< Nehemiah 3 >

1 Then arose Eliashib the high priest and his brethren the priests, and built the sheep-gate, they, hallowed it, and set up the doors thereof, —even unto the tower of Hammeah, hallowed they it, unto the tower of Hananel;
Pambuyo pake Eliyasibu mkulu wa ansembe ndi ansembe anzake anayamba kugwira ntchito ndipo anamanganso Chipata cha Nkhosa. Iwo anachipatulira Mulungu ndipo anayika zitseko zake. Khoma limene analipatula linafika mpaka pa Nsanja ya Zana ndi Nsanja ya Hananeli.
2 and, at his hand, built, the men of Jericho, —and at his [other] hand built Zaccur, son of Imri.
Anthu a ku Yeriko anamanga chigawo china pambali pake ndipo Zakuri mwana wa Imuri anamanga chigawo chinanso choyandikana nawo.
3 And, the fish-gate, did the sons of Hassenaah build, —they, laid the beams thereof, and set up the doors thereof, the locks thereof, and the bars thereof;
Chipata cha Nsomba chinamangidwanso ndi ana a fuko la Hasena. Iwo anayika mitanda yake ndi zitseko, zotsekera zake, ndi mipiringidzo yake.
4 and, at their hand, repaired, Meremoth son of Uriah son of Hakkoz, and, at their hand, repaired, Meshullum son of Berechiah son of Meshezabel, —and, at their hand, repaired, Zadok son of Baana;
Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi, anakonza chigawo choyandikana nacho. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya, mwana wa Mesezabeli anakonza chigawo china. Pambali pake, Zadoki mwana wa Baana anakonzanso chigawo china.
5 and, at their hand, repaired, the Tekoites, —but, their chiefs, put not their neck into the service of their lords.
Pambali pa iwowa anthu a ku Tekowa anakonza chigawo china. Koma wolemekezeka awo anakana kugwira ntchito imene akuluakulu awo anawapatsa.
6 And, the old gate, did Joiada son of Paseah, and Meshullam, son of Besodeiah, repair, —they, laid the beams thereof, and set up the doors thereof, and the locks thereof, and the bars thereof;
Chipata cha Yesana chinakonzedwa ndi Yoyada mwana wa Paseya ndi Mesulamu mwana wa Besodeya. Iwo anayika mitanda yake ndi kuyika zitseko, zotsekera zake ndi mipiringidzo yake.
7 and, at their hand, repaired, Melatiah the Gibeonite and Jadon the Meronothite, men of Gibeon and of Mizpah, —who pertained to the throne of the pasha Beyond the River;
Pambali pawo Melatiya Mgibeyoni ndi Yadoni Mmerenoti ndiponso anthu a ku Gibiyoni ndi a ku Mizipa anakonza chigawo chawo mpaka ku nyumba ya bwanamkubwa wa chigawo cha Patsidya pa Yufurate.
8 at his hand, repaired, Uzziel son of Harhaiah, goldsmiths, and, at his hand, repaired Hananiah son of the perfumers, —and they fortified Jerusalem, as far as the broad wall;
Pambali pawo Uzieli mwana wa Harihaya wa mʼgulu amisiri osula golide anakonzanso chigawo china. Pambali pake Hananiya mmodzi mwa anthu oyenga mafuta onunkhira, anakonzanso chigawo china. Iwo anakonzanso Yerusalemu mpaka ku Khoma Lotambasuka.
9 and, at their hand, repaired, Rephaiah son of Hur, ruler of a half-circuit of Jerusalem;
Refaya mwana wa Huri wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu anakonza chigawo china motsatana nawo.
10 and, at their hand, repaired, Jedaiah son of Harumaph, even over against his own house, —and, at his hand, repaired, Hattush, son of Hashabneiah;
Kulumikiza ichi, Yedaya mwana wa Harumafi anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba yake, ndipo Hatusi mwana wa Hasabaneya anakonzanso motsatana naye.
11 a second length, did Malchijah son of Harim and Hasshub son of Pahath-moab, repair, —also the tower of the ovens;
Malikiya mwana wa Harimu ndi Hasubu mwana wa Pahati-Mowabu anakonzanso chigawo china ndiponso Nsanja ya Ngʼanjo.
12 and, at his hand, repaired, Shallum son of Hallohesh, ruler of a half-circuit of Jerusalem, —he and his daughters.
Salumu mwana wa Halohesi wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu, anakonzanso chigawo chotsatana nawo mothandizidwa ndi ana ake akazi.
13 The valley-gate, did Hanun and the inhabitants of Zanoah, repair, —they, built it, and set up the doors thereof, the locks thereof, and the bars thereof, —also a thousand cubits in the wall, as far as the dung-gate.
Chipata cha ku chigwa chinakonzedwa ndi Hanuni ndi anthu okhala ku Zanowa. Iwo anachimanganso ndi kuyika zitseko zake ndi zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iwo anakonzanso khoma lotalika mamita 450 mpaka ku Chipata cha Zinyalala.
14 And, the dung-gate, did Malchijah son of Rechab, ruler of the circuit of Beth-haccherem, repair, —he, built it, and set up the doors thereof, he locks thereof, and the bars thereof.
Chipata cha Zinyalala chinakonzedwa ndi Malikiya mwana wa Rekabu, wolamulira chigawo cha Beti-Hakeremu. Iye anachimanganso ndi kuyika zitseko zake, zotsekera zake ndi mipiringidzo.
15 And, the fountain-gate, did Shallun son of Col-hozeh ruler of the circuit of Mizpah, repair, he, built it, and covered it, and set up the doors thereof, the locks thereof, and the bars thereof, —also the wall of the pool of Shelah, by the garden of the king, even as far as the stairs that go down from the city of David;
Chipata cha Kasupe chinakonzedwa ndi Saluni mwana wa Koli-Hoze, wolamulira chigawo cha Mizipa. Iye anachimanganso ndi kuyikanso denga ndiponso zitseko, zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iye anakonzanso khoma la Dziwe la Siloamu limene lili pafupi ndi munda wa mfumu mpaka ku makwerero otsikira potuluka mzinda wa Davide.
16 after him, repaired, Nehemiah son of Azbuk, ruler of the half-circuit of Beth-zur, —as far as over against the sepulchres of David, even unto the pool which had been made, and unto the house of heroes;
Pambali pa iyeyo, Nehemiya mwana wa Azibuki, wolamulira theka la chigawo cha Beti Zuri anakonza chigawo china mpaka kumalo oyangʼanana ndi manda a Davide, mpaka ku dziwe lokumba ndi ku nyumba ya anthu ankhondo.
17 after him, repaired, the Levites, Rehum son of Bani, —at his hand, repaired, Hashabiah, ruler of the half-circuit of Keilah, for his circuit;
Pambali pake Alevi anakonza chigawo china, ndipo mtsogoleri wawo anali Rehumi mwana wa Bani. Pambali pa iye Hasabiya wolamulira theka la chigawo cha Keyila anagwira ntchito ku chigawo chake.
18 after him, repaired, their brethren, Bavvai son of Henadad, —ruler of the [other] half-circuit of Keilah;
Pambuyo pa iyeyu abale awo anapitiriza kukonza, ndipo mtsogoleri wawo anali Bawai mwana wa Henadadi, wolamulira theka lina la chigawo cha Keyila.
19 and there repaired at his hand, Ezer son of Jeshua, ruler of Mizpah, a second length, —over against the ascent of the armoury, at the corner;
Motsatana naye Ezeri mwana wa Yesuwa, wolamulira Mizipa anakonza chigawo chinanso choyangʼanana ndi chikweza chofikira ku nyumba yosungira zida za nkhondo pa ngodya.
20 after him, zealously repaired Baruch son of Zabbai, a second length, —from the corner, unto the opening of the house of Eliashib, the high priest;
Motsatana naye, Baruki mwana wa Zakai anakonzanso chigawo china kuchokera pa ngodya mpaka pa chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mkulu wa ansembe.
21 after him, repaired, Meremoth son of Uriah son of Hakkoz, a second length, —from the opening of the house of Eliashib, even unto the end of the house of Eliashib;
Motsatana naye, Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi anakonzanso chigawo china kuchokera ku chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mpaka kumapeto kwake.
22 and, after him, repaired, the priests, the men of the Circuit;
Pambuyo pake ansembe okhala ku chidikha anakonzanso chigawo china.
23 after him, repaired, Benjamin and Hasshub, over against their own house, —after him, repaired, Azariah son of Maaseiah son of Ananiah, beside his own house;
Pambuyo pawo, Benjamini ndi Hasubu anakonza kutsogolo kwa nyumba zawo. Ndipo motsatana nawo, Azariya mwana wa Maaseya mwana wa Ananiya, anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba zawo.
24 after him, repaired, Binnui son of Henadad, a second length, —from the house of Azariah, unto the corner, even unto the pinnacle:
Motsatana naye, Binuyi mwana wa Henadadi anakonzanso chigawo china, kuchokera pa nyumba ya Azariya kukafika potsirizira pa ngodya.
25 Palal, son of Uzai, from over against the corner, and the tower that projecteth from the upper house of the king, which belongeth to the court of custody, —after him, Pedaiah son of Parosh.
Palali mwana Uzai anakonza chigawo china choyangʼanana ndi ngodya ndi nsanja yotuluka pa nyumba yapamwamba ya mfumu ku bwalo la alonda. Motsatana naye, Pedaya mwana wa Parosi,
26 Now, the Nethinim, were dwelling in Ophel, —as far as over against the water-gate, on the east, and the tower that projecteth;
ndi otumikira mʼNyumba ya Mulungu amene amakhala pa khoma la Ofeli anakonza chigawo china mpaka pa malo oyangʼanana ndi Chipata cha Madzi kuloza kummawa ndiponso nsanja yayitali ija.
27 after him, repaired, the Tekoites, a second length, —from over against the great tower that projecteth, even unto the wall of Ophel:
Motsatana nawo, anthu a ku Tekowa anakonzanso chigawo china choyangʼanana ndi nsanja ija yayikulu ndi yayitali mpaka ku khoma la Ofeli.
28 from beside the horse-gate, repaired the priests, every one over against his own house;
Kuyambira ku Chipata cha Akavalo anakonza ndi ansembe ena ndipo aliyense amakonza khoma loyangʼanana ndi nyumba yake.
29 after him, repaired, Zadok son of Immer, over against his own house, —and, after him, repaired, Shemaiah son of Shecaniah, keeper of the east-gate;
Motsatana nawo, Zadoki mwana wa Imeri anakonza chigawo china choyangʼanana ndi nyumba yake. Motsatana naye, Semeya mwana wa Sekaniya, mlonda wa Chipata cha Kummawa, anakonzanso khoma.
30 after him, repaired, Hananiah son of Shelemiah, and Hanun sixth son of Zalaph, a second length, —after him, repaired, Meshullam son of Berechiah, over against his chamber;
Hananiya mwana wa Selemiya ndiponso Hanuni mwana wachisanu ndi chimodzi wa Zalafi anakonza chigawo china. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya anakonza chigawo choyangʼanana ndi chipinda chake.
31 after him, repaired, Malchijah son of Zorphi, as far as the house of the Nethinim, and the traders, —over against the muster-gate, even unto the ascent of the pinnacle;
Motsatana naye, Malikiya mmodzi mwa amisiri a golide anakonza chigawo china mpaka ku nyumba ya atumiki a ku Nyumba ya Mulungu ndiponso ku nyumba ya anthu amalonda moyangʼanana ndi chipata cha Mifikade ndiponso mpaka pa chipinda chapamwamba chapangodya.
32 and, between the ascent of the pinnacle and the sheep-gate, repaired, the goldsmiths, and the traders.
Ndipo pakati pa chipinda chapamwamba chapangodya ndi Chipata cha Nkhosa anakonza ndi amisiri a golide ndi anthu amalonda.

< Nehemiah 3 >