< Lamentations 3 >

1 I, am the man, that hath seen affliction, by the rod of his indignation;
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
2 Me, hath he driven out and brought into darkness, and not light;
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
3 Surely, against me, doth he again and again, turn his hand all the day.
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 He hath worn out my flesh and my skin, hath broken my bones;
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
5 He hath built up against me, and carried round me, fortifications and a trench;
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 In dark places, hath he made me sit, like the dead of age-past times.
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
7 He hath walled up around me, that I cannot get out, hath weighted my fetter;
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
8 Yea, when I make outcry and implore, he hath shut out my prayer;
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
9 He hath walled in my ways with hewn stone, my paths, hath he caused to wind back.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 A bear lying in wait, he is to me, a lion, in secret places;
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
11 My ways, hath he turned aside, and hath torn me in pieces, hath made me desolate;
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 He hath trodden his bow, and set me up, as a mark for the arrow.
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 He hath caused to enter my reins, the sons of his quiver;
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 I have become a derision to all my people, their song all the day;
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 He hath sated me with bitter things, hath drenched me with wormwood.
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
16 And he hath crushed, with gravel-stones, my teeth, hath made me cower in ashes;
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
17 And thou hast thrust away from welfare, my soul, I have forgotten prosperity;
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 And I said, Vanished is mine endurance, even mine expectation, from Yahweh.
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 Remember my humiliation and my fleeings, the wormwood and poison;
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 Thou wilt, indeed remember, that, bowed down concerning myself, is my soul;
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 This, will I bring back to my heart, therefore, will I hope.
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 The lovingkindnesses of Yahweh, verily they are not exhausted, Verily! not at an end, are his compassions:
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 New things for the mornings! Abundant is thy faithfulness:
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 My portion, is Yahweh, saith my soul, For this cause, will I wait for him.
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
25 Good is Yahweh, to them who wait for him, to the soul that will seek him;
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 Good it is—both to wait and to be silent, for the deliverance of Yahweh;
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
27 Good it is for a man, that he should bear the yoke in his youth.
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
28 Let him sit alone, and keep silence, because he took it upon himself:
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 Let him put, in the dust, his mouth, peradventure, there is hope!
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 Let him give, to him that smiteth him, his cheek, let him be sated with reproach.
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
31 Surely My Lord, will not cast off, unto times age-abiding;
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
32 Surely, though he cause grief, yet will he have compassion, according to the multitude of his lovingkindnesses;
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 Surely he hath not afflicted from his heart, nor caused sorrow to the sons of men.
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 To crush, under his feet, any of the prisoners of the earth;
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
35 To turn aside the right of a man, before the face of the Most High;
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
36 To oppress a son of earth in his cause, My Lord, hath made no provision.
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
37 Who was it that spake, and it was done, [when], My Lord, had not commanded?
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
38 Out of the mouth of the Most High, Proceed there not misfortunes and blessing?
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 Why should a living son of earth complain, [Let] a man [complain] because of his sins?
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40 Let us search out our ways, and examine them well, and let us return unto Yahweh;
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 Let us lift up our heart, to the opened palms, to the Mighty One in the heavens;
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 We, have trespassed and rebelled, Thou, hast not pardoned.
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
43 Thou hast covered thyself with anger, and pursued us, hast slain—hast not spared;
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
44 Thou hast screened thyself with the clouds, that prayer, should not pass through;
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 Offscouring and refuse, dost thou make us, in the midst of the peoples.
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
46 With their mouth, opened wide over us, [stand] all our foes.
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 Terror and a pit, have befallen us, tumult and grievous injury;
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 With streams of water, mine eye runneth down, over the grievous injury of the daughter of my people.
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49 Mine eye, poureth itself out and ceaseth not, without relief;
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
50 Until Yahweh out of the heavens shall look forth, and see,
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 Mine eye dealeth severely with my soul, because of all the daughters of my city.
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52 They, have laid snares, for me as a bird, who are mine enemies without cause:
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 They have cut off, in the dungeon, my life, and have cast a stone upon me;
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
54 Waters, flowed over, my head, I said, I am cut off!
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55 I have called upon thy Name, O Yahweh, out of the dungeon below;
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
56 My voice, thou hast heard, —do not close thine ear to my respite, to mine outcry;
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 Thou drewest near, in the day I kept calling on thee, thou saidst, Do not fear!
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
58 Thou hast pleaded, O My Lord, the pleas of my soul, hast redeemed my life;
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
59 Thou hast beheld, O Yahweh, my failure to get justice, Pronounce thou my sentence;
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
60 Thou hast seen all their vindictiveness, all their plots against me.
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
61 Thou hast heard their reproach, O Yahweh, all their plots against me;
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
62 The lips of mine assailants, and their mutterings, are against me, all the day;
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
63 On their downsitting and their uprising, do thou look, I, am their song.
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
64 Thou wilt render to them a recompense, O Yahweh, according to the work of their hands;
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 Thou wilt suffer them a veiling of heart, thy curse to them;
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 Thou wilt pursue in anger, and wilt destroy them, from under the heavens of Yahweh.
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.

< Lamentations 3 >