< 1 Chronicles 24 >

1 These are the groups of the descendants of Aaron [the first Supreme Priest]: Aaron’s four sons were Nadab, Abihu, Eleazar, and Ithamar.
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 But Nadab and Abihu died before their father died, and they had no children. So their [younger] brothers Eleazar and Ithamar became the priests.
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 Zadok, who was a descendant of Eleazar, and Ahimelech, who was a descendant of Ithamar, helped David to separate his descendants into two groups. Each group had certain duties.
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 There were more leaders among the descendants of Eleazar than there were among the descendants of Ithamar. So they appointed 16 leaders from Eleazar’s descendants and eight leaders from Ithamar’s descendants.
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 There were temple officials and priests, including descendants of both Eleazar and Ithamar, to make sure that the work was divided fairly. So they decided what work each person would do by (casting lots/throwing marked stones).
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 Shemaiah, the son of Nethanel, who was a descendant of Levi, wrote down the names [of the leaders of each group] while David and his officials were watching. Zadok, the [Supreme] Priest, and Ahimelech [his assistant], and the leaders of the families of the priests and of the families of the other descendants of Levi also watched.
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 Jehoiarib was the first one whose name was selected [by casting lots/throwing marked stones]. Next Jedaiah was selected.
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 Next, Harim was selected. Next, Seorim was selected.
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 Next, Malkijah was selected. Next, Mijamin was selected.
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 Next, Hakkoz was selected. Next, Abijah was selected.
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 Next, Jeshua was selected. Next, Shecaniah was selected.
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 Next, Eliashib was selected. Next, Jakim was selected.
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 Next, Huppah was selected. Next, Jeshebeab was selected.
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 Next, Bilgah was selected. Next, Immer was selected.
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 Next, Hezir was selected. Next, Happizzez was selected.
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 Next, Pethahiah was selected. Next, Jehezkel was selected.
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 Next, Jakin was selected. Next, Gamul was selected.
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 Next, Delaiah was selected. Next, Maaziah was selected.
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 Those were the men who were chosen to be the leaders of the groups that would serve in the temple, obeying the regulations that were set down by Aaron, regulations which Yahweh, the God to whom the Israeli people belonged, had given to him.
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 [This is a list of some of] the other descendants of Levi: Amram was the ancestor of Shubael and Jehdeiah.
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 Rehabiah was the ancestor of Isshiah, the oldest son in his family.
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 Izhar was the father of Shelomoth and the grandfather of Jahath.
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 [Kohath’s son] Hebron had four sons: Jeriah and his [younger] brothers Amariah, Jahaziel, and Jekameam.
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 Uzziel was the father of Micah and the grandfather of Shamir.
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 Micah’s [younger] brother was the father of Zechariah.
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 The sons of Merari were Mahli, Mushi, and Jaaziah.
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 Jaaziah had four sons: Beno, Shoham, Zaccur, and Ibri.
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 Mahli’s son Eleazar did not have any sons.
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 From the descendants of [Mahli’s second son] there was Jerahmeel.
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 The sons of Mushi were Mahli, Eder, and Jerimoth. Those were descendants of Levi who were listed according to the leaders of their families.
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 The jobs they would do were decided by (casting lots/throwing marked stones), like their fellow Israelis, the descendants of Aaron, did. They cast lots {The lots were cast} while King David, Zadok, Ahimelech, and the leaders of the families of the priests and the [other] descendants of Levi watched. They gave the same jobs to the families of each oldest brother and each youngest brother.
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

< 1 Chronicles 24 >