< 1 Kings 21 >

1 And it came to pass, after these things, that Naboth the Jezreelite had, a vineyard, which was in Jezreel, —hard by the palace of Ahab, king of Samaria.
Zitatha izi, panachitika nkhani yokhudza Naboti wa ku Yezireeli amene anali ndi munda wamphesa ku Yezireeli, pafupi ndi nyumba ya mfumu Ahabu, mfumu ya ku Samariya.
2 Ahab, therefore, spake unto Naboth, saying—Come! give me thy vineyard, that I may have it for a garden of herbs, for, the same, is near by my house, and let me give thee, instead thereof, a vineyard better than it, —if it be good in thine eyes, I will give thee silver to the value of this.
Ahabu anawuza Naboti kuti, “Patse munda wako wa mpesa kuti ukhale munda wanga wa ndiwo zamasamba, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga yaufumu. Mosinthana ndi mundawu ndidzakupatsa wina wabwino, kapena ngati ungafune, ndidzakupatsa ndalama pa mtengo wake wa mundawu.”
3 And Naboth said unto Ahab, —Far be it from me, of Yahweh! that I should give up the inheritance of my fathers, unto thee!
Koma Naboti anayankha Ahabu kuti, “Pali Yehova, sindingakupatseni cholowa cha makolo anga.”
4 So Ahab came into his house, sullen and disturbed, because of the word which Naboth the Jezreelite had spoken unto him, that he should have said, I will not give thee the inheritance of my fathers. So he laid him down upon his bed, and turned away his face, and did eat no food.
Pamenepo Ahabu anapita ku nyumba yake, wachisoni ndi wokwiya chifukwa Naboti wa ku Yezireeli anamuwuza kuti, “Sindidzakupatsani cholowa cha makolo anga.” Ahabu anakagona pa bedi lake atayangʼana kumbali ndipo anakana chakudya.
5 Then came unto him Jezebel his wife, —and said unto him—Why is it, that thy spirit is sullen, that thou art, not eating food?
Yezebeli mkazi wake analowa ndipo anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuoneka achisoni? Chifukwa chiyani simukufuna chakudya?”
6 And he said unto her—Because I spake unto Naboth, the Jezreelite, and said unto him—Come! give me thy vineyard for silver, or, if thou wouldst prefer, I will give thee a vineyard, in its stead; and he said—I will not give thee my vineyard.
Ahabu anayankha mkazi wake kuti, “Chifukwa chake nʼchakuti ine ndinamuwuza Naboti wa ku Yezireeli kuti, ‘Gulitse munda wako wa mpesa kapena ngati ungakonde ine ndidzakupatsa munda wina wabwino mʼmalo mwake.’ Koma iye anandiyankha kuti, ‘Sindidzakupatsani munda wanga wa mpesa.’”
7 Then Jezebel his wife said unto him: Art, thou, still, going to carry on the kingdom over Israel? Rise! eat food, and let thy heart be merry, I, will give thee the vineyard of Naboth the Jezreelite!
Ndipo Yezebeli mkazi wake anati, “Kodi umu ndi mmene mumachitira ngati mfumu ya Israeli? Dzukani, idyani! Sangalalani. Ine ndidzakutengerani munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli.”
8 So she wrote letters, in the name of Ahab, and sealed them with his signet-ring, —and sent the letters unto the elders, and unto the nobles who were in his city, dwelling with Naboth.
Choncho Yezebeli analemba makalata mʼdzina la Ahabu, nawadinda chidindo cha mfumu, nawatumiza makalatawo kwa akuluakulu ndi kwa anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake.
9 Now she wrote in the letters, saying, —Proclaim ye a fast, and cause Naboth to sit at the head of the people;
Mʼmakalatamo Yezebeli analemba kuti: “Lengezani kuti anthu asale chakudya ndipo muyike Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
10 then let two reckless men take their seats before him, that they may bear witness against him, saying, Thou hast reviled God and king! then shall ye carry him forth and stone him, that he die.
Koma muyike anthu awiri oyipa mtima moyangʼanana naye ndipo iwo achitire umboni kuti watemberera Mulungu ndiponso mfumu. Ndipo mumutulutse ndi kumuponya miyala ndi kumupha.”
11 So the men of his city, the elders and the nobles who dwelt in his city, did just as Jezebel had sent unto them, —as it was written in the letters which she had sent unto them:
Choncho akuluakulu ndi anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake anachita monga analamulira Yezebeli mʼmakalata amene anawalembera.
12 they proclaimed a fast, —and caused Naboth to sit at the head of the people.
Iwo analengeza kuti anthu asale chakudya ndipo anayika Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
13 Then came in the two reckless men, and sat before him, and the men bare witness against him, even against Naboth, before the people, saying, Naboth hath reviled God and king! So they carried him forth, outside the city, and stoned him with stones, that he died.
Ndipo anthu awiri oyipa anabwera nakhala moyangʼanana naye ndipo anamunenera zoyipa Naboti pamaso pa anthu, ponena kuti, “Naboti watemberera Mulungu ndiponso mfumu.” Choncho anamutulutsira kunja kwa mzinda ndi kumuponya miyala ndi kumupha.
14 Then sent they unto Jezebel, saying, —Naboth is stoned and is dead.
Atatero anatumiza mawu kwa Yezebeli akuti, “Naboti amuponya miyala ndipo wafa.”
15 And it came to pass, when Jezebel heard that Naboth was stoned and was dead, that Jezebel said unto Ahab—Rise! take possession of the vineyard of Naboth the Jezreelite, which he refused to give thee for silver, for Naboth is not alive, but dead!
Yezebeli atangomva kuti Naboti amuponya miyala ndipo wafa, iye anakamuwuza Ahabu kuti, “Dzukani, katengeni munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli umene anawukaniza kukugulitsani. Naboti sali moyonso, koma wafa.”
16 And it came to pass, when Ahab heard that Naboth was dead, that Ahab arose, to go down unto the vineyard of Naboth the Jezreelite, to take possession thereof.
Ahabu atamva kuti Naboti wafa, ananyamuka kukatenga munda wamphesa wa Naboti.
17 Then came the word of Yahweh unto Elijah the Tishbite, saying:
Ndipo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
18 Arise! go down to meet Ahab king of Israel, who is in Samaria, —lo! he is in the vineyard of Naboth, whither he hath gone down, to take possession thereof.
“Nyamuka, pita ukakumane ndi Ahabu, mfumu ya Israeli amene amalamulira ku Samariya. Pano ali ku munda wamphesa wa Naboti kumene wapita kuti akatenge mundawo kuti ukhale wake.
19 Then shalt thou speak unto him, saying—Thus, saith Yahweh, Hast thou committed murder, and also taken possession? Then shalt thou speak unto him, saying: Thus, saith Yahweh, In the place where the dogs have lapped up the blood of Naboth, shall the dogs lap up thy blood, even thine.
Ukamuwuze kuti: ‘Yehova akuti, Kodi siwapha munthu ndi kumulandanso munda wake?’ Ndipo ukamuwuzenso kuti, ‘Yehova akuti, Pamalo pamene agalu ananyambita magazi a Naboti, pamalo pomwepo agalu adzanyambita magazi ako, inde, akonso!’”
20 Then said Ahab unto Elijah, Hast thou found me, O mine enemy? And he said: I have found [thee]! Because thou hast sold thyself to do the thing that is wicked in the eyes of Yahweh,
Ahabu anati kwa Eliya, “Tsono wandipeza, iwe mdani wanga!” Eliya anayankha kuti, “Inde ndakupezani chifukwa mwadzigulitsa kuti muchite zoyipa pamaso pa Yehova.
21 Behold me! [saith he] bringing in upon thee, calamity, and I will consume after thee, —and cut off of Ahab, even the meanest, whether shut up or left at large in Israel;
Iye akuti ‘Taonani, ine ndidzabweretsa mavuto pa iwe. Ndidzawononga kotheratu zidzukulu zako ndi kuchotsa mu Israeli munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu, kapolo kapena mfulu.
22 and will deliver up thy house—Like the house of Jeroboam son of Nebat, and like the house of Baasha son of Ahijah, —for the provocation wherewith thou hast provoked, and caused, Israel, to sin.
Ndidzawononga nyumba yako monga momwe ndinawonongera nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati nyumba ya Baasa mwana wa Ahiya, chifukwa wandikwiyitsa Ine ndi kuchimwitsa Israeli.’
23 Moreover also, concerning Jezebel, hath Yahweh spoken, saying, —The dogs, shall eat Jezebel, in the town-land of Jezreel:
“Ndipo kunena za Yezebeli, Yehova akuti, ‘Agalu adzadya Yezebeli mʼmbali mwa khoma la Yezireeli.’
24 Him that dieth, of Ahab, in the city, shall, the dogs, eat, —and, him that dieth in the field, shall, the birds of heaven, eat.
“Agalu adzadya munthu aliyense wa nyumba ya Ahabu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya aliyense wofera ku thengo.”
25 But indeed, there was none like Ahab, who sold himself to do the thing that was wicked in the eyes of Yahweh, —whom Jezebel his wife goaded on;
(Kunalibe munthu ngati Ahabu, amene anadzigulitsa kuchita zoyipa pamaso pa Yehova, amene anakopedwa ndi mkazi wake Yezebeli.
26 so that he did very abominably, in going after the manufactured gods, —according to all which the Amorites had done, whom Yahweh dispossessed from before the sons of Israel.
Iye anachita zonyansa kwambiri popembedza mafano, monga mmene ankachitira Aamori amene Yehova anawachotsa pamene Aisraeli ankafika).
27 And it came to pass, when Ahab heard these words, that he rent his clothes, and put sackcloth upon his flesh, and fasted, —and lay in sackcloth, and went softly.
Ahabu atamva mawu amenewa, anangʼamba zovala zake, navala ziguduli ndi kusala chakudya. Anagona pa ziguduli, nayenda pangʼonopangʼono.
28 Then came the word of Yahweh unto Elijah the Tishbite, saying:
Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
29 Hast thou seen that Ahab hath humbled himself, before me? Because he hath humbled himself before me, I will not bring in the calamity in his days, In the days of his son, will I bring in the calamity upon his house.
“Kodi waona mmene Ahabu wadzichepetsera pamaso panga? Chifukwa wadzichepetsa, sindidzabweretsa mavuto amenewa pa nthawi ya moyo wake, koma ndidzawabweretsa pa nyumba yake pa nthawi ya mwana wake.”

< 1 Kings 21 >