< Psalms 58 >

1 To the Chief Musician. "Do not Destroy." A precious Psalm, of David. Are ye, indeed, silent [when] righteousness, ye should speak? When, with equity, ye should judge, O ye sons of men?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
2 Aye! ye all do work, perversity, —Throughout the land, your hands, weigh out, violence!
Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
3 Lawless men have been estranged from birth, They have gone astray from their nativity, speaking falsehood;
Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
4 Their poison, is like unto the poison of a serpent, Like the deaf adder, that stoppeth his ear;
Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
5 That will not hearken to the voice of whisperers, Though the wise one try to bind him with spells.
Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
6 O God! break away their teeth in their mouth, The biters of the young lions, knock thou out, O Yahweh!
Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
7 Let such men flow away like waters that disperse themselves: He prepareth his arrow, Like [grass] let them be cut down:
Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
8 Like a snail, which melteth away as it goeth, An untimely birth of a woman, which hath not seen the sun:
Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
9 Before your kettles can perceive the [kindled] bramble, Be he green or be he withered, he shall be swept away.
Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 The righteous man will rejoice when he hath seen an avenging, His feet, will he bathe in the blood of the lawless one: —
Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 So that a son of earth may say—Surely there is fruit for the righteous man! Surely there are gods who judge in the earth!
Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”

< Psalms 58 >