< Job 37 >
1 At this my heart trembleth, And leapeth out of its place.
“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
2 Hear, O hear, the thunder of his voice, And the noise which goeth forth from his mouth!
Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
3 He directeth it under the whole heaven, And his lightning to the ends of the earth.
Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
4 After it the thunder roareth; He thundereth with his voice of majesty, And restraineth it not, when his voice is heard.
Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
5 God thundereth with his voice marvellously; Great things doeth he, which we cannot comprehend.
Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
6 For he saith to the snow, “Be thou on the earth!” To the shower also, even the showers of his might.
Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
7 He sealeth up the hand of every man, That all men whom he hath made may acknowledge him.
Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
8 Then the beasts go into dens, And abide in their caverns.
Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
9 Out of the south cometh the whirlwind, And cold out of the north.
Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
10 By the breath of God ice is formed, And the broad waters become narrow,
Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
11 Yea, with moisture he burdeneth the clouds; He spreadeth abroad his lightning-clouds.
Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
12 They move about by his direction, To execute all his commands throughout the world;
Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
13 Whether he cause them to come for punishment, Or for the land, or for mercy.
Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
14 Give ear to this, O Job! Stand still, and consider the wondrous works of God!
“Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
15 Dost thou know when God gave commandment to them, And caused the lightning of his cloud to flash?
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
16 Dost thou understand the balancing of the clouds, The wondrous works of Him that is perfect in knowledge?
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
17 How thy garments become warm, When he maketh the earth still by the south wind?
Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
18 Canst thou like him spread out the sky, Which is firm like a molten mirror?
kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
19 Teach us what we shall say to him! For we cannot set in order our words by reason of darkness.
“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
20 Shall it be told him that I would speak? Shall a man speak, that he may be consumed?
Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
21 For now men do not look upon the light, When it is bright in the skies, When the wind hath passed over them, and made them clear.
Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
22 From the north cometh gold; But with God is terrible majesty!
Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
23 The Almighty, we cannot find him out; Great is he in power and justice, Abundant in righteousness; he doth not oppress.
Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
24 Therefore let men fear him! Upon none of the wise in heart will he look.
Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”