< Numbers 18 >

1 And Yahweh said unto Aaron, Thou and thy sons and the house of thy father with thee, shall bear the iniquity of the sanctuary, —and, thou, and thy sons with thee, shall bear the iniquity of your priesthood.
Yehova anawuza Aaroni kuti, “Iwe, ana ako aamuna ndi banja la abambo ako mudzasenza tchimo la malo wopatulika, koma iwe ndi ana ako aamuna okha mudzasenza tchimo lokhudza unsembe wanu.
2 Therefore also thy brethren of the tribe of Levi the stem of thy father, bring thou near with thee, and let them be joined unto thee, and let them wait upon thee, —both on thee and on thy sons with thee, before the tent of the testimony.
Ubweretse Alevi, abale ako, kuchokera ku fuko la abambo ako kuti azikhala ndi iwe ndi kumakuthandiza pamodzi ndi ana ako amuna pamene mukutumikira mu tenti ya umboni.
3 So shall they keep thy charge, and the charge of all the tent, —only, unto the vessels of the sanctuary, and unto the altar, shall they not come near, lest they die—both they, and ye.
Iwowo azikutumikirani ndipo azichita ntchito zonse za ku tenti, koma asamafike pafupi ndi zipangizo za ku malo opatulika kapena guwa lansembe, kuopa kuti iwo ndi inu mungafe.
4 So shall they be joined unto thee, and shall keep the charge of the tent of meeting, as to all the laborious work of the tent, —but a stranger, shall not come near unto you.
Azikhala ndi inu ndipo azisamalira ntchito yonse ya mu tenti ya msonkhano koma munthu wina aliyense wapadera sayenera kufika pafupi nanu.
5 So shall ye keep the charge of the sanctuary, and the charge of the altar, —that there no more be wrath against the sons of Israel.
“Inuyo muzisamalira malo wopatulika ndi guwa lansembe, kuti ukali wa Yehova usawagwerenso Aisraeli.
6 I, therefore, lo! I have taken your brethren the Levites, out of the midst of the sons of Israel, —unto you, as a gift are they given, unto Yahweh, to do the laborious work of the tent of meeting.
Ine mwini ndasankha Alevi, abale ako, pakati pa Aisraeli ngati mphatso yako ndipo aperekedwa kwa Yehova kuti azigwira ntchito ku tenti ya msonkhano.
7 But thou and thy sons with thee, shall keep the charge of your priesthood, as to every matter of the altar and as to the interior of the veil, and shall do the laborious work, as a laborious service of gifts, do I give your priesthood, and, the stranger who cometh near shall be put to death.
Koma iwe wekha ndi ana ako aamuna muzitumikira ngati ansembe ndi zina zonse zokhudza pa guwa lansembe ndi za mʼkati mwa malo wopatulika kwambiri. Ndikukupatsani mphatso ya utumiki wa unsembe. Aliyense woyandikira malo wopatulika ayenera kuphedwa.
8 And Yahweh spake unto Aaron, I, therefore, lo! I have given unto thee the charge of my heave-offerings, —as to all the hallowed things of the sons of Israel—unto thee, have I given them. as pertaining to the anointing, and unto thy sons. for a statute age-abiding,
“Kenaka Yehova anati kwa Aaroni, ona, Ine mwini ndikukuyika kuti ukhale woyangʼanira zopereka zobwera kwa Ine; zopereka zonse zopatulika za Aisraeli zimene amapereka kwa ine ndi kuzipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ngati gawo lanu la nthawi zonse.
9 This, shall be thine, out of the things most holy, out of the fire, —their every oblation—to the extent of their every meal-offering, and their every sin-bearer, and their every guilt-bearer wherewith they make amends unto me, most holy unto thee, shall it be and unto thy sons.
Uzilandiranso gawo la zopereka zopatulika kwambiri zomwe sizinawotchedwe pa moto. Kuchokera pa mphatso zonse zimene amabweretsa kwa Ine ngati zopatulika kwambiri, nsembe zachakudya kapena nsembe zopepesera machimo, gawo limenelo ndi lako ndi ana ako aamuna.
10 As something most holy, shall ye eat it, —every male, shall eat it, holy, shall it be unto thee.
Muzidya zimenezo ngati zinthu zopatulika kwambiri; mwamuna aliyense adyeko. Uzitenge kukhala zopatulika.
11 This, therefore, shall be thine—the heave-offering of their gift even all the wave-offerings of the sons of Israel, unto thee, have I given them and unto thy sons and unto thy daughters with thee by a statute age-abiding, —every one that is clean in thy house, shall eat it.
“Izinso ndi zako: chilichonse chopatulidwa kuchokera ku mphatso zoweyula za Aisraeli ndapereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lako la nthawi zonse. Aliyense wa mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa monga mwa mwambo angathe kudyako.
12 All the best of oil, and all the best of new-wine and corn, —the firstfruits thereof which they shall give unto Yahweh, unto thee, have I given them.
“Ndikukupatsani mafuta onse abwino kwambiri a olivi ndi vinyo yense watsopano wabwino kwambiri ndi tirigu yense zomwe Aisraeli amapereka kwa Yehova ngati zipatso zoyamba pa zokolola zawo.
13 The firstfruits of all that is in their land which they shall bring in unto Yahweh, thine, shall it be, —every one that is clean in thy house, shall eat it:
Zipatso zonse zoyamba kucha za mʼdziko lawo zomwe amapereka kwa Yehova zidzakhala zako. Aliyense mʼnyumba mwako amene ali woyeretsedwa angathe kudyako.
14 every devoted thing in Israel, thine, shall it be:
“Chilichonse mu Israeli chomwe chapatulidwira Yehova ndi chako.
15 every thing that is born first of all flesh that may be offered unto Yahweh among men and among beasts, shall be thine, —only thou shalt, redeem, the firstborn of men, and the firstborn of unclean beasts, shalt thou redeem.
Chilichonse choyamba kubadwa kwa munthu kaya nyama, chomwe chaperekedwa kwa Yehova ndi chako. Koma uyenera kuwombola mwana aliyense wamwamuna ndi mwana aliyense woyamba wa nyama zodetsedwa.
16 And, as to the redemption price thereof, from a month old, shalt thou redeem, by thine estimate five shekels of silver by the shekel of the sanctuary, —twenty gerahs, it is.
Pamene zili ndi mwezi umodzi wa kubadwa, uziwombole pa mtengo wowombolera wa ndalama zisanu zasiliva, monga mwa ndalama za ku malo wopatulika.
17 Only a firstling ox or a firstling sheep or a firstling goat, shalt thou not redeem, hallowed, they are, —their blood, shalt thou dash against the altar and of their fat, shalt thou make a perfume, an altar-flame, for a satisfying odour unto Yahweh:
“Koma usawombole ana oyamba kubadwa a ngʼombe, nkhosa kapena mbuzi. Iwo ndi opatulika. Uwaze magazi a nyamazi pa guwa lansembe ndi kutentha mafuta ake ngati nsembe yotentha ndi moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
18 and their flesh, shall be thine, —as the wave-breast and as the right leg, thine, shall it be:
Nyama yake ikhale yanu monga momwe chimakhalira chidale cha nsembe yoweyula ndi ntchafu za miyendo ya kumanja, zonsezi ndi zako.
19 all the heave-offerings of the holy things which the sons of Israel shall heave up unto Yahweh, have I given unto thee and unto thy sons and unto thy daughters with thee by a statute age-abiding, —an age-abiding covenant of salt, it is before Yahweh, for thee and for thy seed with thee.
Zonse zimene mwazichotsa ku zopereka zoyera zomwe Aisraeli anapereka kwa Yehova ndazipereka kwa iwe ndi ana ako aamuna ndi aakazi ngati gawo lanu nthawi zonse. Ili ndi pangano losatha la mchere pamaso pa Yehova kwa iwe ndi ana ako.”
20 Then said Yahweh unto Aaron: In their land, thou shalt have no inheritance, and no allotted portion, shalt thou have in their midst, —I, am thine allotted portion and thine inheritance in the midst of the sons of Israel.
Ndipo Yehova anati kwa Aaroni, “Iweyo sudzakhala ndi cholowa mʼdziko lawo, ndiponso sudzalandira gawo lililonse pakati pawo. Ine ndine gawo lako ndi cholowa chako pakati pa Aisraeli.
21 And unto the sons of Levi, lo! I have given all the tenth in Israel for an inheritance, —the allotted portion for their laborious work which, they are performing, the laborious work of the tent of meeting:
“Taonani, ndawapatsa Alevi chakhumi chonse mu Israeli ngati cholowa chawo chifukwa cha ntchito ya ku tenti ya msonkhano.
22 that the sons of Israel come near no more, unto the tent of meeting, —to bear sin, to die.
Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo Aisraeli asamapite pafupi ndi tenti ya msonkhano. Ngati atero adzasenza zotsatira za tchimo lawo ndipo adzafa.
23 So shall the Levites themselves perform the laborious work of the tent of meeting, and, they, shall bear their iniquity, a statute age-abiding, unto your generations, and in the midst of the sons of Israel, shall they take no inheritance.
Alevi ndi amene azidzagwira ntchito ya ku tenti ya msonkhano ndipo adzalangidwa chilichonse chikalakwika. Ili ndi lamulo losatha kwa mibado yawo yonse. Iwowo sadzalandira cholowa pakati pa Aisraeli.
24 Because the tenth of the sons of Israel which they shall offer up unto Yahweh as a heave-offering, have I given unto the Levites as an inheritance, —for this cause, said I regarding them, In the midst of the sons of Israel, shall they take no inheritance.
Mʼmalo mwake, ndikuwapatsa Aleviwo chakhumi ngati cholowa chawo chimene Aisraeli amapereka kwa Yehova. Nʼchifukwa chake zokhudza iwo ndinati: ‘Sadzakhala ndi cholowa pakati pa Aisraeli.’”
25 Then spake Yahweh unto Moses, saying:
Yehova anati kwa Mose,
26 Unto the Levites, therefore shalt thou speak and shalt say unto them, When ye shall take of the sons of Israel the tenth which I have given unto you from them as your inheritance, then shall ye offer up therefrom the heave-offering of Yahweh, a tenth of the tenth.
“Yankhula ndi Alevi ndi kunena nawo kuti, ‘Pamene mulandira chakhumi kuchoka kwa Aisraeli chimene ndimakupatsani ngati cholowa chanu, muyenera kupereka chakhumi cha choperekacho kwa Yehova.
27 So shall your heave-offering be reckoned your own, —as corn out of the threshing-floor, and as the abundance out of the wine-press.
Chopereka chanucho chidzawerengedwa kwa inu ngati tirigu wochokera kopunthira kapena ngati mphesa zopsinya kuchokera kopsinyira mphesa.
28 Thus, shall ye also, offer up the heave-offering of Yahweh, out of all your tenths which ye shall take from the sons of Israel, —and give therefrom the heave-offering of Yahweh, unto Aaron the priest.
Mwa njira imeneyi inunso muzipereka chopereka kwa Yehova kuchokera ku chakhumi chanu chilichonse chimene mumalandira kuchokera kwa Aisraeli. Kuchokera ku chakhumicho muziperekako gawo la Yehova kwa Aaroni, wansembe.
29 Out of all your gifts, shall ye offer up every heave-offering of Yahweh, —out of all the best thereof, the hallowed pert thereof out of it.
Muyenera kupereka monga gawo la Yehova magawo abwino kwambiri ndi opatulika a chilichonse chimene chapatsidwa kwa inu.’
30 And thou shalt say unto them, —When ye offer the best thereof out of it, then shall it be reckoned to belong unto the Levites, as the increase of the threshing-floor and as the increase of the wine-press,
“Nena kwa Alevi: ‘Pamene mupereka gawo labwino lopambana zonse, gawo limenelo lidzawerengedwa kwa inu ngati lochokera popunthira tirigu kapenanso kopsinyira mphesa.
31 And ye shall eat it in any place, ye, and your household, —for a reward, it is unto you, the allotted portion for your laborious work in the tent of meeting.
Inu ndi a pa banja panu mungathe kudyera zimenezi paliponse chifukwa ndi malipiro a ntchito yanu ya ku tenti ya msonkhano.
32 And ye shall not by reason of it bear sin, when ye offer up the best thereof, out of it; and the hallowed things of the sons of Israel, shall ye not profane neither shall ye die.
Popereka gawo labwino kwambirilo simudzapezeka olakwa. Mukatero simudzadetsa zopereka zoyera za Aisraeli, ndipo simudzafa.’”

< Numbers 18 >