< Genesis 16 >

1 But Sarai, Abram’s wife, had borne him no children, —she had, however, an Egyptian handmaid, whose name was Hagar.
Tsono Sarai, mkazi wa Abramu anali asanamuberekere ana Abramuyo. Koma anali ndi wantchito wamkazi wa ku Igupto dzina lake Hagara;
2 So then Sarai said unto Abram Behold, I pray thee, Yahweh hath restrained me, from bearing, go in I pray thee unto, my handmaid, peradventure I may be built up from, her, And Abram hearkened to the voice of Sarai.
ndipo Sarai anati kwa Abramu, “Yehova sanalole kuti ine ndikhale ndi ana. Bwanji mulowe mwa wantchito wanga wamkaziyu kuti mwina ndingaone ana kudzera mwa iyeyu.” Abramu anamvera Sarai.
3 So Sarai, Abram’s wife, took Hagar the Egyptian. her handmaid, at the end of ten years of Abram’s dwelling in the land of Canaan, and gave her to Abram her husband, to be to him as a wife.
Tsono Sarai anatenga Hagara wantchito wake wamkazi wa ku Igupto uja namupereka kwa Abramu mwamuna wake kuti akhale mkazi wake. Izi zinachitika Abramu atakhala ku Kanaani zaka khumi.
4 And he went in unto Hagar and she conceived, —and when she saw that she had conceived, lightly esteemed, was her lady, in her eyes.
Abramu atalowana ndi Hagara, Hagara uja anatenga mimba. Pamene Hagara anadziwa kuti anali woyembekezera anayamba kunyoza mbuye wake Sarai.
5 Then said Sarai unto Abram: My wrong, is, on thee! I, gave my handmaid into thy bosom, and when she seeth that she hath conceived, then am I lightly esteemed in her eyes Yahweh judge betwixt me and her.
Pamenepo Sarai anati kwa Abramu, “Inu ndinu amene mwandiputira nkhanza zikundichitikirazi. Ndinakupatsani wantchito wanga wamkazi kuti akhale mkazi wanu, ndiye tsopano wayamba kundinyoza ine chifukwa wadziwa kuti ndi woyembekezera. Yehova ndiye amene aweruze pakati pa inu ndi ine.”
6 And Abram said unto Sarai, Lo! thy handmaid, is in thy hand, do to her what is good in thine eyes. So Sarai humbled her, and she fled from her face.
Abramu anati, “Wantchito wakoyu ali mʼmanja mwako. Chita naye chilichonse chimene ukuganiza kuti ndi chokukomera.” Tsono Sarai anazunza Hagara mpaka anathawa.
7 And the messenger of Yahweh found her by the fountain of water in the desert, —by the fountain in the way to Shur.
Mngelo wa Yehova anamupeza Hagara pafupi ndi chitsime mʼchipululu. Chinali chitsime chimene chili mʼmphepete mwa msewu wopita ku Suri.
8 So he said Hagar! handmaid of Sarai! Whence hast thou come, and whither wouldst thou go? And she said, From the face of Sarai, my lady, am, I, fleeing.
Ndipo mngeloyo anati, “Hagara, iwe wantchito wa Sarai, ukuchokera kuti ndipo ukupita kuti?” Iye anayankha, “Ndikuthawa mbuye wanga Sarai.”
9 And the messenger of Yahweh said to her, Return unto thy lady, —and humble thyself under her hands.
Mngelo wa Yehova anamuwuza kuti, “Bwerera kwa mbuye wako ndipo ukamugonjere.
10 And the messenger of Yahweh said to her, I will, greatly multiply, thy seed—so that it shall not be numbered for multitude.
Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri zoti munthu sangaziwerenge.”
11 And the messenger of Yahweh said to her, Behold thee! with child, and about bearing a son—and thou shalt call his name Ishmael ["God hearkeneth"] for Yahweh hath hearkened unto thy humiliation.
Mngelo wa Yehova uja anamuwuzanso kuti, “Ndiwe woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna. Udzamutcha dzina lake Ismaeli, pakuti Yehova wamva kulira chifukwa cha kuzunzika kwako.
12 But, he, will be a wild ass of a man, his hand, against every one, and every one’s hand against him—yet, in presence of all his brethren, shall he have his habitation.
Iye adzakhala munthu wa khalidwe ngati mʼmbulu wamisala; adzadana ndi aliyense ndipo anthu onse adzadana naye, adzakhala mwaudani pakati pa abale ake onse.”
13 And she called the name of Yahweh, who had spoken unto her, Thou GOD of vision! For she said. Do I even here, retain my vision after a vision?
Hagara anatcha Yehova amene anamuyankhula uja dzina loti: “Ndinu Mulungu amene mumandiona,” popeza anati, “Ndakumana ndi Yehova atatha kundikomera mtima.”
14 On this account, is the well called, the well of the life of vision, lo! it is between Kadesh and Bered.
Nʼchifukwa chake chitsime chija chimene chili pakati pa Kadesi ndi Beredi chinatchedwa Beeri-lahai-roi.
15 So Hagar bare to Abram a son, —and Abram called the name of his son, whom Hagar bare, Ishmael.
Tsono Hagara anamuberekera Abramu mwana wamwamuna ndipo Abramu anamutcha mwanayo Ismaeli.
16 Now, Abram, was eighty—six years old, —when Hagar bare Ishmael to Abram.
Pamene Hagara anamubalira Ismaeli nʼkuti Abramuyo ali ndi zaka 86.

< Genesis 16 >