< Leviticus 5 >
1 [Yahweh also said to tell the people], “If [a judge] orders any of you to tell [in court] something that you have seen or something that you heard someone say, if you refuse to say what you know is true, you must (pay a penalty/be punished) [MTY] for refusing to tell what you know.
“‘Ngati munthu anayitanidwa ku bwalo kuti akachitire umboni pa zimene anaziona kapena kuzimva koma iye nʼkukana kuchitira umboni, munthu ameneyo wachimwa ndipo ayenera kulangidwa.
2 If you accidentally touch something which God considers impure [DOU], such as the carcass of a wild animal or the carcass of a bull or cow, or of an animal that scurries across the ground, you must (pay a penalty/be punished).
“‘Munthu akakhudza chinthu chilichonse chodetsedwa, monga nyama yakufa ya mʼthengo, kapena chiweto chakufa kapenanso chokwawa chakufa, ngakhale iyeyo wachikhudza mosadziwa, wasanduka wodetsedwa ndipo wachimwa.
3 If you touch any human feces, even if you do not intend to do that, when you realize what you have done, you must (pay a penalty/be punished).
“‘Munthu akakhudza choyipitsa munthu cha mtundu uliwonse, ndipo pochikhudzapo ndi kuyipitsidwa nacho mosadziwa, munthuyo adzakhala wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
4 If you carelessly make a solemn promise [to do something] that is good or that is bad, when you realize what you have done, you must (pay a penalty/be punished).
“‘Munthu akalumbira mofulumira kapena mosasamala kuti adzachita chinthu, choyipa kapena chabwino, ngakhale kuti wachita izi mosadziwa kuti nʼkulakwa, pamene wazindira kulakwa kwake, iye adzakhalabe wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
5 If you are guilty of committing any of those sins, you must confess what you have done.
“‘Pamene munthu wazindikira kuti wachimwa motere, awulule tchimo limene wachitalo.
6 And for a penalty you must bring to Yahweh a female lamb or female goat, to be an offering for the sin that you have committed, and the priest will sacrifice it, and then you will no longer be guilty for your sin.
Pambuyo pake, munthuyo abwere kwa Yehova ndi mwana wankhosa wamkazi kapena mbuzi kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo ndipo wansembe achite mwambo wopepesera tchimo lomwe wachitalo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo.
7 If you [are poor and] cannot afford to bring a lamb, you must bring to Yahweh two doves or two young pigeons. One will be an offering for your sin and one will be an offering that will be completely burned [on the altar].
“‘Ngati munthuyo alibe mwana wankhosa, abweretse njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri kwa Yehova ngati chopereka chopepesera tchimo lake. Imodzi ikhale nsembe yopepesera tchimo, ndipo inayo ikhale nsembe yopsereza.
8 You must bring them to the priest. First he will offer one of them to be an offering for your sin. He will wring/twist its neck [to kill it], but he must not pull off its head completely.
Tsono abwere nazo kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayambe wapereka mbalame imodzi ngati yopepesera tchimo. Apotole khosi koma osayidula mutu,
9 Then he must sprinkle some of the blood against the side of the altar. The remaining blood must be drained out at the base of the altar. That will be an offering for your sin.
kenaka awaze magazi a chopereka chopepesera tchimocho mʼmbali mwa guwa. Magazi ena onse awathire pa tsinde la guwa. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
10 The priest will then do what I have commanded and offer the other bird to be completely burned [on the altar]. Then you will no longer be guilty for the sin you have committed, and Yahweh will forgive you.
Pambuyo pake wansembe apereke mbalame inayo kuti ikhale chopereka chopsereza potsata mwambo wake. Wansembe atatha kupereka nsembe yopepesera tchimo limene munthu uja wachita, wochimwayo adzakhululukidwa.
11 However, if you [are very poor and] cannot afford two doves or two young pigeons, you must bring to be an offering for your sin (2 pounds/1 kg.) of fine flour. You must not put olive oil or incense on it, because it is an offering for sin.
“‘Koma ngati munthuyo alibe njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri, abweretse ufa wosalala wokwanira kilogalamu imodzi kuti ukhale chopereka chopepesera tchimo limene wachita. Asathiremo mafuta kapena lubani chifukwa ndi chopereka chopepesera tchimo.
12 You must take it to the priest. He will take a handful of it, to symbolize that the whole offering truly belongs to Yahweh, and burn it on the altar, on top of the other offerings.
Abweretse ufawo kwa wansembe ndipo wansembeyo atapeko dzanja limodzi kuti ukhale ufa wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa pamodzi ndi chopereka chopsereza kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
13 And by doing that, the priest will enable you to no longer be guilty for any of the sins that you have committed, and you will be forgiven. The part of the offering that is not burned will belong to the priest, like was true for the offerings made from grain.”
Umu ndi mmene wansembe adzachitire mwambo wopepesera machimo ena aliwonse amene munthu wachita, ndipo munthuyo adzakhululukidwa. Zopereka zonse zotsala zidzakhala za wansembeyo monga momwe amachitira ndi chopereka chachakudya.’”
14 Yahweh also said to Moses/me,
Yehova anawuza Mose kuti,
15 “When you sin, without intending to, by not giving to Yahweh the things that you are required to give to him, you must pay a penalty by bringing to Yahweh a ram that has no defects. You must determine how much silver it is worth, by using the official standard in the temple. It will be an offering to cause you to no longer be guilty.
“Munthu akachita zinthu mosakhulupirika, nachimwa mosadziwa posapereka zinthu zopatulika zofunika kwa Yehova, munthuyo apereke kwa Yehova nsembe yopepesera machimo ake. Nsembeyo ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale wokwana masekeli oyenera a siliva pakawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu. Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula.
16 But you must also make restitution for what you failed to give to Yahweh, adding one-fifth of its value. You must give that to the priest. He will offer the ram as a sacrifice for the sin that you have committed, and cause you to no longer be guilty; and you will be forgiven.
Munthuyo ayenera kubweza zinthu zopatulika zimene sanaperekezo. Awonjezepo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse ndi kuzipereka zonsezo kwa wansembe amene adzachita mwambo wopepesera machimo a munthuyo, popereka nkhosa yayimuna ija ngati nsembe yopepesera ndipo wochimwayo adzakhululukidwa.
17 If you sin by doing something that is forbidden by any of Yahweh’s commands, even if you do not know that you have disobeyed one of my commands, you are guilty and must pay a penalty [to me].
“Ngati munthu wachimwa mosadziwa pochita chilichonse chimene Yehova salola, munthuyo ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kulangidwa.
18 [When you realize what you have done], you must bring a ram to the Supreme Priest to be an offering in order that you will no longer be guilty. You must bring one that has no defects. He will offer the ram to be a sacrifice to me, and as a result you will no longer be guilty for the sin that you have committed, and you will be forgiven.
Abwere kwa wansembe ndi chopereka chopepesera kupalamula kwake. Chopereka chikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale woyenera nsembe yopepesera kupalamula kumene anachimwa mosadziwako, ndipo munthuyo adzakhululukidwa.
19 It is an offering to cause you to no longer be guilty for sinning against me.”
Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula popeza munthuyo wapezeka wolakwa pamaso pa Yehova.”