< Ezekiel 5 >
1 “Also, you human, [when you start doing those things, ] take a sharp sword and use it like [SIM] a razor to shave your head and your beard. Then put the hair that you shaved off on scales, and divide the [into three equal parts].
Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu.
2 When the time during [you will symbolize that] the city will be [by enemy troops] ends, put a third of the hair inside [drawing of the] city and burn it. Take another third of the hair, [scatter it] all [the drawing of] the city, and then strike it with your sword. That will symbolize that I will strike the people of Jerusalem [their enemies’] swords. Then allow the wind to scatter the other third of the hair. That will symbolize [even if they flee from the city], I will [cause their enemies to] pursue them and attack them with swords.
Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga.
3 Take a few of your hairs and tuck them into the folds of your robe.
Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako.
4 Then take a few of those hairs, throw them into the fire, and burn them up. [That will symbolize that] a fire will spread from Jerusalem [and destroy things] throughout Israel.
Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”
5 This is what [I, ] Yahweh the Lord, say: ‘[drawing will represent] Jerusalem, [the city which] I have set in the center of the nations, with [other] countries around it.
Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira.
6 But the wicked people of Jerusalem rebelled against [obeying] my commands, and [they show that] they are more wicked than the people of the surrounding countries. They rejected my laws and refused to obey my commands.’
Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.
7 Therefore, this is what I, Yahweh the Lord, say: ‘You people of Jerusalem have been more rebellious than the people of the nations around you; you have not obeyed any of my laws [DOU]. You have not even obeyed the laws of the nations around you!’
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.
8 Therefore, this is [I, ] Yahweh the Lord, say: ‘I am opposed to [you people of] Jerusalem. I will punish you, and the [people of other] nations will see it happen.
“Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona.
9 Because of all your detestable [idols], I will punish [people of Jerusalem] like I have never done before and will never do again.
Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo.
10 As a result, parents among you will eat their children, and children will eat their [because there will be nothing else to eat]. I will punish you [severely], and I will cause those who will still be alive to be scattered in all directions [IDM].’
Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi.
11 Therefore, I, Yahweh the Lord, declare that as surely as I am alive, because you have polluted my temple with all your disgusting [statues of idols] and by the other detestable things that you do, I will no longer bless you. I will not pity [you] or act mercifully [toward you].
Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni.
12 One-third of your people will die inside the city because of the plagues [they will experience] or by (famine/lack of food). One-third of your people will be killed [your enemies’] swords outside the city. And one-third I will cause to be scattered in all directions; [your enemies] will [still] pursue you and kill you with their swords.
Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.
13 Then I will no longer be angry with you; I will stop punishing [MTY] you after I have gotten revenge on you. And when I stop punishing you, you will know that I, Yahweh, have spoken to you because I have been very strongly concerned [what you have done].
“Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.
14 I will cause your [city] to be a ruins, with the result that [people of other] nations that are around you will pass by and see it and sneer at you.
“Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo
15 They will make fun of you and taunt you. When I severely punish you because of my being very angry [DOU] with you, they will be horrified and they will be warned. [That will surely happen because] I, Yahweh, have said it.
Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula.
16 When I cut off your food supply and cause there to be more famine, [it will be as though] [MET] I am shooting at you with my arrows that will destroy you.
Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku.
17 I will cause you to experience a famine, and I will send wild beasts to attack you and your children, and [all] your children will be killed. You will experience plagues and wars, and I will cause [your enemies] to attack you with their swords. [That will surely happen because] I, Yahweh, have said it.”
Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”