< Psalms 52 >

1 To the Chief Musician. A Psalm of Instruction, of David. When Doeg the Edomite went, and told Saul; and said to him, —David, hath entered the house of Ahimelech. Why dost thou boast thyself of wickedness, O mighty man? The lovingkindness of GOD, [lasteth] all the day.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.” Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu? Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse, iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?
2 Engulfing ruin, doth thy tongue devise, Like a whetted razor, working deceit;
Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena; lilime lako lili ngati lumo lakuthwa, ntchito yako nʼkunyenga.
3 Thou lovest Evil more than good, Falsehood, more than speaking righteousness. (Selah)
Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi. Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona. (Sela)
4 Thou lovest all devouring words, O deceitful tongue!
Umakonda mawu onse opweteka, iwe lilime lachinyengo!
5 GOD also, will break thee down utterly, He will snatch thee up and tear thee away tentless, And uproot thee, out of the land of the living. (Selah)
Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya: iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako; iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.
6 The righteous shall both see and fear, And, over him, shall laugh:
Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha; adzamuseka nʼkumanena kuti,
7 Lo! the man who made not God his refuge, —But trusted in the abundance of his riches, Emboldened himself in his wealth!
“Pano tsopano pali munthu amene sanayese Mulungu linga lake, koma anakhulupirira chuma chake chambiri nalimbika kuchita zoyipa!”
8 But, I, am like a flourishing olive-tree, in the house of God, I have put confidence in the lovingkindness of God, for times age-abiding and beyond.
Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu; ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu kwa nthawi za nthawi.
9 I will praise thee to times age-abiding, Because thou didst effectually work, —And I will wait on thy Name, Because it is good, In the presence of thy men of lovingkindness.
Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita; chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.

< Psalms 52 >