< 1 Chronicles 24 >

1 and to/for son: descendant/people Aaron division their son: child Aaron Nadab and Abihu Eleazar and Ithamar
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 and to die Nadab and Abihu to/for face: before father their and son: child not to be to/for them and to minister Eleazar and Ithamar
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 and to divide them David and Zadok from son: child Eleazar and Ahimelech from son: child Ithamar to/for punishment their in/on/with service: ministry their
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 and to find son: child Eleazar many to/for head: leader [the] great man from son: child Ithamar and to divide them to/for son: child Eleazar head: leader to/for house: household father six ten and to/for son: child Ithamar to/for house: household father their eight
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 and to divide them in/on/with allotted these with these for to be ruler holiness and ruler [the] God from son: child Eleazar and in/on/with son: child Ithamar
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 and to write them Shemaiah son: child Nethanel [the] secretary from [the] Levi to/for face: before [the] king and [the] ruler and Zadok [the] priest and Ahimelech son: child Abiathar and head: leader [the] father to/for priest and to/for Levi house: household father one to grasp to/for Eleazar and to grasp to grasp to/for Ithamar
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 and to come out: casting(lot) [the] allotted [the] first to/for Jehoiarib to/for Jedaiah [the] second
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 to/for Harim [the] third to/for Seorim [the] fourth
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 to/for Malchijah [the] fifth to/for Mijamin [the] sixth
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 to/for Hakkoz [the] seventh to/for Abijah [the] eighth
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 to/for Jeshua [the] ninth to/for Shecaniah [the] tenth
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 to/for Eliashib eleven ten to/for Jakim two ten
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 to/for Huppah three ten to/for Jeshebeab four ten
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 to/for Bilgah five ten to/for Immer six ten
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 to/for Hezir seven ten to/for Happizzez eight ten
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 to/for Pethahiah nine ten to/for Jehezkel [the] twenty
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 to/for Jachin one and twenty to/for Gamul two and twenty
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 to/for Delaiah three and twenty to/for Maaziah four and twenty
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 these punishment their to/for service: ministry their to/for to come (in): come to/for house: temple LORD like/as justice: rule their in/on/with hand: by Aaron father their like/as as which to command him LORD God Israel
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 and to/for son: descendant/people Levi [the] to remain to/for son: child Amram Shebuel to/for son: child Shebuel Jehdeiah
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 to/for Rehabiah to/for son: child Rehabiah [the] head: leader Isshiah
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 to/for Izharite Shelomoth to/for son: child Shelomoth Jahath
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 and son: child Jeriah Amariah [the] second Jahaziel [the] third Jekameam [the] fourth
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 son: child Uzziel Micah to/for son: child Micah (Shamir *Q(K)*)
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 brother: male-sibling Micah Isshiah to/for son: child Isshiah Zechariah
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 son: child Merari Mahli and Mushi son: child Jaaziah (Beno *L(F)*)
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 son: child Merari to/for Jaaziah (Beno *L(F)*) and Shoham and Zaccur and Ibri
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 to/for Mahli Eleazar and not to be to/for him son: child
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 to/for Kish son: child Kish Jerahmeel
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 and son: child Mushi Mahli and Eder and Jerimoth these son: child [the] Levi to/for house: household father their
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 and to fall: allot also they(masc.) allotted to/for close brother: male-sibling their son: child Aaron to/for face: before David [the] king and Zadok and Ahimelech and head: leader [the] father to/for priest and to/for Levi father [the] head: leader to/for close brother: male-relative his [the] small
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

< 1 Chronicles 24 >