< Psalms 109 >

1 [For the Chief Musician. A Psalm by David.] God of my praise, do not remain silent,
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
2 for they have opened the mouth of the wicked and the mouth of deceit against me. They have spoken to me with a lying tongue.
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
3 They have also surrounded me with words of hatred, and fought against me without a cause.
Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
4 In return for my love, they are my adversaries; but I am in prayer.
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
5 They have rewarded me evil for good, and hatred for my love.
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
6 Set a wicked man over him. Let an adversary stand at his right hand.
Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
7 When he is judged, let him come forth guilty. Let his prayer be turned into sin.
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
8 Let his days be few. Let another take his office.
Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
9 Let his children be fatherless, and his wife a widow.
Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 Let his children be wandering beggars. Let them be sought from their ruins.
Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 Let the creditor seize all that he has. Let strangers plunder the fruit of his labor.
Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 Let there be none to extend kindness to him, neither let there be any to have pity on his fatherless children.
Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 Let his posterity be cut off. In the generation following let their name be blotted out.
Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 Let the iniquity of his fathers be remembered by the LORD. Do not let the sin of his mother be blotted out.
Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 Let them be before the LORD continually, that he may cut off the memory of them from the earth;
Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
16 because he did not remember to show kindness, but persecuted the poor and needy man, the broken in heart, to kill them.
Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
17 Yes, he loved cursing, and it came to him. He did not delight in blessing, and it was far from him.
Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
18 He clothed himself also with cursing as with his garment. It came into his inward parts like water, like oil into his bones.
Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
19 Let it be to him as the clothing with which he covers himself, for the belt that is always around him.
Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 This is the reward of my adversaries from the LORD, of those who speak evil against my soul.
Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
21 But deal with me, the LORD the Lord, for your name's sake, because your loving kindness is good, deliver me;
Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
22 for I am poor and needy. My heart is wounded within me.
Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 I fade away like an evening shadow. I am shaken off like a locust.
Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 My knees are weak through fasting. My body is thin and lacks fat.
Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
25 I have also become a reproach to them. When they see me, they shake their head.
Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
26 Help me, LORD, my God. Save me according to your loving kindness;
Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 that they may know that this is your hand; that you, LORD, have done it.
Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 They may curse, but you bless. When they arise, they will be shamed, but your servant shall rejoice.
Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 Let my adversaries be clothed with dishonor. Let them cover themselves with their own shame as with a robe.
Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
30 I will give great thanks to the LORD with my mouth. Yes, I will praise him among the multitude.
Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 For he will stand at the right hand of the needy, to save him from those who judge his soul.
Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.

< Psalms 109 >