< Psalms 145 >

1 [A praise psalm by David.] I will exalt you, my God, the King. I will praise your name forever and ever.
Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 Every day I will praise you. I will extol your name forever and ever.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 Great is the LORD, and greatly to be praised. His greatness is unsearchable.
Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 One generation will commend your works to another, and will declare your mighty acts.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 Of the glorious splendor of your majesty they will speak, of your wondrous works, I will meditate.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 Men will speak of the might of your awesome acts. I will declare your greatness.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 They will utter the memory of your great goodness, and will sing of your righteousness.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 The LORD is gracious, merciful, slow to anger, and of great loving kindness.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 The LORD is good to all. His tender mercies are over all his works.
Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 All your works will give thanks to you, LORD. And your faithful ones will bless you.
Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
11 They will speak of the glory of your kingdom, and talk about your power;
Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 to make known to the descendants of Adam his mighty acts, the glory of the majesty of his kingdom.
kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Your kingdom is an everlasting kingdom. Your dominion endures throughout all generations. The LORD is faithful in all his words, and gracious in all his deeds.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 The LORD upholds all who fall, and raises up all those who are bowed down.
Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 The eyes of all wait for you. You give them their food in due season.
Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 You yourself open your hand and satisfy the desire of every living thing.
Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 The LORD is righteous in all his ways, and faithful in all his deeds.
Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 The LORD is near to all those who call on him, to all who call on him in truth.
Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 He will fulfill the desire of those who fear him. He also will hear their cry, and will save them.
Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 The LORD preserves all those who love him, but all the wicked he will destroy.
Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 My mouth will speak the praise of the LORD. Let all flesh bless his holy name forever and ever.
Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.

< Psalms 145 >