netheles his helthe is niy men dredynge him; that glorie dwelle in oure lond.
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
10 Merci and treuthe metten hem silf; riytwisnesse and pees weren kissid.
Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 Treuthe cam forth of erthe; and riytfulnesse bihelde fro heuene.
Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 For the Lord schal yyue benignyte; and oure erthe schal yyue his fruyt.
Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 Riytfulnesse schal go bifore him; and schal sette hise steppis in the weie.
Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.

< Psalms 85 >