< Ezekiel 23 >
1 And the word of the Lord was maad to me,
Yehova anandiyankhula nati:
2 and he seide, Thou, sone of man, twei wymmen weren the douytris of o modir, and diden fornycacioun in Egipt;
“Iwe mwana wa munthu, panali atsikana awiri ana a mayi mmodzi.
3 in her yonge wexynge age thei diden fornicacioun; there the brestis of hem weren maad low, and the tetis of the tyme of mariage of hem weren brokun.
Iwo ankachita za chiwerewere ku Igupto. Za chiwerewerezo anayamba ali achichepere. Kumeneko anthu ankangowasisita pa chifuwa ndi kuwagwiragwira mawere awo aja.
4 Forsothe the names of hem ben, Oolla, the more sistir, and Ooliba the lesse sistir of hir. And Y hadde hem, and thei childiden sones and douytris; certis the names of hem ben Samarie Oolla, and Jerusalem Ooliba.
Wamkulu dzina lake anali Ohola, ndipo mngʼono wakeyo anali Oholiba. Ine ndinawakwatira ndipo anabereka ana aamuna ndi ana aakazi. Ohola ndiye Samariya, ndipo Yerusalemu ndiye Oholiba.
5 Therfor Oolla dide fornicacioun on me, and was wood on hir louyeris, on Assiriens neiyinge,
“Ohola anachita zachiwerewere ngakhale anali mkazi wanga; ndipo iye anakangamira abwenzi ake a ku Asiriya.
6 clothid with iacinct, princes, and magistratis, yonge men of coueytise, alle kniytis, and stieris of horsis.
Amenewo anali asilikali ovala zibakuwa zamlangali, abwanamkubwa ndiponso atsogoleri a nkhondo. Onsewo anali anyamata osiririka ndipo ankakwera pa akavalo.
7 And sche yaf hir fornicaciouns on hem, on alle the chosun sones of Assiriens; and in alle on whiche sche was wood, sche was defoulid in the vnclennessis of hem.
Ohola anachita zachiwerewere ndi onsewa, anthu otchuka a ku Asiriya. Iye anadziyipitsa ndi mafano a munthu aliyense amene anagona naye.
8 Ferthermore and sche lefte not hir fornicaciouns, whiche sche hadde in Egipt; for whi and thei slepten with hir in the yongthe of hir, and thei braken the tetis of the tyme of mariage of hir, and thei scheden out her fornicacioun on hir.
Iye sanaleke za chiwerewere zimene anaziphunzira ku Igupto. Paja akanali mtsikana anyamata ankagona naye. Iwo ankamusisita mawere akanali anthete nachita naye zachiwerewere.
9 Therfor Y yaf hir in to the hondis of hir louyeris, in to the hondis of the sones of Assur, on whos letcherie sche was wood.
“Nʼchifukwa chake Ine ndinamupereka kwa achikondi ake, Asiriya, amene iye ankawalakalaka.
10 Thei diskyueriden the schenschipe of hir; thei token awei the sones and the douytris of hir, and killiden hir with swerd; and the wymmen weren maad famouse, that is, sclaundrid, and thei diden domes in hir.
Iwowa anamuvula, namulanda ana ake aamuna ndi aakazi ndipo anamupha ndi lupanga. Ndipo atalangidwa choncho, iye anasanduka chinthu chonyozeka pakati pa akazi.
11 And whanne hir sistir Ooliba hadde seyn this, sche was wood in letcherie more than that sistre, and yaf vnschamefastli hir fornicacioun on the fornicacioun of hir sistre,
“Mphwake Oholiba anaona zimenezi natengerako. Koma iye anachita zachiwerewere kuposa mkulu wake.
12 to the sones of Assiriens, to duykis and magistratis comynge to hir, that weren clothid with dyuerse cloth, to knyytis that weren borun on horsis, and to yonge men with noble schap, to alle men.
Iyenso anakangamira Asiriya, abwanamkubwa, olamulira asilikali, ankhondo ovala zovala zonse za nkhondo ndi okwera pa akavalo. Onsewa anali anyamata osiririka.
13 And Y siy that o weie of both sistris was defoulid,
Ndinaona kuti iyenso anadziyipitsa; ndipo onse awiriwo anatsata njira imodzi.
14 and sche encreesside hir fornycaciouns. And whanne sche hadde seyn men peyntid in the wal, the ymagis of Caldeis expressid with colouris,
“Koma Oholiba uja anachita chigololo kopitirira mkulu wake. Iye anaona zithunzi za amuna pa khoma, zithunzi za Ababuloni zolembedwa ndi inki yofiira,
15 and gird on the reynes with kniytis girdlis, and cappis peyntid in the heedis of hem, the foormes of alle duykis, the licnesse of the sones of Babiloyne, and of the lond of Caldeis, in which thei weren borun;
atamanga malamba mʼchiwuno mwawo ndi kuvala nduwira pa mitu yawo. Onse amaoneka ngati atsogoleri a magaleta a Ababuloni, mbadwa za ku Kaldeya.
16 sche was wood on hem bi coueitise of hir iyen, and sche sente messangeris to hem in to Caldee.
Oholiba atangowaona, anawalakalaka ndipo anatuma amithenga ku Kaldeya kukawayitana.
17 And whanne the sones of Babiloyne weren comun to hir, to the bed of tetis, thei defouliden hir in her letcheries of virgyns; and sche was defoulid of hem, and the soule of hir was fillid of hem.
Ndipo Ababuloni anabwera nʼkudzagona naye. Choncho mwa chilakolako chawo anamuyipitsa. Koma atamuyipitsa choncho, iye ananyansidwa nawo.
18 Also sche made nakid hir fornicaciouns, and diskyuered hir schenschipe; and my soule yede awei fro hir, as my soule hadde go awei fro hir sistir.
Iye atachita chiwerewere chake poyera ndi kuonetsa umaliseche wake, Ine ndinamuchokera monyansidwa monga mmene ndinachitira ndi mʼbale wake.
19 For sche multiplied hir fornicaciouns, and hadde mynde on the daies of hir yongthe, in whiche sche dide fornicacioun in the lond of Egipt.
Koma anachitabe zachiwerewere osalekeza. Ankakumbukira masiku a ubwana wake pamene ankachita za chiwerewere mʼdziko la Igupto.
20 And sche was wood in letcherie on the liggyng bi of hem, whos fleischis ben as the fleischis of assis, and as the membris of horsis ben the membris of hem.
Kumeneko iye ankalakalaka zibwenzi zake, amene ziwalo zawo zinali ngati za abulu ndipo kutentha kwawo kunali ngati kwa akavalo.
21 And thou visitidist the grete trespas of thi yongthe, whanne thi brestis weren maad low in Egipt, and the tetis of the tyme of thi mariage weren brokun.
Motero, iwe Oholiba unafuna kuchitanso zadama monga unkachitira ku Igupto pamene unali mtsikana. Nthawi imene ija ankakusisita pa chifuwa ndi kugwiragwira mawere ako osagwa aja.
22 Therfor, thou Ooliba, the Lord God seith these thingis, Lo! Y schal reise alle thi louyeris ayens thee, of whiche thi soule was fillid, and Y schal gadere hem ayens thee in cumpas;
“Tsono iwe Oholiba, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakudzutsira zibwenzi zako zimene unkanyansidwa nazo zija kuti zilimbane nawe. Ndidzaziyitana kuti zibwere kuchokera mbali zonse.
23 the sones of Babiloyne, and alle Caldeis, noble and miyti men, and princes, alle the sones of Assiriens, and yonge men of noble foorme, duykis, and magistratis, alle princes of princes, and named stieris of horsis.
Ndidzayitana anthu a ku Babuloni ndi Akaldeya onse, anthu a ku Pekodi, Sowa ndi Kowa pamodzi ndi Asiriya onse. Onsewa ndi amuna osiririka, abwanamkubwa, atsogoleri a ankhondo, oyenda pa magaleta, anthu a maudindo akuluakulu. Onsewa ndi okwera akavalo.
24 And thei araied with chare and wheel schulen come on thee, the multitude of puplis schulen be armed with haburioun, and scheeld, and basynet, ayens thee on ech side; and Y schal yyue doom bifor hem, and thei schulen deme thee bi her domes.
Iwo adzabwera kudzalimbana nawe ndi zida za nkhondo, magaleta ndi ngolo, pamodzi ndi anthu ambiri. Adzakuzinga mbali zonse atavala zishango zankhondo ndi zipewa zankhondo. Ndidzakupereka kwa iwo kuti akulange ndipo adzakulanga monga momwe adzafunire.
25 And Y schal sette my feruour in thee, which thei schulen vse with thee in woodnesse; thei schulen kitte awei thi nose and thin eeris, and thei schulen sle with swerd tho thingis that weren left; thei schulen take thi sones and thi douytris, and thi laste thing schal be deuourid bi fier.
Ndidzaonetsa mkwiyo wanga pa iwe ndipo iwo adzakulanga iwe mwankhanza. Adzadula mphuno zanu ndi makutu anu, ndipo amene adzatsalira mwa iwe adzaphedwa ndi lupanga. Iwo adzakulanda ana ako aamuna ndi aakazi ndipo amene adzatsalira adzaphedwa ndi moto.
26 And thei schulen make thee nakid of thi clothis, and thei schulen take awei the vessels of thi glorie.
Adzakuvulaninso zovala zanu ndikukulandani zodzikongoletsera zanu zamtengowapatali.
27 And Y schal make thi greet trespasse to reste fro thee, and thi fornicacioun fro the lond of Egipt; and thou schalt not reise thin iyen to hem, and thou schalt no more haue mynde on Egipt.
Motero ndidzathetsa zonyansa zako ndi zachigololo zomwe unaziyamba ku Igupto. Choncho sudzalakalaka za ku Igupto kapena kuzikumbukiranso.
28 For the Lord God seith these thingis, Lo! Y schal yyue thee in to the hondis of hem whiche thou hatist, `in to the hondis of hem of whiche thi soule was fillid,
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikukupereka mʼmanja mwa amene amadana nawe, kwa iwo amene unawafulatira moyipidwa nawo.
29 and thei schulen do with thee in hatrede. And thei schulen take awei alle thi trauels, and thei schulen leeue thee nakid, and ful of schenschipe; and the schenschipe of thi fornicaciouns schal be schewid. Thi greet
Adzachita nawe mwachidani. Adzakulanda zonse zimene unagwirira ntchito. Adzakusiya wamaliseche ndiponso wausiwa. Kuyipa kwa makhalidwe ako achiwerewere kudzakhala pammbalambanda. Zonyansa zako ndi chiwerewere chako,
30 trespas and thi fornycaciouns han do these thingis to thee; for thou didist fornicacioun aftir hethene men, among whiche thou were defoulid in the idols of hem.
zabweretsa izi pa iwe chifukwa unachita zonyansa ndi anthu a mitundu ndi kudziyipitsa ndi mafano awo.
31 Thou yedist in the weie of thi sister, and Y schal yyue the cuppe of hir in thin hond.
Unatsata zochita za mkulu wako; choncho Ine ndidzayika chikho cha chilango chake mʼdzanja lako.
32 The Lord God seith these thingis, Thou schalt drinke the cuppe of thi sistir, the depthe, and the broodnesse; thou that art most able to take, schalt be in to scornyng, and in to mouwyng.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Udzamwera chikho cha mkulu wako, chikho chachikulu ndi chakuya; anthu adzakuseka ndi kukunyoza, pakuti chikhocho ndi chodzaza kwambiri.
33 Thou schalt be fillid with drunkenesse and sorewe, with the cuppe of mourenyng and of heuynesse, with the cuppe of thi sister Samarie.
Udzaledzera ndipo mtima wako udzadzaza ndi chisoni. Chimenechi ndi chikho chachiwonongeko ndi chipasupasu, chikho cha mkulu wako Samariya.
34 And thou schalt drynke it, and thou schalt drinke of til to the drastis, and thou schalt deuoure the relifs therof, and thou schalt to-reende thi brestis, for Y the Lord spak, seith the Lord God.
Udzamwa chikhocho mpaka kugugudiza. Tsono udzaphwanyaphwanya chikhocho ndipo udzangʼamba mawere ako ndi zigoba zake. Ine ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
35 Therfor the Lord God seith these thingis, For thou hast foryete me, and hast cast forth me bihynde thi bodi, bere thou also thi greet trespas and thi fornicaciouns.
“Chifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza wandiyiwala Ine ndi kundifulatira, chomwecho uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi chiwerewere chako.”
36 And the Lord God seide to me, and spak, Sone of man, whether thou demest Ooliba and Oolla, and tellist to hem the grete trespassis of hem?
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? Tsono uwayimbe mlandu chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
37 For thei diden auowtrie, and blood was in the hondis of hem, and thei diden fornicacioun with her idols; ferthermore and thei offriden to tho the sones whiche thei gendriden to me, for to be deuourid.
Iwo achita chigololo ndipo anapha anthu. Anachita chigololo popembedza mafano awo. Ngakhale ana amene anandiberekera Ine anawapereka kwa mafanowo ngati chakudya chawo.
38 But also thei diden this to me, thei defouleden my seyntuarie in that dai, and maden vnhooli my sabatis.
Anachitanso izi: Iwo anayipitsa malo anga opatulika ndi kudetsa masabata anga.
39 And whanne thei sacrifisiden her sones to her idols, and entriden in to my seyntuarie in that dai, that thei schulden defoule it, thei diden also these thingis in the myddis of myn hous.
Atapereka ana awo kwa mafano, tsiku lomwelo anakalowanso mʼNyumba yanga yopatulika ndi kuyipitsamo. Izi ndi zimene anachita mʼNyumba mwanga.
40 Thei senten to men comyng fro fer, to whiche thei hadden sent messangeris. Therfor lo! thei camen, to whiche thou waischidist thee, and anoyntidist thin iyen with oynement of wymmen, and thou were ourned with wymmens atier.
“Iwo anatuma amithenga kukayitana amuna a ku mayiko akutali. Anthuwo atabwera, abale awiri aja anasambasamba, kudzola utoto wodzikometsera kumaso, kenaka ndi kuvala zovala zamakaka.
41 Thou satist in a ful fair bed, and a boord was ourned bifor thee; thou settidist myn encense and myn oynement on it.
Anakhala pa bedi lokongola ndipo patsogolo pawo panali tebulo pamene munayikapo lubani ndi mafuta. Zonse zowapatsa Ine.
42 And a vois of multitude makynge ful out ioye was ther ynne; and in men that weren brouyt of the multitude of men, and camen fro desert, thei settiden bies in the hondis of hem, and faire corouns on the heedis of hem.
“Mfuwu wa chigulu cha anthu unamveka. Anthu oledzera ochokera ku chipululu anabwera pamodzi ndi anthu wamba ndipo anaveka akaziwo zibangiri kumanja ndi zipewa zaufumu zokongola ku mutu.
43 And Y seide to hir, that was defoulid in auoutries, Now also this schal do fornycacioun in hir fornicacioun.
Ndipo ine ndinati za mkazi wotheratu ndi chigololoyo, ‘Tsono asiyeni kuti achite naye monga wachiwerewere, pakuti ichi ndi chimene iye ali basi.’
44 And thei entriden to hir; as to a womman, an hoore, so thei entriden to Oolla and to Ooliba, cursid wymmen.
Tsono anapita kwa iwo monga mmene anthu amapitira kwa mkazi wadama. Momwemo anapita kwa Ohola ndi kwa Oholiba kukachita nawo zadama.
45 Therfor these men ben iust, these schulen deme thilke wymmen bi the doom of auoutressis, and bi the doom of hem that scheden out blood; for thei ben auoutressis, and blood is in the hondis of hem, and thei diden fornicacioun with her idols.
Koma anthu olungama adzawazenga anthuwa mlandu wa chigololo ndi wa kupha anthu. Ndi iwodi anthu achigololo ndiponso mʼmanja mwawo muli magazi.
46 For the Lord God seith these thingis, Bringe thou multitudis to hem, and yyue thou hem in to noise, and in to raueyn;
“Ambuye Yehova akuti: Itanitsani chigulu cha anthu kuti chidzawalange ndi kulanda chuma chawo.
47 and be thei stoonyd with the stoonys of puplis, and be thei stikid togidere with the swerdis of hem. Thei schulen sle the sones and the douytris of hem, and thei schulen brenne with fier the housis of hem.
Anthuwo adzawaponye miyala akazi awiriwo ndi kuwatema ndi malupanga awo. Ana awo aamuna ndi aakazi adzawaphe ndi kutentha nyumba zawo.
48 And Y schal do awei greet trespas fro the lond; and alle wymmen schulen lerne, that thei do not aftir the greet trespas of hem.
“Motero Ine ndidzathetsa zachigololo mʼdzikomo, ndipo akazi onse adzatengapo phunziro kuti asadzachite zachigololo monga za iwowo.
49 And thei schulen yyue youre grete trespas on you; and ye schulen bere the synnes of youre idols, and ye schulen wite, that Y am the Lord God.
Ndidzawalanga chifukwa cha ntchito zawo za dama ndipo adzazunzika chifukwa cha tchimo lawo lopembedza mafano. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.”