< Leviticus 13 >

1 And Yahweh spake unto Moses and unto Aaron, saying—
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
2 When, any man, shall have—in the skin of his flesh—a rising, or a scab, or a bright spot, and it shall become in the skin of his flesh the plague-spot of leprosy, then shall he be brought in unto Aaron the priest, or unto one of his sons the priests;
“Munthu akakhala ndi chithupsa, kapena mʼbuko, kapena chikanga pa thupi lake chimene chitha kusanduka nthenda ya khate, abwere naye munthuyo kwa Aaroni wansembe kapena kwa mmodzi mwa ana ake amene ndi ansembe.
3 and the priest shall view the spot in the skin of his flesh—if, the hair in the plague, have turned white and the appearance of the spot be deeper than the skin of his flesh, the plague-spot of leprosy, it is, —so the priest shall view him and pronounce him unclean.
Tsono wansembe ayangʼanitsitse nthendayo pa khungupo, ndipo ngati ubweya wa pamalo pamene pali nthendapo wasanduka woyera, komanso kuti nthendayo yazama mʼkati kupitirira khungu, ndiye kuti nthendayo ndi khate. Wansembe akamuonetsetsa alengeze kuti ndi wodetsedwa.
4 But, if the bright spot, though white in the skin of his flesh, is not deeper in appearance than the skin, and, the hair, hath not turned white, then shall the priest shut up the plagued one, seven days.
Ngati chikanga cha pa khungulo chikuoneka choyera, ndipo kuya kwake sikukuonekera kuti kwapitirira khungu ndi ubweya wake pamalopo sunasanduke woyera, wansembe amuyike wodwalayo padera kwa masiku asanu ndi awiri.
5 And the priest shall view him on the seventh day, and lo! if the spot hath stayed to his sight, and the spot hath not spread in the skin, then shall the priest shut him up seven days more,
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso bwino wodwalayo. Ndipo ngati waona kuti nthendayo sinasinthe ndipo sinafalikire pa khungu, amuyikenso wodwalayo padera kwa masiku ena asanu ndi awiri.
6 Then shall the priest view him on the seventh day, a second time, and lo! if the spot is, faint, and the spot hath not spread in the skin, then shall the priest pronounce him clean—it is, a scab, and he shall wash his clothes, and be clean.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembeyo amuonenso bwino munthuyo, ndipo ngati nthendayo yazima ndi kusafalikira pa khungu, wansembe amutchule munthuyo kuti ndi woyera. Umenewo unali mʼbuko chabe. Choncho munthuyo achape zovala zake ndipo adzakhala woyera.
7 But if the scab shall have, verily spread, in the skin, since he was shown to the priest that he might be cleansed, then shall he shew himself again unto the priest;
Koma ngati mʼbukowo ufalikira pakhungu atakadzionetsa kale kwa wansembe ndipo wansembeyo nʼkulengeza kuti munthuyo ndi woyeretsedwa, ndiye kuti apitenso kukadzionetsa kwa wansembeyo.
8 and the priest shall take a view, and lo! if the scab hath spread in the skin, then shall the priest pronounce him unclean—leprosy, it is.
Wansembe amuonetsetsenso munthuyo, ndipo ngati mʼbukowo wafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa ndi kuti nthendayo ndi khate.
9 When, the plague of leprosy, cometh to be in any human being, then shall he be brought in unto the priest;
“Ngati munthu aliyense ali ndi nthenda ya pakhungu yoyipitsa thupi, wodwalayo abwere naye kwa wansembe.
10 and the priest shall take a view, and lo! if there is a white rising in the skin and, the same, hath turned the hair white, —and there be a wound of raw flesh in the rising,
Wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati ali ndi chithupsa chamaonekedwe woyera pa khungupo chimene chasandutsa ubweya wa pamalopo kukhala woyera, ndipo ngati pali zilonda pa chotupacho,
11 an old leprosy, it is in the skin of his flesh, and the priest shall pronounce him unclean, —he shall not shut him up, for unclean, he is.
limenelo ndi khate lachikhalire la pa khungu, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Asamutsekere munthu woteroyo pakuti ndi wodetsedwa kale.
12 But, if the leprosy, cometh quite out, in the skin, and the leprosy covereth all the skin of him that, is plagued, from his head even unto his feet, —so far as appeareth to the eyes of the priest,
“Ndipo ngati, mʼkuona kwa wansembe, khate lija lafalikira pa khungu lonse moti lamugwira thupi lonse kuyambira kumutu mpaka kumapazi,
13 then shall the priest takes view and lo! if the leprosy hath covered all his flesh, then shall he pronounce clean him that was plagued, —all of it, hath turned white, clean, he is.
wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati khatero lagwira thupi lake lonse, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Popeza kuti thupi lonse lasanduka loyera, munthuyo ndi woyeretsedwa.
14 But, the very day there appeareth in him raw flesh, he shall be unclean;
Koma pa tsiku limene zilonda zidzaoneka pa iye, munthuyo adzakhala wodetsedwa.
15 so then the priest shall view the raw flesh, and pronounce him unclean, —as for the raw flesh, unclean, it is, leprosy, it is.
Wansembe aonetsetse zilondazo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zilondazo ndi zodetsedwa ndipo ili ndi khate.
16 Or, if the raw flesh turn again and be changed to white, then shall he come in unto the priest;
Koma zilondazo zikasinthika ndi kusanduka zoyera, munthuyo ayenera kupita kwa wansembe.
17 and the priest shall view him, and lo! if the spot hath changed to white, then shall the priest pronounce clean him that was plagued—clean, he is.
Wansembe amuonetsetse ndipo ngati zilondazo zasanduka zoyera, wansembe amutchule wodwalayo kuti ndi woyera ndipo adzakhala woyera ndithu.
18 And, when, any one’s flesh, hath, in the skin thereof, a boil, —and then it is healed;
“Ngati pa khungu la munthu wodwalayo pali chithupsa chimene chinapola kale,
19 but in the place of the boil, is a white rising, or a bright spot, reddish white, then shall it be shown unto the priest.
ndipo pamalo pamene panali chithupsacho pakatuluka chotupa choyera kapena banga loyera mofiirira, munthuyo ayenera kukadzionetsa kwa wansembe.
20 And the priest shall take a view and lo! if the appearance thereof, is lower than the skin, and, the hair thereof, hath turned white, then shall the priest pronounce him unclean—the plague-spot of leprosy, it, is, in the boil, broken out.
Wansembe aonetsetse bwino ndipo ngati chikuoneka kuti chazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka woyera, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Imeneyo ndi nthenda ya khate imene yatuluka mʼchithupsacho.
21 But, if the priest shall view it and lo! there is no white hair therein, and it is not deeper than the skin, and, in itself, is faint, then shall the priest shut him up seven days;
Koma ngati wansembe waonetsetsa napeza kuti palibe ubweya woyera ndipo chithupsacho sichinazame, koma chazimirira, wansembeyo amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
22 and, if it, clearly spreadeth, in the skin, then shall the priest pronounce him unclean—a plague-spot, it is.
Ngati nthendayo ikufalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limeneli ndi khate.
23 But if in its place the bright spot stayeth hath not spread, a boil, it is, —and the priest shall pronounce him clean.
Koma bangalo likakhala malo amodzi, wosafalikira, chimenecho ndi chipsera cha chithupsacho, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera.
24 Or, when, any one’s flesh, hath in the skin thereof a fiery burning, —and the burning wound becometh a bright spot reddish white, or white,
“Munthu akakhala ndi bala lamoto pa khungu lake, ndipo chilonda cha balalo chikasanduka banga loyera mofiirira kapena loyera,
25 then shall the priest view it—and lo! if the hair is turned white in the bright spot and the appearance thereof is deeper than the skin, leprosy, it is, broken out, in the burning, —so the priest shall pronounce him unclean, the plague-spot of leprosy, it is.
wansembe aonetsetse bangalo, ndipo ngati ubweya wa pa bangapo usanduka woyera, ndipo balalo lioneka kuti ndi lozama, limenelo ndi khate lomwe latuluka pa balalo. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate la pa khungu.
26 But, if the priest shall view it and lo! there is not, in the bright spot white hair, and it is not deeper than the skin but, itself, is faint, then shall the priest shut him up seven days;
Koma ngati wansembe waonetsetsa balalo ndipo palibe ubweya woyera, ndipo ngati balalo silinazame ndi kuti lazirala, wansembe amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
27 and the priest shall view him on the seventh day, —if it, hath plainly spread in the skin, then shall the priest pronounce him unclean, the plague-spot of leprosy, it is.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso wodwalayo, ndipo ngati bangalo lafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate.
28 But, if, in its place the bright spot hath stayed, and hath not spread in the skin, but, itself, is faint, the rising of a burning, it is, —and the priest shall pronounce him clean, for only the inflaming of the burning, it is.
Koma ngati bangalo likhala pa malo amodzi wosafalikira pa khungu, ndipo lazimirira, limenelo ndi thuza la bala lamoto, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Chimenecho ndi chipsera chamoto.
29 And, when there cometh to be in, any man or woman, a spot, —in the head or in the beard,
“Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi nthenda kumutu kapena ku chibwano,
30 then shall the priest view the spot and lo! if, the appearance thereof, is deeper than the skin, and, therein, is yellow, thin hair, then shall the priest pronounce him unclean a scall, it is, a leprosy of the head or of the beard, it is.
wansembe aonetsetse balalo ndipo likaoneka kuti lazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka wachikasu ndi wonyololoka, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zimenezo ndi mfundu zonyerenyetsa, khate lakumutu kapena ku chibwano.
31 But when the priest vieweth the spot, and lo! there is, no appearance, of it deeper than the skin, and, no dark hair, is therein, then shall the priest shut up him that hath the plague-spot of scall, seven days;
Koma wansembe akaonetsetsa mfundu zonyerenyetsazo, ndipo zikaoneka kuti sizinazame ndi kuti palibe ubweya wakuda, wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku asanu ndi awiri.
32 and the priest shall view the spot on the seventh day, and lo! if the scall hath not spread, and there hath not come to be therein yellow hair, —and, the appearance of the scall, is not deeper than the skin,
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo, ndipo ngati sizinafalikire ndipo palibe ubweya wachikasu pamalopo ndiponso sizinazame,
33 then shall he shave himself, but the scall, shall he not shave, and the priest shall shut up him who hath the scall seven days, more;
wodwalayo ametedwe, koma pamene pali mfunduyo pasametedwe. Wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
34 then shall the priest view the scall, on the seventh day, and lo! if the scall hath not spread in the skin, and, the appearance thereof, is not deeper than the skin, then shall the priest pronounce him clean, and he shall wash his clothes, and be clean.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo ndipo ngati sizinafalikire pa khungu ndi kuti sizinazame, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Tsono achape zovala zake, ndipo adzakhala woyera.
35 But, if the scall do indeed spread in the skin, —after he hath been pronounced clean,
Koma mfundu zonyerenyetsazo zikafalikira pa khungu, wansembe atalengeza kuti ndi woyera,
36 then shall the priest take a view, and lo! if the scall hath spread in the skin, the priest shall not search for the yellow hair—unclean, he is.
wansembe amuonetsetsenso wodwalayo ndipo ngati mfunduzo zafalikira pa khungu, iye asalabadirenso zoyangʼana ngati ubweya uli wachikasu. Munthuyo ndi wodetsedwa.
37 But, if in his eyes, the scall is at a stay, and dark hair hath grown up therein, the scall is healed, clean, he is, —and the priest shall pronounce him clean.
Koma ngati wansembe waonetsetsa kuti mfunduzo sizinasinthe ndipo ubweya wakuda wamera pa mfundupo, ndiye kuti wodwalayo wachira. Tsono wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa.
38 And when either, man or woman, hath in the skin of their flesh bright spots, —bright spots that are white,
“Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi mawanga woyera pa khungu,
39 then shall the priest take a view and lo! if, in the skin of their flesh, are bright spots that are dull white, dead white spot, it is, that hath broken through in the skin—clean, he is.
wansembe aonetsetse mawangawo, ndipo ngati ali otuwa, ndiye kuti ndi mibuko chabe yotuluka pa khungu. Munthuyo ndi woyera.
40 And, when, any man’s, head loseth its hair, though, bald, he is, clean.
“Tsitsi la munthu likayoyoka kumutu ndiye kuti ndi dazi limenelo koma munthuyo ndi woyeretsedwa.
41 And if, in front, his head loseth its hair, though bald in the forehead, he is, clean.
Ngati tsitsi lake layoyoka chapamphumi ndiye kuti ndi dazi la pa chipumi limenelo koma munthuyo ndi woyera.
42 But, should there be, in the baldness behind, or in the baldness in front, a spot that is reddish white, leprosy broken out, it is, in his baldness behind, or in his baldness in front.
Koma ngati pa dazi la pamutu kapena la pa chipumi pakhala chithupsa choyera mofiirira, ndiye kuti ndi khate limenelo lochokera mu dazi la pamutu lija kapena pa chipumi lija.
43 So the priest shall view it, and lo! if, the rising-spot, be reddish white in his baldness behind or in his baldness in front, —like the appearance of leprosy in the skin of the flesh,
Tsono wansembe amuonetsetse wodwalayo ndipo ngati chithupsa cha pa dazi lapankhongo kapena pa dazi lapachipumicho ndi choyera mofiirira monga nthenda ya khate imaonekera,
44 a leprous man, is he, unclean, he is, —unclean, shall the priest pronounce him in his head, is his plague.
ndiye kuti munthuyo ali ndi khate, motero ndi wodetsedwa. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa chifukwa cha chithupsa cha pamutu pakepo.
45 Now, as for the leper in whom is the plague, His clothes, shall be rent, And, his head, shall be bare, And, his beard, shall he cover, —And, Unclean! Unclean! shall he cry.
“Munthu wa khate lotere avale sanza, tsitsi lake alilekerere, aphimbe mlomo wake wapamwamba ndipo azifuwula kuti, ‘Ndine wodetsedwa, ndine wodetsedwa!’
46 All the days that the plague is in him, shall he continue unclean, Unclean, he is, —Alone, shall he remain, Outside the camp, shall be his dwelling.
Munthu wodwalayo adzakhala wodetsedwa kwa nthawi yonse imene ali ndi nthendayo. Iye ayenera kumakhala payekha kunja kwa msasa.
47 And, when, in a garment, there is a plague-spot of leprosy, —whether in a garment of wool, or a garment of flax;
“Nsalu iliyonse ikakhala ndi nguwi,
48 either in warp or in weft, made with flax, or with wool, —or in a skin, or in anything wrought of skin;
kaya ndi chovala chopangidwa ndi nsalu yathonje kapena yaubweya, yoluka ndi thonje kapena ubweya, yachikopa kapena yopangidwa ndi chikopa,
49 and the spot cometh to be of a greenish yellow or reddish, in the garment or in the skin, whether in warp or in weft, or in any utensil of skin, the plague-spot of leprosy, it is, —and shall be shown unto the priest;
ndipo ngati pamalo pamene pachita nguwiyo pali ndi maonekedwe obiriwira kapena ofiirira imeneyo ndi nguwi yoyipitsa chovala ndipo chovalacho chikaonetsedwe kwa wansembe.
50 and the priest shall view the spot, —and shall shut up him that is plagued seven days;
Wansembeyo ayionetsetse nguwiyo ndipo chovalacho achiyike padera kwa masiku asanu ndi awiri.
51 then shall he view the spot, on the seventh day if the spot hath spread in the garment whether in warp or in weft, or in the skin, or anything which may be made of skin for service, the spot is a fretting leprosy, unclean, it is.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri ayionetsetsenso nguwiyo ndipo ngati nguwiyo yafalikira pa chovalacho, chathonje kapena chaubweya, kapena pa chikopacho, kaya ndi cha ntchito ya mtundu wanji, imeneyo ndi nguwi yoopsa ndipo chovalacho ndi chodetsedwa.
52 Then shall he burn up the garment whether it be in the warp or the weft in wool or in flax, or any utensil of skin, wherein shall be the plague-spot, —for, a fretting leprosy, it is, in fire, shall it be burnt up.
Wansembe atenthe chovala chathonje kapena chaubweya chija, ngakhalenso chinthu chachikopa chija popeza nguwiyo yachidetsa. Nguwiyo ndi yoopsa choncho chinthucho achitenthe.
53 But if the priest shall take a view, and lo! the spot has not spread, in the garment, either in warp or in weft, —or in any utensil of skin,
“Koma ngati wansembe akayangʼanitsitsa nguwiyo apeza kuti sinafalikire pa chovalacho kapena pa chinthu chilichonse chachikopa,
54 then shall the priest give command, and they shall wash that wherein is the spot, —and he shall shut it up seven days more;
iye alamulire kuti chinthu choyipitsidwacho achichape. Akatero achiyike padera kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
55 then shall the priest take a view after the plagued garment hath been washed and lo! if the spot hath not changed its look, then though the spot hath not spread, yet unclean, it is, in the fire, shalt thou burn it up, —a sunken spot, it is, in the back thereof, or in the front thereof.
Chovalacho chitachapidwa, wansembe achionenso ndipo ngati nguwiyo sinasinthe maonekedwe ake, ngakhale kuti sinafalikire, chovalacho ndi chodetsedwa ndithu. Muchitenthe, ngakhale kuti nguwiyo ili kumbuyo kapena kumaso kwa chinthucho.
56 And, if the priest hath taken a view, and lo! the spot is, faint, since it hath been washed, then shall he rend it out of the garment, or out of the skin, whether out of the warp or out of the weft;
Koma ngati wansembe aonetsetsa nʼkupeza kuti nguwi ija yathimbirira pa chovala chija kapena pa chinthu chachikopa chija atachichapa, ndiye angʼambeko chinthucho pa banga la nguwiyo.
57 and, if it appear still in the garment—either in the warp or in the weft, or in any utensil of skin, a breaking out, it is, —in the fire, shalt thou burn up that wherein is the plague.
Koma ngati nguwiyo iwonekanso pa chovala chathonje kapena chaubweya ndiye kuti nguwiyo ikufalikira. Chilichonse chimene chili ndi nguwi chiyenera kutenthedwa.
58 But, as for the garment—whether the warp or the weft or any utensil of skin which thou shalt wash, and the plague shall depart therefrom, then shall it be washed a second time, and shall be clean.
Chovala chathonje kapena chaubweya, ngakhale chinthu china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, mukachichapa nguwi yake nʼkuchoka muchichapenso kawiri ndipo chidzakhala choyeretsedwa.”
59 This, is the law as to the plague-spot of leprosy, in a garment of wool or of flax, whether in the warp or the weft, or in any utensil of skin, —To pronounce it clean, or to pronounce it unclean.
Amenewa ndiwo malamulo a nguwi yokhala pa chovala chaubweya kapena pa chovala chathonje, kapenanso pa chinthu chilichonse chopangidwa ndi chikopa kuti muzitha kulekanitsa choyeretsedwa ndi chodetsedwa.

< Leviticus 13 >