< Psalms 6 >

1 [For the Chief Musician; on stringed instruments, upon the eight-stringed lyre. A Psalm by David.] LORD, do not rebuke me in your anger, neither discipline me in your wrath.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
2 Be gracious to me, LORD, for I am frail. LORD, heal me, for my bones are trembling.
Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
3 And my soul is greatly troubled. But you, LORD, how long?
Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
4 Return, LORD. Deliver my soul. Save me because of your lovingkindness.
Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
5 For in death there is no memory of you. In Sheol, who shall give you thanks? (Sheol h7585)
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
6 I am weary with my groaning. Every night I drench my bed; I melt my couch with my tears.
Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
7 My eye wastes away because of grief. It grows old because of all my adversaries.
Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
8 Depart from me, all you workers of iniquity, for the LORD has heard the sound of my weeping.
Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
9 The LORD has heard my plea. The LORD has accepted my prayer.
Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
10 May all my enemies be ashamed and greatly terrified. May they turn back, suddenly ashamed.
Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

< Psalms 6 >