< Isaiah 4 >
1 When that happens, [there will be very few unmarried men still alive]. [As a result], seven [unmarried] women will grab one man, and say, “Allow us [all] to marry you [IDM]! We will provide our own food and clothing. All that we want is to no longer be disgraced [because of not being married].”
Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri adzagwira mwamuna mmodzi, nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu, ndi kuvala zovala zathu; inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu. Tichotseni manyazi aumbeta!”
2 [But] some day, Israel [MTY] will be [very] beautiful and great/glorious. The people of Israel who will still be there will be very proud of the wonderful fruit that grows in their land.
Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli.
3 All the people who will remain in Jerusalem, who were not killed when Jerusalem was destroyed, whose names are listed among those who live there, will be [called] holy.
Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu.
4 [That will happen when] Yahweh washes away the guilt of the women of Jerusalem, and when he stops the violence [MET] [on the streets of Jerusalem] by punishing [the people of Jerusalem]. When he does that, it will be like a fire to burn up all the impure things.
Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto.
5 Then Yahweh will send a cloud of smoke every day and a flaming fire every night to cover Jerusalem and [all] those who gather there; it will be [like] a glorious canopy over the city
Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova.
6 that will shelter the people from the sun during the daytime and protect them when there are windstorms and rain.
Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.