< Psalms 38 >

1 [A Psalm by David, for a memorial.] LORD, do not rebuke me in your wrath, neither chasten me in your hot displeasure.
Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
2 For your arrows have pierced me, your hand presses hard on me.
Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
3 There is no soundness in my flesh because of your indignation, neither is there any health in my bones because of my sin.
Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
4 For my iniquities have gone over my head. As a heavy burden, they are too heavy for me.
Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
5 My wounds are loathsome and corrupt, because of my foolishness.
Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
6 I am pained and bowed down greatly. I go mourning all day long.
Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
7 For my waist is filled with burning. There is no soundness in my flesh.
Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
8 I am faint and severely bruised. I have groaned by reason of the anguish of my heart.
Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
9 Lord, all my desire is before you. My groaning is not hidden from you.
Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
10 My heart throbs. My strength fails me. As for the light of my eyes, it has also left me.
Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
11 My loved ones and my friends keep their distance because of my affliction. My kinsmen stand far away.
Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
12 They also who seek after my life lay snares. Those who seek my hurt speak mischievous things, and meditate deceits all day long.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
13 But I, as a deaf man, do not hear. I am as a mute man who doesn't open his mouth.
Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
14 Yes, I am as a man who doesn't hear, in whose mouth are no reproofs.
Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
15 For in you, LORD, do I hope. You will answer, LORD my God.
Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
16 For I said, "Do not let them gloat over me, or exalt themselves over me when my foot slips."
Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
17 For I am ready to fall. My pain is continually before me.
Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
18 Yes, I confess my iniquity. I am anxious because of my sin.
Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
19 But my enemies, for no reason, are many. Those who hate me wrongfully are numerous.
Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
20 They who also render evil for good are adversaries to me, because I follow what is good.
Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
21 Do not forsake me, LORD. My God, do not be far from me.
Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
22 Hurry to help me, LORD, my salvation.
Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.

< Psalms 38 >