< 1 Chronicles 10 >
1 Forsothe Filisteis fouyten ayens Israel, and the sones of Israel fledden Palestyns, and felden doun woundid in the hil of Gelboe.
Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa.
2 And whanne Filisteis hadde neiyed pursuynge Saul and hise sones, thei killiden Jonathan, and Abynadab, and Melchisue, the sones of Saul.
Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa.
3 And the batel was agreggid ayens Saul; and men archeris foundun hym, and woundiden hym with dartis.
Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza.
4 And Saul seide to his squiere, Drawe out thi swerd, and sle me, leste these vncircumcidid men come, and scorne me. Sothli his squyer was aferd bi drede, and nolde do this; therfor Saul took a swerd, and felde on it.
Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe, kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere ndi kudzandizunza ine.” Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo.
5 And whanne his squyer hadde seyn this, that is, that Saul was deed, he felde also on his swerd, and was deed.
Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa.
6 Therfor Saul perischide, and hise thre sones, and al his hows felde doun togidere.
Motero Sauli ndi ana ake atatu anafa, pamodzi ndi banja lake lonse anafera limodzi.
7 And whanne the men of Israel, that dwelliden in feeldi places, hadden seyn this, thei fledden; and whanne Saul and hise sones weren deed, thei forsoken her citees, and weren scaterid hidur and thidur; and Filisteis camen, and dwelliden in tho.
Pamene Aisraeli onse amene anali mʼchigwa anaona kuti gulu lankhondo lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
8 Therfor in the tother day Filisteis drowen awei the spuylis of slayn men, and founden Saul and hise sones liggynge in the hil of Gelboe.
Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa, anapeza Sauli ndi ana ake atafa pa phiri la Gilibowa.
9 And whanne thei hadden spuylid hym, and hadden gird of the heed, and hadden maad hym nakid of armeris, thei senten in to her lond, that it schulde be borun aboute, and schulde be schewid in the templis of idols and to puplis;
Iwo anamuvula zovala zake, natenga mutu wake ndi zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo.
10 forsothe thei halewiden his armeris in the temple of her god, and thei settiden the heed in the temple of Dagon.
Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba zopembedzera milungu yawo ndipo anapachika mutu wake mʼnyumba ya Dagoni.
11 Whanne men of Jabes of Galad hadden herd this, that is, alle thingis whiche the Filisteis diden on Saul,
Pamene anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli,
12 alle stronge men risiden togidere, and took the deed bodies of Saul and of hise sones, and brouyten tho in to Jabes; and thei birieden the boonus of hem vndur an ook, that was in Jabes; and thei fastiden seuene daies.
anthu awo onse olimba mtima anapita kukatenga mitembo ya Sauli ndi ana ake ndipo anabwera nayo ku Yabesi. Anakwirira mafupa awo pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.
13 Therfor Saul was deed for hise wickidnessis, for he brak the comaundement of the Lord, whiche he comaundide, and kepte not it, but ferthirmore also he took counsel at a womman hauynge a feend spekynge in the wombe, and he hopide not in the Lord;
Sauli anafa chifukwa anali wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Iye sanasunge mawu a Yehova, pakuti anakafunsira nzeru kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa,
14 for which thing both the Lord killide hym, and translatide his rewme to Dauid, sone of Ysay.
sanafunsire nzeruzo kwa Yehova. Choncho Yehova anamupha ndi kupereka ufumu kwa Davide mwana wa Yese.