< Psalms 27 >
1 [A Psalm] of David. The LORD is my light and my salvation; whom shall I fear? the LORD is the strength of my life; of whom shall I be afraid?
Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
2 When evil-doers came upon me to eat up my flesh, [even] mine adversaries and my foes, they stumbled and fell.
Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
3 Though an host should encamp against me, my heart shall not fear: though war should rise against me, even then will I be confident.
Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
4 One thing have I asked of the LORD, that will I seek after; that I may dwell in the house of the LORD all the days of my life, to behold the beauty of the LORD, and to inquire in his temple.
Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
5 For in the day of trouble he shall keep me secretly in his pavilion: in the covert of his tabernacle shall he hide me; he shall lift me up upon a rock.
Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
6 And now shall mine head be lifted up above mine enemies round about me; and I will offer in his tabernacle sacrifices of joy; I will sing, yea, I will sing praises unto the LORD.
Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
7 Hear, O LORD, when I cry with my voice: have mercy also upon me, and answer me.
Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
8 [When thou saidst], Seek ye my face; my heart said unto thee, Thy face, LORD, will I seek.
Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
9 Hide not thy face from me; put not thy servant away in anger: thou hast been my help; cast me not off, neither forsake me, O God of my salvation.
Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
10 For my father and my mother have forsaken me, but the LORD will take me up.
Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
11 Teach me thy way, O LORD; and lead me in a plain path, because of mine enemies.
Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
12 Deliver me not over unto the will of mine adversaries: for false witnesses are risen up against me, and such as breathe out cruelty.
Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
13 [I had fainted], unless I had believed to see the goodness of the LORD in the land of the living.
Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
14 Wait on the LORD: be strong, and let thine heart take courage; yea, wait thou on the LORD.
Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.