< Joshua 24 >

1 And Joshua gathered together all the tribes of Israel, unto Shechem, —and called for the elders of Israel, and for their heads, and for their judges, and for their officers, and they presented themselves before God.
Tsono Yoswa anasonkhanitsa mafuko onse a Israeli ku Sekemu. Iye anayitanitsa akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi akuluakulu a boma la Israeli, ndipo iwo anafika pamaso pa Mulungu.
2 Then said Joshua unto all the people—Thus, saith Yahweh, God of Israel, Beyond the River, dwelt your fathers from age-past times, [unto] Terah, father of Abraham, and father of Nahor, —and they served other gods.
Yoswa anati kwa anthu onse, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Kalekale makolo anu, kuphatikiza Tera, abambo a Abrahamu ndi Nahori ankakhala kutsidya kwa Mtsinje ndipo ankapembedza milungu ina.
3 So I took your father, Abraham, from beyond the River, and led him through all the land of Canaan, —and multiplied his seed, and gave unto him, Isaac;
Koma ine ndinatenga kholo lanu Abrahamu kumuchotsa ku dziko la kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndipo ndinamutsogolera kupita ku dziko la Kanaani. Ndinamupatsa zidzukulu zambiri. Ndinamupatsa Isake,
4 and gave unto Isaac Jacob and Esau, —and gave unto Esau, Mount Seir, to possess it, but, Jacob and his sons, went down into Egypt.
ndipo Isake ndinamupatsa Yakobo ndi Esau. Ndinapereka dziko la mapiri la Seiri kwa Esau, koma Yakobo ndi ana ake anapita ku Igupto.
5 Then sent I Moses and Aaron, and plagued Egypt, according to that which I did in their midst, and, afterwards, brought you forth.
“‘Kenaka ndinatuma Mose ndi Aaroni, ndipo ine ndinazunza Aigupto. Pambuyo pake ndinakutulutsani.
6 Yea I brought forth your fathers, out of Egypt, and ye came unto the sea, and the Egyptians pursued after your fathers, with chariots and with horsemen, unto the Red Sea.
Nditatulutsa makolo anu ku Igupto ndinafika nawo ku Nyanja Yofiira. Aigupto anawathamangira ndi magaleta ndi okwera pa akavalo mpaka ku Nyanja Yofiira.
7 So they made outcry unto Yahweh, and he put darkness between you and the Egyptians, and brought in upon them the sea, and covered them, —and your eyes beheld what I did with the Egyptians. And, when ye had remained in the desert many days,
Tsono makolo anuwo anapemphera kwa Ine kuti ndiwathandize, ndipo ndinayika mtambo wakuda pakati pawo ndi Aiguptowo, ndipo Nyanja inamiza Aigupto aja. Inu munaona ndi maso anu zimene ndinachita kwa Aiguptowo ndipo inu munakhala mʼchipululu nthawi yayitali.
8 then I brought you into the land of the Amorites, who were dwelling over the Jordan, and they fought with you, —then delivered I them into your hand, and ye took possession of their land, so I destroyed them from before you.
“‘Pambuyo pake Ine ndinabwera nanu ku dziko la Aamori amene amakhala kummawa kwa Yorodani. Iwo anamenyana nanu koma ndinawapereka mʼdzanja lanu. Ndinawawononga pamaso panu, ndipo inu munalanda dziko lawo.
9 Then rose up Balak, son of Zippor, king of Moab, and made war with Israel, —and sent and called for Balaam son of Beor, to curse you;
Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, analimbana ndi Israeli. Iye anayitanitsa Balaamu mwana wa Beori kuti akutemberereni.
10 but I was not willing to hearken unto Balaam, —so, he kept on blessing, you, and I rescued you out of his hand.
Koma ine sindinamvere Balaamu, kotero iye anakudalitsani mowirikiza ndipo ndinakulanditsani mʼdzanja lake.
11 Then passed ye over the Jordan, and came in unto Jericho, and, when they would have made war with you—even the lords of Jericho—the Amorite and the Perizzite and the Canaanite and the Hittite and the Girgashite, the Hivite and the Jebusite, then delivered I them into your hand.
“‘Ndipo inu munawoloka Yorodani ndi kufika ku Yeriko. Anthu a ku Yeriko analimbana nanu pamodzi ndi Aamori, Aperezi, Akanaani, Ahiti, Agirigasi, Ahivi ndi Ayebusi. Koma Ine ndinawapereka mʼdzanja lanu.
12 And I sent before you the hornet, which drave them out from before you, the two kings of the Amorites, —not with thy sword, nor with thy bow.
Ine ndinatumiza mavu amene anapirikitsa mafumu awiri Aamori aja pamaso panu. Inu simunachite izi ndi lupanga ndi uta wanu.
13 Thus I gave unto you a land on which thou hadst not laboured, and cities which ye had not built, and ye proceeded to dwell therein, —of vineyards and oliveyards, which ye planted not, ye are eating.
Motero ndinakupatsani dziko limene simunalivutikire ndiponso mizinda imene simunamange. Inu mukukhala mʼmenemo ndi kumadya zipatso za mʼmunda wamphesa ndi kuthyola zipatso mʼmitengo ya olivi zimene simunadzale.’
14 Now, therefore, revere ye Yahweh, and serve him, in sincerity and in truth, —and put away the gods which your fathers served beyond the River, and in Egypt, and serve ye Yahweh.
“Ndipo tsopano wopani Yehova ndi kumutumikira Iye mokhulupirika ndi moona. Chotsani milungu imene makolo anu ankapembedza kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndi ku Igupto ndipo tumikirani Yehova.
15 But, if it be, a vexation, in your eyes, to serve Yahweh, choose ye for yourselves, to-day, whom ye will serve, whether the gods which your fathers served, that were beyond the River, or the gods of the Amorites, in whose land ye are dwelling, —but, I and my house, will serve Yahweh.
Koma ngati kutumikira Yehova kukuyipirani, sankhani lero amene mudzamutumikire, kapena milungu imene makolo anu ankayitumikira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, kapena milungu ya Aamori, amene mukukhala mʼdziko lawo. Koma ine ndi banja langa, tidzatumikira Yehova.”
16 Then responded the people, and said, Far be it from us, that we should forsake Yahweh, —to serve other gods;
Ndipo anthu anayankha, “Sizingatheke kuti timusiye Yehova ndi kutumikira milungu ina!
17 for, as for Yahweh our God, he, brought up both us and our fathers, out of the land of Egypt, out of the house of servants, —and who did before our eyes, these great signs, and preserved us throughout all the way wherein we journeyed, and among all the peoples through the midst of whom we passed;
Yehova Mulungu wathu ndiye amene anatitulutsa ife ndi makolo athu mu ukapolo, mʼdziko la Igupto. Tinaona ndi maso athu zizindikiro zozizwitsa zimene anachita. Iye anatiteteza pa ulendo wathu wonse ndi pakati pa mitundu yonse imene tinkakumana nayo.
18 then did Yahweh drive out all the peoples, even the Amorites were dwelling in the land, from before us, —we too, will serve Yahweh, for, he, is our God.
Ife tikufika Iye anapirikitsa anthu onse pamodzi ndi Aamori amene ankakhala mʼdzikoli. Ifenso tidzatumikira Yehova chifukwa Iye ndiye Mulungu.”
19 Then said Joshua unto the people—Ye cannot serve Yahweh, for, a holy God, he is, a jealous GOD, he is, he will not forgive your transgression, nor your sins.
Koma Yoswa anati kwa anthuwo, “Inutu simungathe kutumikira Yehova. Iye ndi Mulungu woyera, salola kupikisana naye. Sadzakukhululukirani ngati mumuwukira ndi kumuchimwira.
20 When ye forsake Yahweh, and serve the gods of a stranger, then will he turn, and inflict on you calamity, and consume you, after that he hath dealt well with you.
Ngati inu musiya Yehova ndi kutumikira milungu yachilendo, adzakufulatirani. Iye adzakulangani ndi kukuwonongani ngakhale kuti poyamba anakuchitirani zabwino.”
21 But the people said unto Joshua, —Nay! but, Yahweh, will we serve.
Koma anthuwo anati kwa Yoswa, “Ayi! Ife tidzatumikira Yehova.”
22 Then said Joshua unto the people—Witnesses, are ye, against yourselves, that, ye yourselves, have chosen you Yahweh, to serve him. And they said: Witnesses!
Kenaka Yoswa anati, “Inu mukudzichitira nokha umboni kuti mwasankha kutumikira Yehova.” Iwo anayankha kuti, “Inde ife ndife mboni.”
23 Now, therefore, put ye away the gods of the stranger, that are in your midst, —and incline your heart unto Yahweh, God of Israel.
Yoswa anati, “Tsono chotsani milungu yachilendo imene ili pakati panu ndipo perekani mitima yanu kwa Yehova Mulungu wa Israeli.”
24 And the people said unto Joshua, —Yahweh our God, will we serve, and, unto his voice, will we hearken.
Ndipo anthuwo anati kwa Yoswa, “Ife tidzatumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera Iye.”
25 So then Joshua solemnised a covenant for the people, on that day, —and set for them a statute and a regulation, in Shechem.
Choncho pa tsiku limenelo Yoswa anachita pangano mʼmalo mwa anthuwo, ndipo pa Sekemu pomwepo iye anapereka malamulo ndi malangizo kwa anthu aja.
26 And Joshua wrote these words in the scroll of the law of God, —and took a great stone, and set it up there, under the oak that was by the sanctuary of Yahweh.
Ndipo Yoswa analemba zinthu izi mʼbuku la malamulo a Mulungu. Kenaka iye anatenga mwala waukulu nawuyimika pansi pa mtengo wa thundu pa malo wopatulika a Yehova.
27 And Joshua said unto all the people—Lo! this stone, shall serve against us as a witness, for, it, hath heard all the sayings of Yahweh, which he hath spoken with us, —so shall it serve against you as a witness, lest ye should act deceptively against your God.
Yoswa anati kwa anthu onse, “Tamvani! Mwala uwu udzakhala mboni yotitsutsa. Mwalawu wamva mawu onse amene Yehova wayankhula kwa ife. Udzakhala mboni yotitsutsa ngati mukhala osakhulupirika kwa Mulungu wanu.”
28 And Joshua sent the people away, every man unto his inheritance.
Kenaka Yoswa analola anthu kuti apite, aliyense ku dera lake.
29 And it came to pass, after these things, that Joshua son of Nun, servant of Yahweh, died, being a hundred and ten years old.
Zitatha zinthu izi, Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110,
30 And they buried him within the bounds of his own inheritance, in Timnath-serah, which is in the hill country of Ephraim, on the north of Mount Gaash.
ndipo anamuyika mʼmanda mʼdziko lake, ku Timnati-Sera dziko lamapiri la ku Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
31 So then Israel served Yahweh all the days of Joshua, —and all the days of the elders who prolonged their days after Joshua, and who had known all the work of Yahweh, which he had wrought for Israel.
Israeli anatumikira Yehova pa nthawi yonse imene Yoswa anali ndi moyo ndiponso pa nthawi ya akuluakulu amene anali moyo Yoswa atamwalira, anthu amene ankadziwa zonse zimene Yehova anachitira Israeli.
32 And, the bones of Joseph—which the sons of Israel had brought up out of Egypt, buried they in Shechem, in the portion of field, which Jacob bought of the sons of Hamor, father of Shechem, for a hundred pieces of money, —and they belonged unto the sons of Joseph, as an inheritance.
Ndipo mafupa a Yosefe amene Aisraeli anawatulutsa ku Igupto anawayika mʼmanda a ku Sekemu pa malo amene Yakobo anagula ndi ndalama zasiliva 100 kwa ana a Hamori, abambo a Sekemu. Malo awa anakhala cholowa cha adzukulu a Yosefe.
33 And, Eleazar son of Aaron, died, —and they buried him in the hill of Phinehas his son, which was given to him, in the hill country of Ephraim.
Ndipo Eliezara mwana wa Aaroni anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda ku Gibeya, malo amene anapatsidwa kwa Finehasi mwana wake, mʼdziko lamapiri la Efereimu.

< Joshua 24 >