< Numbers 10 >

1 And Yahweh spake unto Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Make thee two trumpets of silver, of beaten work, shalt thou make them, —and they shall be unto thee for calling the assembly, and for setting forward the camps.
“Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa.
3 As soon as they blow therewith, so soon shall all the assembly assemble themselves unto thee, unto the entrance of the tent of meeting.
Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano.
4 And, if, only once, they blow, then shall the princes, the heads of the thousands of Israel, gather themselves unto thee.
Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe.
5 But when ye blow an alarm, then shall set forward the camps that are encamped eastwards;
Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka.
6 and when ye blow a second alarm, then shall set forward the camps that are encamped southwards, —an alarm, shall they blow for setting them forward,
Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo.
7 But in calling together the convocation, ye shall blow but shall not sound an alarm.
Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.
8 And, the sons of Aaron the priests, shall blow with the trumpets, —and it shall be unto you for a statute age-abiding, unto your generations.
“Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse.
9 And when ye go into war in your land against the assailant that assaileth you, then shall ye blow an alarm with the trumpets, —and bring yourselves to mind before Yahweh your God, and be saved, from your enemies,
Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu.
10 And in your day of rejoicing and in your appointed seasons and in the beginnings of your months, then shall ye blow with the trumpets, over your ascending-sacrifices, and over your peace-offerings, —so shall they be unto you for a memorial before your God. I—Yahweh, am your God.
Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”
11 And so it came to pass in the second year, in the second month on the twentieth of the month, that the cloud lifted itself up, from off the habitation of the testimony;
Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni.
12 and the sons of Israel set forward by their removals from the desert of Sinai, and then the cloud abode in the desert of Paran.
Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani.
13 Thus then did they set forward for the first time, —at the bidding of Yahweh, by the hand of Moses.
Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.
14 So the standard of the camp of the sons of Judah set forward first, by their hosts, and over his own host, was Nahshon, son of Amminadab;
Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu.
15 and, over the host of the tribe of the sons of Issachar, Nethanel, son of Zuar;
Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara,
16 and, over the host of the tribe of the sons of Zebulun, Eliab, son of Helon.
Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni.
17 Then was taken down the habitation, —and the sons of Gershon and the sons of Merari set forward bearing the habitation.
Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.
18 Then set forward the standard of the camp of Reuben, by their hosts, —and over his own host, Elizur, son of Shedeur;
Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri.
19 and, over the host of the tribe of the sons of Simeon, Shelumiel, son of Zurishaddai;
Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai,
20 and, over the host of the tribe of the sons of Gad, Eliasaph, son of Deuel.
ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi.
21 Then set forward the Kohathites, bearing the sanctuary, —and so the habitation was reared by the time they came in.
Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.
22 Then set forward the standard of the camp of the sons of Ephraim by their hosts, —and over his own host, was Elishama son of Ammihud;
Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo.
23 and, over the host of the tribe of the sons of Manasseh, Gamaliel, son of Pedahzur;
Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase.
24 and, over the host of the tribe of the sons of Benjamin, Abidan, son of Gideoni.
Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.
25 Then set forward the standard of the camp of the sons of Dan, bringing up the rear of all the camps, by their hosts, —and over his own host, Ahiezur, son of Ammishaddai;
Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
26 and, over the host of the tribe of the sons of Asher, Pagiel, son of Ochran;
Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri,
27 and, over the host of the tribe of the sons of Naphtali, Ahira, son of Enan.
ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani.
28 These, were the settings-forward of the sons of Israel by their hosts, —thus did they set forward.
Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.
29 Then said Moses to Hobab, son of Raguel the Midianite, father-in-law of Moses: Setting forward, are we unto the place of which Yahweh hath said, The same, will I give unto you, —Oh come with us and we will do thee good, for, Yahweh, hath spoken good, concerning Israel.
Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”
30 And he said unto him, I will not go, —but unto my own land, and unto my own kindred, will I go.
Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”
31 Then said he: I beseech thee, do not forsake us, —for, on this account, hast thou come to know of our encamping in the desert, so shalt thou be unto us as eyes;
Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu.
32 and it shall be if thou wilt go with us, —yea it shall be that with the very good wherewith Yahweh shall do us good, will we do good unto thee.
Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”
33 So then they went forward, from the mountain of Yahweh, a journey of three days, —and the ark of the covenant of Yahweh, was going before them a journey of three days, to search out for them a resting-place,
Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo.
34 And the cloud of Yahweh, was over them by day, —when they set forward out of the camp.
Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.
35 And it came to pass when the ark set forward, that Moses said: Arise, O Yahweh! and scattered be thy foes, Let them that hate thee flee before thee;
Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti, “Dzukani, Inu Yehova! Adani anu abalalike; Odana nanu athawe pamaso panu.
36 But when it rested, he said, —Return, O Yahweh! unto the myriads of the thousands of Israel.
“Pamene likupumula, ankanena kuti, “Bwererani, Inu Yehova, ku chinamtindi cha Aisraeli.”

< Numbers 10 >