< 2 Samuel 4 >

1 Now, when Ish-bosheth son of Saul heard that Abner had died in Hebron, his hands became feeble, —and, all Israel, were dismayed.
Isiboseti mwana wa Sauli atamva kuti Abineri waphedwa ku Hebroni, anataya mtima ndipo Aisraeli onse anachita mantha kwambiri.
2 And two men, captains of bands, pertained to Ish-bosheth son of Saul—the name of the one, was Baanah, and, the name of the other, Rechab—sons of Rimmon the Beerothite, of the sons of Benjamin, —for, even Beeroth, used to be reckoned unto Benjamin;
Koma Isiboseti anali ndi anthu akuluakulu awiri amene ankatsogolera magulu a ankhondo. Mmodzi mwa iwo dzina lake linali Baana ndipo mnzakeyo anali Rekabu. Iwo anali ana a Rimoni wa banja la Beeroti wa fuko la Benjamini Beeroti. Iwo ankatengedwa ngati mbali imodzi ya Benjamini,
3 and the Beerothites fled to Gittaim, —and have been sojourners there, until this day.
chifukwa anthu a ku Beeroti anathawira ku Gitaimu ndipo akhala ali kumeneko ngati alendo mpaka lero lino.
4 And, Jonathan, son of Saul, had a son, lame of his feet, —five years old, was he, when tidings came in of Saul and Jonathan from Jezreel, so his nurse took him up, and fled, and it came to pass, when she started up to flee, that he fell and was lamed, and, his name, was, Mephibosheth.
(Yonatani mwana wa Sauli anali ndi mwana wamwamuna amene anali wolumala mapazi ake onse awiri. Iye anali ndi zaka zisanu pamene nkhani ya Sauli ndi Yonatani inamveka kuchokera ku Yezireeli. Amene amamulera anamunyamula ndi kuthawa naye, koma pamene amachita zinthu mofulumira mwanayo anagwa ndipo analumala. Dzina lake linali Mefiboseti).
5 So then the sons of Rimmon the Beerothite, Rechab and Baanah, took their journey and came in, about the heat of the day, unto the house of Ish-bosheth, —when, he, was lying on his noonday couch;
Choncho Rekabu ndi Baana ana a Rimoni wa ku Beeroti ananyamuka kupita ku nyumba ya Isi-Boseti, ndipo anafika nthawi ya masana kukutentha pamene iye amapumula.
6 and, thither, entered they as fro as the middle of the house, to fetch wheat, and they smote him in the belly, —and, Rechab and Baanah his brother, escaped.
Iwo analowa mʼchipinda chamʼkati ngati kuti amakatenga tirigu, ndipo anamulasa mʼmimba. Kenaka Rekabu ndi mʼbale wake Baana anathawa.
7 Thus they entered the house when, he, was lying on his bed, in his sleeping-chamber, and smote him, and slew him, and beheaded him, —and took his head, and journeyed by way of the waste plain all the night;
Iwo analowa mʼnyumbamo iye akugona pa bedi mʼchipinda chake. Atamulasa ndi kumupha, anadula mutu wake nʼkuwutenga, nayenda usiku wonse mʼnjira yopita ku Araba.
8 and brought in the head of Ish-bosheth unto David, at Hebron, and said unto the king, Lo! the head of Ish-bosheth son of Saul, thine enemy, who sought thy life: so hath Yahweh given to my lord the king, avengement this day, on Saul and on his seed.
Iwo anabweretsa mutu wa Isi-Boseti kwa Davide ku Hebroni ndipo anati kwa mfumu, “Nawu mutu wa Isiboseti mwana wa Sauli, mdani wanu, amene anafuna kukuphani. Lero lino Yehova wabwezera mbuye wanga mfumu adani anu, Sauli ndi ana ake.”
9 Then David responded to Rechab and Baanah his brother, sons of Rimmon the Beerothite, and said unto them, —By the life of Yahweh, who hath redeemed my soul out of all distress,
Davide anayankha Rekabu ndi mʼbale wake Baana, ana a Rimoni wa ku Beeroti kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene wandipulumutsa ku mavuto anga onse,
10 when he that brought tidings to me, saying, Lo! Saul is dead, though, he, was as one that bringeth good tidings, in his own eyes, yet I seized him, and slew him in Ziklag, —which was how I gave him reward for his tidings:
pamene munthu wina anandiwuza kuti, ‘Sauli wafa’ ndipo ankaganiza kuti wabweretsa nkhani yabwino, ine ndinamugwira ndi kumupha ku Zikilagi. Iyi inali mphotho imene ndinapereka kwa iyeyo chifukwa cha uthenga wake!
11 how much more, when, lawless men, have slain a righteous person, in his own house, upon his bed? …Now, therefore, must I not require his blood at your hands, and so consume you, out of the earth?
Nanji pamene anthu oyipa apha munthu wosalakwa ali mʼnyumba mwake ndiponso pa bedi lake! Kodi ine ndingaleke kukulangani ndi kukuchotsani pa dziko lapansi pano?”
12 David therefore commanded the young men, and they slew them, and cut off their hands, and their feet, and hanged them up over the pool, in Hebron, —but, the head of Ish-bosheth, took they, and buried in the grave of Abner, in Hebron.
Kotero Davide analamulira ankhondo ake, ndipo anawapha. Iwo anawadula manja ndi mapazi ndi kupachika matupi awo pa dziwe la ku Hebroni. Koma anatenga mutu wa Isi-Boseti nawuyika mʼmanda a Abineri ku Hebroni.

< 2 Samuel 4 >