< 2 Chronicles 22 >

1 And the inhabitants of Jerusalem made Ahaziah his youngest son king, in his stead, for, all the elder sons, had the band of men slain who came in with the Arabians into the camp, —so Ahaziah son of Jehoram king of Judah reigned.
Anthu a mu Yerusalemu anayika Ahaziya mwana wamngʼono kwambiri wa Yehoramu kukhala mfumu mʼmalo mwake, popeza gulu lankhondo limene linabwera ndi Aarabu ku misasa, linapha ana onse aakulu. Motero Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Forty-two years old, was Ahaziah when he began to reign, and, one year, reigned he in Jerusalem, —and, the name of his mother, was Athaliah, daughter of Omri.
Ahaziya anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Dzina la amayi ake linali Ataliya, chidzukulu cha Omuri.
3 He too, walked in the ways of the house of Ahab, —for, his mother, became his counselor, to work lawlessness.
Nayenso anayenda mʼnjira ya banja la Ahabu, pakuti amayi ake anamulimbikitsa kuchita zolakwika.
4 Wherefore he did the thing that was wicked in the eyes of Yahweh, like the house of Ahab, —for, they, became his counselors, after the death of his father, to his destruction.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe banja la Ahabu linachitira, pakuti atamwalira abambo ake, iwo anakhala alangizi ake, kumene kunali kudziwononga kwake.
5 Even in their counsel, he walked, and went with Jehoram son of Ahab king of Israel, to war against Hazael king of Syria, in Ramoth-gilead, —and the Syrians smote Joram.
Iyeyo anatsatiranso uphungu wawo pamene anapita ndi Yehoramu, mwana wa Ahabu, mfumu ya Israeli kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yehoramu,
6 And he returned to be healed in Jezreel, because of the wounds wherewith they smote him in Ramah, when he fought with Hazael, king of Syria, —and, Azariah son of Jehoram king of Judah, went down to see Jehoram son of Ahab in Jezreel, because, sick, was he!
kotero iye anabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene anamuvulaza ku Ramoti pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aaramu. Ndipo Ahaziya, mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anapita ku Yezireeli kukaona Yehoramu mwana wa Ahabu chifukwa anavulazidwa.
7 But, from God, came the downfall of Azariah, through his coming to Joram, —and because, through his coming, he went out with Jehoram against Jehu son of Nimshi, whom Yahweh had anointed to cut off the house of Ahab.
Mulungu anakonza kuti Ahaziya akaphedwe pa ulendo wake wokacheza. Ahaziya atafika, iye ndi Yoramu anapita kukakumana ndi Yehu mwana wa Nimisi, amene Yehova anamudzoza kuti akawononge banja la Ahabu.
8 And so it came to pass, when Jehu was executing judgment upon the house of Ahab, —and found the rulers of Judah and the sons of the brethren of Ahaziah ministering to Ahaziah, that he slew them.
Pamene Yehu ankalanga banja la Ahabu anapeza atsogoleri a ku Yuda ndiponso ana aamuna a abale ake a Ahaziya amene amatumikira Ahaziya, ndipo anawapha.
9 And he sought Ahaziah, and they captured him, he, having hid himself in Samaria, and they brought him unto Jehu, and he put him to death, and they buried him, because, said they, he is, the son of Jehoshaphat, who sought Yahweh with all his heart, —and, no one of the house of Ahaziah, had ability for the kingdom.
Kenaka anapita kukafunafuna Ahaziya, ndipo anthu ake anagwira Ahaziya pamene amabisala mu Samariya. Anabwera naye kwa Yehu ndipo anaphedwa. Iwo anamuyika mʼmanda, pakuti anati, “Iyeyu anali mwana wa Yehosafati amene anafunafuna Yehova ndi mtima wake wonse.” Kotero panalibe wamphamvu mʼbanja la Ahaziya kuti nʼkukhala mfumu.
10 But, when, Athaliah mother of Ahaziah, saw that her son was dead, she rose up and destroyed all the seed royal of the house of Judah.
Ataliya, amayi ake a Ahaziya, ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakapha onse a banja laufumu la Yuda.
11 But Jehoshabeath, daughter of the king, took Joash son of Ahaziah, and stole him from among the sons of the king who were being slain, and put him and his nurse in a bedchamber, —so Jehoshabeath daughter of King Jehoram—wife of Jehoiada the priest, for, she, was the sister of Ahaziah—hid him from the face of Athaliah so that she slew him not.
Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, momuba ndi kumuchotsa pakati pa ana aamuna a mfumu amene amati aphedwe ndipo anamuyika iye ndi mlezi wake mʼchipinda chogona. Motero Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, mkazi wa wansembe Yehoyada, yemwe anali mlongo wake wa Ahaziya anamubisa mwanayo kuti Ataliya asamuphe.
12 And it came to pass that he was with them, in the house of God, hidden six years, -while, Athaliah, was reigning over the land.
Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi iwo mu Nyumba ya Mulungu kwa zaka zisanu ndi chimodzi muulamuliro wa Ataliya.

< 2 Chronicles 22 >