< Job 38 >

1 Then Yahweh spoke to Job from inside a great windstorm. He said to him,
Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2 “(Who are you to question what I plan to do?/You have no right/authority to question what I plan to do.) [RHQ] You are speaking ignorantly!
“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
3 I want to ask you [some] questions, so, just like men prepare themselves for a difficult task [MET], prepare to answer my questions.
Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
4 (“Where were you/Were you there with me) [long ago] when I (laid the foundations of/created) the earth? Since you know so much, tell me [where you were at that time].
“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
5 Do you know how I decided how large the earth would be? Do you know who stretched a measuring tape around the earth? Surely [since you think that you know so much, ] you should know that!
Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6 What supports the pillars on which the earth rests? When the stars [that shine early] in the morning sang together, and someone put in place the stone that causes the earth to stay in its place, and all the angels shouted joyfully [when they saw that happening], who laid that cornerstone? [Did you?]
Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7
pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8 “When the seas poured forth from inside the earth, who prevented the water from flooding over the land?
“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9 It was I, [not you, ] who caused clouds to come over the seas and caused it to become very dark [under those clouds].
pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10 I set limits for the seas, and I put barriers [so that the water would not come over the land].
pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11 [I pointed to the shore] and said to the water, ‘I permit you to come up to here, but I do not permit you to come any farther. Your powerful waves must stop there!’
Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12 “Job, have you [ever] commanded the morning [to begin]? Have you [ever] told the dawn to start a new day?
“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13 Have you [ever] told the dawn to spread out over the whole earth, with the result that wicked people run away from the light?
kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14 When it becomes light after the dawn, the hills and the valleys become clear like the folds in a cloth.
Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15 When it becomes daylight, the wicked do not have the darkness [that they like]; [in the daylight] they no longer are able to raise up their arms, ready to hurt people.
Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16 “[Job, ] have you traveled to the springs [in the bottom of the ocean] from which the water in the seas comes? Have you investigated/explored the very bottom of the oceans?
“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
17 Has someone shown you the gates to the place where dead people are, the gates to the place where it is very dark?
Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18 Do you know how big the earth is? Tell me, if you know all these things!
Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19 “Where is the road to the place where light comes from? And [can you tell me] where darkness lives?
“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
20 Can take me to its home? Do you know where the road is that goes there?
Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21 I am sure that you know these things, because you [talk as though you] were born before the time when all things were created; you [must] be very old!
Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22 “Have you entered the place where I store the snow and the place where I keep the hail?
“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23 I store the snow and the hail [in order that I can use them to help my people] when [they have] troubles, in times when [they are fighting] wars [DOU].
zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24 And where is the road to the place from which I cause the lightning to flash? Where is the place from where the east wind begins to blow over all the earth?
Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25 Who created the channels in which the rain comes down from the sky? Who makes the roads for the thunder/lightning?
Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26 Who causes rain to fall in the desert, in places where no one lives?
kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
27 Who sends the rain that gives moisture/water to areas where nothing has grown, with the result that grass begins to grow again?
kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
28 Does the rain have a father? Does the dew [also] have a father?
Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29 And from whose womb does ice come [in the (winter/cold season)]? Who gives birth to the frost that comes down from the sky?
Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30 [In the winter, ] the water [freezes and] becomes hard, like a rock, and the surface of lakes becomes frozen.
pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31 “[Job], can you fasten the chains that hold the stars together in clusters/groups in the sky?
“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32 Can you tell the stars when they should shine? Can you guide [the stars in the groups in the northern sky whose names are] the Big Bear and the Little Bear?
Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33 Do you know the laws that the stars must obey? Can you cause those same laws to rule [everything here] on the earth?
Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34 “Can you shout to the clouds and cause rain to pour down on you?
“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
35 Can you cause flashes of lightning to come down and strike where you want it to strike? Do those flashes say to you, ‘Where do you want us to strike next?’
Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36 Who enables the clouds to know when they should cause rain to fall?
Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37 And who is skilled/wise enough to be able to count the clouds? Who can tilt the jugs of water in the sky [to cause the rain to fall],
Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38 with the result that the dry ground becomes hard as the dry (clods/lumps of soil) [become wet and] stick together?
pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
39 “When a lioness and her cubs crouch in their dens or hide in a thicket, [waiting for some animal to pass by that they can kill, ] can you find animals for a lioness to kill so that [she and] her cubs can [eat the meat and] not be hungry any more?
“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
41 Who provides dead animals for crows, when the baby crows are calling out to me [for food], [when they are so weak] because of their lack of food [that] they (stagger around/can hardly stand up) [in their nests]?”
Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?

< Job 38 >