< Psalms 78 >

1 [A contemplation by Asaph.] Hear my teaching, my people. Turn your ears to the words of my mouth.
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 I will open my mouth in a parable. I will utter dark sayings since the beginning of the world,
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 which we have heard and known, and our fathers have told us.
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 We will not hide them from their descendants, telling to the generation to come the praises of the LORD, his strength, and his wondrous works that he has done.
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 For he established a testimony in Jacob, and appointed a teaching in Israel, which he commanded our fathers, that they should make them known to their children;
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 that the generation to come might know it, the children yet unborn, and arise and tell their children,
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 that they might set their hope in God, and not forget the works of God, but keep his commandments,
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 and might not be as their fathers, a stubborn and rebellious generation, a generation that did not make their hearts loyal, whose spirit was not steadfast with God.
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 The people of Ephraim, being armed and carrying bows, turned back in the day of battle.
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 They did not keep God's covenant, and refused to walk by his Law.
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 They forgot his doings, his wondrous works that he had shown them.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 He did marvelous things in the sight of their fathers, in the land of Egypt, in the field of Zoan.
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 He split the sea, and caused them to pass through. He made the waters stand as a heap.
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 In the daytime he also led them with a cloud, and all night with a light of fire.
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 He split rocks in the wilderness, and gave them drink abundantly as out of the depths.
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 He brought streams also out of the rock, and caused waters to run down like rivers.
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 Yet they still went on to sin against him, to rebel against the Most High in the desert.
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 They tempted God in their heart by asking food according to their desire.
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 Yes, they spoke against God. They said, "Can God prepare a table in the wilderness?
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 Look, he struck the rock, so that waters gushed out, and streams overflowed. Can he give bread also? Will he provide flesh for his people?"
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 Therefore the LORD heard, and was angry. A fire was kindled against Jacob, anger also went up against Israel,
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 because they did not believe in God, and did not trust in his salvation.
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 Yet he commanded the clouds above, and opened the doors of heaven.
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 He rained down manna on them to eat, and gave them bread from heaven.
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 Man ate the bread of the mighty ones. He sent them food to the full.
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 He caused the east wind to blow in the sky. By his power he guided the south wind.
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 He rained also flesh on them as the dust; winged birds as the sand of the seas.
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 He let it fall in the midst of his camp, all around his tent.
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 So they ate, and were well filled. He gave them their own desire.
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 They did not turn from their cravings. Their food was yet in their mouths,
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 when the anger of God went up against them, killed some of the fattest of them, and struck down the young men of Israel.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 For all this they still sinned, and did not believe in his wondrous works.
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 Therefore he consumed their days in vanity, and their years in terror.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 When he killed them, then they inquired after him. They returned and sought God earnestly.
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 They remembered that God was their rock, the Most High God, their redeemer.
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 But they flattered him with their mouth, and lied to him with their tongue.
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 For their heart was not right with him, neither were they faithful in his covenant.
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 But he, being merciful, forgave iniquity, and did not destroy them. Yes, many times he turned his anger away, and did not stir up all his wrath.
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 He remembered that they were but flesh, a wind that passes away, and doesn't come again.
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 How often they rebelled against him in the wilderness, and grieved him in the desert.
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 They turned again and tempted God, and gave pain to the Holy One of Israel.
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 They did not remember his hand, nor the day when he redeemed them from the adversary;
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 how he set his signs in Egypt, his wonders in the field of Zoan,
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 he turned their rivers into blood, and their streams, so that they could not drink.
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 He sent among them swarms of flies, which devoured them; and frogs, which destroyed them.
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 He gave also their increase to the caterpillar, and their labor to the locust.
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 He destroyed their vines with hail, their sycamore fig trees with frost.
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 He gave over their livestock also to the hail, and their flocks to hot thunderbolts.
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 He threw on them the fierceness of his anger, wrath, indignation, and trouble, and a band of destroying angels.
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 He made a path for his anger. He did not spare their soul from death, but gave their life over to the pestilence,
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 and struck all the firstborn in Egypt, the chief of their strength in the tents of Ham.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 But he led forth his own people like sheep, and guided them in the wilderness like a flock.
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 He led them safely, so that they weren't afraid, but the sea overwhelmed their enemies.
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 He brought them to the border of his sanctuary, to this mountain, which his right hand had taken.
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 He also drove out the nations before them, allotted them for an inheritance by line, and made the tribes of Israel to dwell in their tents.
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 Yet they tempted and rebelled against the Most High God, and did not keep his testimonies;
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 but turned back, and dealt treacherously like their fathers. They were turned aside like a deceitful bow.
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 For they provoked him to anger with their high places, and moved him to jealousy with their engraved images.
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 When God heard this, he was angry, and greatly abhorred Israel;
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 So that he forsook the tabernacle at Shiloh, the tent where he dwelt among men;
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 and delivered his strength into captivity, his glory into the adversary's hand.
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 He also gave his people over to the sword, and was angry with his inheritance.
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 Fire devoured their young men. Their virgins had no wedding song.
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 Their cohanim fell by the sword, and their widows couldn't weep.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 Then the Lord awakened as one out of sleep, like a mighty man who shouts by reason of wine.
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 He struck his adversaries backward. He made them a permanent shame.
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 Moreover he rejected the tent of Joseph, and did not choose the tribe of Ephraim,
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 But chose the tribe of Judah, Mount Zion which he loved.
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 He built his sanctuary like the heights, like the earth which he has established forever.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 He also chose David his servant, and took him from the sheepfolds;
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 from following the ewes that have their young, he brought him to be the shepherd of Jacob his servant, and Israel his inheritance.
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 So he was their shepherd according to the integrity of his heart, and guided them by the skillfulness of his hands.
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.

< Psalms 78 >