< Psalms 63 >

1 [A Psalm by David, when he was in the desert of Judah.] God, you are my God. I will earnestly seek you. My soul thirsts for you. My flesh longs for you, in a dry and weary land, where there is no water.
Salimo la Davide. Pamene anali mʼchipululu cha Yuda. Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga, moona mtima ine ndimakufunafunani; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu, thupi langa likulakalaka inu, mʼdziko lowuma ndi lotopetsa kumene kulibe madzi.
2 So I have seen you in the sanctuary, watching your power and your glory.
Inu ndinakuonani ku malo anu opatulika ndipo ndinapenya mphamvu zanu ndi ulemerero wanu.
3 Because your loving kindness is better than life, my lips shall praise you.
Chifukwa chikondi chanu ndi choposa moyo, milomo yanga idzakulemekezani.
4 So I will bless you while I live. I will lift up my hands in your name.
Ndidzakutamandani masiku onse a moyo wanga, ndipo mʼdzina lanu ndidzakweza manja anga.
5 My soul shall be satisfied as with the richest food. My mouth shall praise you with joyful lips,
Mudzakhutitsa moyo wanga ndi zonona. Ine ndidzakutamandani ndi mawu anthetemya.
6 when I remember you on my bed, and think about you in the night watches.
Pa bedi panga ndimakumbukira inu; ndimaganiza za Inu nthawi yonse ya usiku.
7 For you have been my help. I will rejoice in the shadow of your wings.
Chifukwa ndinu thandizo langa, ine ndimayimba mu mthunzi wa mapiko anu.
8 My soul stays close to you. Your right hand holds me up.
Moyo wanga umakangamira Inu; dzanja lanu lamanja limandigwiriziza.
9 But those who seek my soul, to destroy it, shall go into the lower parts of the earth.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga adzawonongedwa; adzatsikira kunsi kozama kwa dziko lapansi.
10 They shall be given over to the power of the sword. They shall be jackal food.
Iwo adzaperekedwa ku lupanga ndi kukhala chakudya cha ankhandwe.
11 But the king shall rejoice in God. Everyone who swears by him will praise him, for the mouth of those who speak lies shall be silenced.
Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; onse amene amalumbira mʼdzina la Mulungu adzalemekeza Mulunguyo, koma pakamwa pa anthu onama padzatsekedwa.

< Psalms 63 >