< Psalms 3 >

1 `The salm of Dauid, whanne he fledde fro the face of Absolon, his sone. Lord, whi ben thei multiplied that disturblen me?
Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu. Inu Yehova, achulukadi adani anga! Achulukadi amene andiwukira!
2 many men rysen ayens me. Many men seien of my soule, Noon helthe is to hym in his God.
Ambiri akunena za ine kuti, “Mulungu sadzamupulumutsa.” (Sela)
3 But thou, Lord, art myn vptakere; my glorye, and enhaunsyng myn heed.
Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza, Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
4 With my vois Y criede to the Lord; and he herde me fro his hooli hil.
Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera. (Sela)
5 I slepte, and `was quenchid, and Y roos vp; for the Lord resseyuede me.
Ine ndimagona ndi kupeza tulo; ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
6 I schal not drede thousyndis of puple cumpassynge me; Lord, rise thou vp; my God, make thou me saaf.
Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
7 For thou hast smyte alle men beynge aduersaries to me with out cause; thou hast al to-broke the teeth of synneris.
Dzukani, Inu Yehova! Pulumutseni, Inu Mulungu wanga. Akantheni adani anga onse pa msagwada; gululani mano a anthu oyipa.
8 Helthe is of the Lord; and thi blessyng, Lord, is on thi puple.
Chipulumutso chimachokera kwa Yehova. Madalitso akhale pa anthu anu. (Sela)

< Psalms 3 >