< 1 Kings 15 >
1 After Jeroboam had been the king of Israel for almost 18 years, Abijah became the king of Judah.
Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Nebati, Abiya anakhala mfumu ya Yuda,
2 He ruled for three years in Jerusalem. His mother’s name was Maacah, the granddaughter of [David’s son] Absalom.
ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zitatu. Amayi ake anali Maaka, mwana wa Abisalomu.
3 Abijah committed the same kind of sins that his father had committed. He was not fully dedicated/committed to Yahweh his God, as his grandfather David had been.
Abiya anachita zoyipa zonse zimene abambo ake anazichita. Sanali wangwiro pamaso pa Yehova Mulungu wake, monga linachitira kholo lake Davide.
4 But, because of [what Yahweh his God had promised to] David, Yahweh gave Abijah a son [MET] to rule in Jerusalem after him, and in order to protect Jerusalem [from their enemies].
Komabe chifukwa cha Davide, Yehova Mulungu wake anamupatsa nyale mu Yerusalemu pomupatsa mwana wolowa mʼmalo mwake ndi kumukhazikitsa kukhala wamphamvu mu Yerusalemu;
5 Yahweh did that because David had always done what pleased Yahweh and because David had always obeyed Yahweh. The only time when he disobeyed Yahweh was when he caused Uriah [to be killed].
pakuti Davide anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo sanalephere kusunga chilichonse chimene Yehova anamulamula masiku onse a moyo wake kupatula nkhani ija ya Uriya Mhiti.
6 There were wars between [the armies of] Rehoboam and Jeroboam all during the time that Abijah ruled.
Panali nkhondo pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu masiku onse a moyo wa Abiya.
7 Everything else that Abijah did is written [RHQ] in the scroll called ‘The History of the Kings of Judah’.
Tsono ntchito zina za Abiya, ndi zina zonse anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
8 Abijah died [EUP] and was buried in [the part of Jerusalem called] ‘The City of David’, and his son Asa became king.
Ndipo Abiya anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Asa, mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
9 After Jeroboam had been the king of Israel for almost 20 years, Asa started to rule Judah.
Mʼchaka cha makumi awiri cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Asa anakhala mfumu ya Yuda,
10 He ruled in Jerusalem for 41 years. His grandmother was Maacah, the granddaughter of Absalom.
ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 41. Agogo ake akazi anali Maaka mwana wa Abisalomu.
11 Asa did what was pleasing to Yahweh, as his ancestor David had done.
Asa anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
12 He got rid of the male prostitutes that were at the places where the people worshiped idols, and he also got rid of all the idols that his ancestors had made.
Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zadama pochita chipembedzo chawo ndiponso anachotsa mafano onse amene makolo ake anawapanga.
13 He also removed his grandmother Maacah so that she no longer had influence in the government [because of] being the mother of a previous king. He did that because she had made a disgusting [wooden] statue of the goddess Asherah. Asa [told his workers to] cut down the statue and burned it in the Kidron Valley.
Iye anachotsanso gogo wake Maaka pa udindo wake wa amayi a mfumu, chifukwa choti anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo nakalitentha ku Chigwa cha Kidroni.
14 He was not able to destroy all the places where the people worshiped [idols] on the high hills, but he continued to be dedicated/committed to Yahweh his entIre life.
Ngakhale sanachotse malo opembedzerapo mafano, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova masiku onse a moyo wake.
15 He [told his workers to] place in the temple all the items that his father had dedicated to God, and all the gold and silver things that he had dedicated to God.
Asa anabweretsa ku Nyumba ya Yehova zinthu zimene abambo ake anazipereka, ndiponso zinthu zimene iye mwini anazipereka: zagolide, siliva ndi ziwiya zotengera.
16 There were wars between [the armies of] Asa and Baasha, the king of Israel, all during the time that they ruled.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
17 Baasha’s army invaded Judah. They captured Ramah [town north of Jerusalem]. Then they started to build a wall around it in order to prevent people from entering or leaving the area in Judah that was ruled by King Asa.
Baasa mfumu ya Israeli anapita kukathira nkhondo dziko la Yuda, ndipo anamangira linga mzinda wa Rama kuletsa kuti wina aliyense asatuluke kapena kulowa mʼdziko la Asa, mfumu ya Yuda.
18 So Asa [told] his workers [to] take all the silver and gold that was still in the storerooms in the temple and in the palace. He told them to take it to Damascus and give it to King Ben-Hadad who ruled Syria. Ben-Hadad was the son of Tabrimmon and grandson of Hezion. He told the workers to say this to Ben-Hadad:
Tsono Asa anatenga siliva yense pamodzi ndi golide zimene zinatsala ku malo osungira chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso ku nyumba yake yaufumu. Anazipereka kwa atumiki ake, nawatuma kupita nazo kwa Beni-Hadadi mwana wa Tabirimoni, mwana wa Heziyoni, mfumu ya Aramu, amene ankakhala ku Damasiko ndipo anakamuwuza kuti,
19 “I want there to be a peace treaty between you and me, like there was between your father and my father. For that reason, I am giving you this silver and gold. So now please cancel the treaty that you made with Baasha, the king of Israel, in order that he will take his soldiers away from attacking mine, [because he will be afraid of your army].”
“Tiyeni tigwirizane inu ndi ine, monga panali mgwirizano pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Onani, ndikukutumizirani mphatso za siliva ndi golide. Tsopano kathetseni mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti andisiye.”
20 [So the workers went and gave the message to] Ben-Hadad, [and he] did what Asa suggested. He sent his army commanders [and their soldiers] to attack some of the towns in Israel. They captured Ijon, Dan, Abel-Beth-Maacah, the area near Galilee Lake, and all the land of [the tribe of] Naphtali.
Choncho Beni-Hadadi anamvera zimene ananena mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira magulu ake ankhondo ku mizinda ya Israeli. Ndipo iye anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Beti-Maaka ndi dera lonse la Kinereti kuphatikiza dziko lonse la Nafutali.
21 When Baasha heard about that, he [told his soldiers to] stop working at Ramah. He [and his soldiers returned to] Tirzah [and] stayed there.
Baasa atamva zimenezi, anasiya kumangira linga Rama ndipo anakakhala ku Tiriza.
22 Then King Asa sent a message to all the [people in the] towns in Judah, stating that they all were required to go to Ramah and carry away the stones and timber that Baasha’s soldiers had been using to build a wall around the city. With those stones and timber they fortified Mizpah [city north of Jerusalem], and Geba, [a town] in the territory of the tribe of Benjamin.
Pamenepo Mfumu Asa analamula anthu onse a ku Yuda osasiya ndi mmodzi yemwe, ndipo anachotsa ku Rama miyala ndi matabwa amene Baasa ankamangira kumeneko. Zipangizo zimenezi Mfumu Asa inamangira linga la Geba ku Benjamini ndi la ku Mizipa.
23 Everything else that Asa did, the armies that his soldiers defeated, and the names of the cities that he caused to be fortified, are [RHQ] written in the scroll called ‘The History of the Kings of Judah’. But when Asa became old, he got a disease in his feet.
Tsono ntchito zina za Asa, za mphamvu zake ndi mizinda imene anayimanga ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Koma pa nthawi ya ukalamba wake anadwala nthenda ya mapazi.
24 He died [EUP] and was buried where his ancestors were buried in [the part of Jerusalem called] ‘The City of David’. Then his son Jehoshaphat became king.
Ndipo Asa anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu mzinda wa Davide kholo lake. Ndipo Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 After Asa had been the king of Judah for almost two years, King Jeroboam’s son Nadab started to rule Israel. He ruled for two years.
Nadabu, mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli mʼchaka chachiwiri cha Asa mfumu ya Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
26 He did things that Yahweh considered to be evil. His behavior was sinful like his father’s behavior had been, and what he did led the people of Israel to sin.
Nadabu anachita zoyipa pamaso pa Yehova, anayenda mʼnjira za abambo ake ndi mu uchimo womwe anachimwitsa nawo Israeli.
27 [A man named] Baasha, from the tribe of Issachar, planned to harm him. He killed Nadab when Nadab and his army had surrounded Gibbethon [city] in the Philistia area.
Baasa mwana wa Ahiya, wa banja la Isakara anakonzera Nadabuyo chiwembu, ndipo anamukantha ku Gibetoni, mzinda wa Afilisti, pamene Nadabu ndi anthu onse a ku Israeli anali atawuzungulira.
28 That [DOU] was when Asa had been [the king ruling] Judah for almost three years. Then Baasha became the king of Israel.
Baasa anapha Nadabu mʼchaka chachitatu cha Asa, mfumu ya ku Yuda ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 As soon as Baasha became king, [he commanded his soldiers to] kill all of Jeroboam’s family. Doing what Yahweh had told the prophet Ahijah from Shiloh would happen, they killed all of Jeroboam’s family. None of them (was left/remained alive).
Iye atangoyamba kulamulira, anapha anthu onse a banja la Yeroboamu. Sanasiye ndi mmodzi yemwe wamoyo pa banjapo, koma anawononga anthu onse, molingana ndi mawu a Yehova amene anayankhula mwa mtumiki wake Ahiya wa ku Silo
30 That happened because Yahweh had become very angry with Jeroboam because of all the sins that Jeroboam had committed, and because of the sins that he had persuaded the people of Israel to commit.
chifukwa cha machimo amene Yeroboamu anachita, ndiponso kuchimwitsa anthu a ku Israeli, naputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israeli.
31 Everything else that Nadab did is written [RHQ] in the scroll called ‘The History of the Kings of Israel’.
Tsono ntchito za Nadabu ndi zina zonse zimene anazichita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
32 There were wars between [the armies of] King Asa and King Baasha all the time that they ruled.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli pa nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
33 After Asa had been the king of Judah for almost three years, Baasha, the son of Ahijah, started to rule Israel at Tirzah [city]. He ruled for 24 years.
Chaka chachitatu cha Asa mfumu ya Yuda, Baasa mwana wa Ahiya anakhala mfumu ya Aisraeli onse ku Tiriza, ndipo analamulira zaka 24.
34 He did things that Yahweh considered to be evil, and his behavior was sinful like his father’s had been, and he led the people of Israel to sin.
Anachita zoyipa pamaso pa Yehova, nayenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchita tchimo lake limene linachimwitsa anthu a ku Israeli.