< Job 30 >
1 But now [they that are] younger than I, have me in derision, whose fathers I would have disdained to set with the dogs of my flock.
“Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
2 Yes, to what [might] the strength of their hands [profit] me, in whom old age had perished?
Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
3 For want and famine [they were] solitary; fleeing into the wilderness in former time desolate and waste.
Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
4 Who cut up mallows by the bushes, and juniper roots [for] their food.
Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
5 They were driven forth from among [men], (they cried after them, as [after] a thief; )
Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
6 To dwell in the clefts of the valleys, [in] caves of the earth, and [in] the rocks.
Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
7 Among the bushes they brayed; under the nettles they were collected.
Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
8 [They were] children of fools, yes, children of base men: they were viler than the earth.
Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
9 And now I am their song, yes, I am their by-word.
“Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
10 They abhor me, they flee far from me, and spare not to spit in my face.
Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
11 Because he hath loosed my cord, and afflicted me, they have also let loose the bridle before me.
Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
12 Upon [my] right [hand] rise the youth; they push away my feet, and they raise up against me the ways of their destruction.
Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
13 They mar my path, they set forward my calamity, they have no helper.
Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
14 They came [upon me] as a wide breaking in [of waters]: in the desolation they rolled themselves [upon me].
Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
15 Terrors are turned upon me: they pursue my soul as the wind: and my welfare passeth away as a cloud.
Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
16 And now my soul is poured out upon me; the days of affliction have taken hold upon me.
“Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
17 My bones are pierced in me in the night season: and my sinews take no rest.
Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
18 By the great force [of my disease] is my garment changed: it bindeth me about as the collar of my coat.
Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
19 He hath cast me into the mire, and I have become like dust and ashes.
Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
20 I cry to thee, and thou dost not hear me: I stand up, and thou regardest me [not].
“Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
21 Thou hast become cruel to me: with thy strong hand thou opposest thyself against me.
Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
22 Thou liftest me up to the wind; thou causest me to ride [upon it], and dissolvest my substance.
Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
23 For I know [that] thou wilt bring me [to] death, and [to] the house appointed for all living.
Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
24 Yet he will not stretch out [his] hand to the grave, though they cry in his destruction.
“Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
25 Did not I weep for him that was in trouble? was [not] my soul grieved for the poor?
Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
26 When I looked for good, then evil came: and when I waited for light, there came darkness.
Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
27 My bowels boiled, and rested not: the days of affliction came upon me.
Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
28 I went mourning without the sun: I stood up, [and] I cried in the congregation.
Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
29 I am a brother to dragons, and a companion to owls.
Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
30 My skin is black upon me, and my bones are burned with heat.
Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
31 My harp also is [turned] to mourning, and my organ into the voice of them that weep.
Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.