< Numbers 6 >

1 The LORD spoke to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 "Speak to the children of Israel, and tell them: When either man or woman shall make a special vow, the vow of a Nazirite, to separate himself to the LORD,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mwamuna kapena mkazi afuna kuchita lonjezo lapadera, lonjezo lodzipatula yekha kwa Yehova ngati Mnaziri,
3 he shall separate himself from wine and strong drink. He shall drink no vinegar of wine, or vinegar of fermented drink, neither shall he drink any juice of grapes, nor eat fresh grapes or dried.
sayenera kumwa vinyo kapena zakumwa zosasa ndipo asamamwe chakumwa chilichonse cha mphesa. Asamamwe madzi a mphesa kapena kudya mphesa zaziwisi kapena zowuma.
4 All the days of his separation he shall eat nothing that is made of the grapevine, from the seeds even to the skins.
Pa nthawi yonse imene ali Mnaziri, asamadye chilichonse chopangidwa kuchokera ku mphesa ngakhale mbewu zake kapena makungu ake.’
5 "All the days of his vow of separation there shall no razor come on his head, until the days are fulfilled, in which he separates himself to the LORD. He shall be holy. He shall let the locks of the hair of his head grow long.
“‘Pa nthawi yonse ya lonjezo lodzipatula yekhalo, asamete kumutu kwake ndi lumo. Akhale wopatulika mpaka nthawi yake yonse ya kudzipatula yekha kwa Yehova itatha. Alileke tsitsi la pamutu pake kuti likule.’
6 "All the days that he separates himself to the LORD he shall not go near a dead body.
Pa nthawi yonse imene munthuyo wadzipatula yekha kwa Yehova asayandikire mtembo.
7 He shall not make himself unclean for his father, or for his mother, for his brother, or for his sister, when they die; because his separation to God is on his head.
Ngakhale abambo ake kapena amayi ake kapena mchimwene wake kaya mchemwali wake atamwalira, asadzidetse pokhudza mitembo yawo chifukwa kulumbira kwake kwa kudzipatula yekha kwa Yehova kuli pamutu pake.
8 All the days of his separation he is holy to the LORD.
Munthuyo ndi wopatulika masiku onse odzipereka kwake kwa Yehova.
9 "If any man dies very suddenly beside him, and he defiles the head of his separation; then he shall shave his head in the day of his cleansing. On the seventh day he shall shave it.
“Ngati munthu wina afa mwadzidzidzi pafupi naye ndi kudetsa tsitsi lake loperekedwalo, amete mutu wake pa tsiku lodziyeretsa, tsiku lachisanu ndi chiwiri.
10 On the eighth day he shall bring two turtledoves or two young pigeons to the cohen, to the door of the Tent of Meeting.
Tsono pa tsiku lachisanu ndi chitatu abweretse nkhunda ziwiri kapena mawunda awiri anjiwa kwa wansembe pa khomo lolowera ku tenti ya msonkhano.
11 The cohen shall offer one for a sin offering, and the other for a burnt offering, and make atonement for him, because he sinned by reason of the dead, and shall make his head holy that same day.
Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yauchimo ndi ina nsembe yopsereza yotetezera tchimo chifukwa anachimwa popezeka pafupi ndi mtembo. Ndipo tsiku lomwelo apatulenso tsitsi la pamutu pake.
12 He shall separate to the LORD the days of his separation, and shall bring a male lamb a year old for a trespass offering; but the former days shall be void, because his separation was defiled.
Adzipereke kwa Yehova pa nthawi yodzipatula ndipo abweretse nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi ngati nsembe yopepesera. Masiku akale sawerengedwanso chifukwa anadzidetsa pa nthawi yodzipatulira kwake.
13 "This is the law of the Nazirite: when the days of his separation are fulfilled, he shall be brought to the door of the Tent of Meeting,
“Tsono ili ndi lamulo la Mnaziri pamene nthawi yodzipatula kwake yatha: Abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
14 and he shall offer his offering to the LORD, one male lamb a year old without blemish for a burnt offering, and one ewe lamb a year old without blemish for a sin offering, and one ram without blemish for peace offerings,
Pamenepo apereke chopereka chake kwa Yehova: Nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi yopanda chilema kuti ikhale nsembe yopsereza, mwana wankhosa wamkazi mmodzi wopanda chilema kuti ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa imodzi yayikulu yayimuna kuti ikhale nsembe yachiyanjano,
15 and a basket of unleavened bread, cakes of fine flour mixed with oil, and unleavened wafers anointed with oil, and their meal offering, and their drink offerings.
ndipo abwere pamodzi ndi nsembe yachakudya ndi nsembe yachakumwa ndi dengu la buledi wopanda yisiti, makeke opangidwa ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda ta buledi topakidwa mafuta.
16 The cohen shall present them before the LORD, and shall offer his sin offering, and his burnt offering.
“Wansembe apereke zimenezi pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe ya uchimo ndi nsembe yopsereza.
17 He shall offer the ram for a sacrifice of peace offerings to the LORD, with the basket of unleavened bread. The cohen shall offer also its meal offering, and its drink offering.
Apereke dengu la buledi wopanda yisiti ndiponso nsembe yachiyanjano kwa Yehova ya nkhosa yayimuna, pamodzi ndi chopereka cha chakudya ndi chopereka cha chakumwa.
18 The Nazirite shall shave the head of his separation at the door of the Tent of Meeting, and shall take the hair of the head of his separation, and put it on the fire which is under the sacrifice of peace offerings.
“Mnaziriyo amete tsitsi limene analipereka lija pa khomo la tenti ya msonkhano. Atenge tsitsilo ndi kuliyika pa moto umene uli pansi pa nsembe yachiyanjano.
19 The cohen shall take the boiled shoulder of the ram, and one unleavened cake out of the basket, and one unleavened wafer, and shall put them on the hands of the Nazirite, after he has shaved the head of his separation;
“Mnaziriyo atatha kumeta tsitsi analiperekalo, wansembe ayike mʼmanja mwake mwendo wa mmwamba wankhosa yayimuna umene waphikidwa ndipo atengenso keke ndi kamtanda ka buledi, zonse zopanda yisiti zomwe zili mʼdengu lija.
20 and the cohen shall wave them for a wave offering before the LORD. This is holy for the cohen, together with the breast that is waved and the thigh that is offered. After that the Nazirite may drink wine.
Wansembe aziweyule pamaso pa Yehova ngati nsembe yoweyula. Zimenezi ndi zopatulika ndipo ndi za wansembe pamodzi ndi chidale chimene anachiweyula ndi ntchafu yomwe anayipereka ija. Zitatha izi, Mnaziri akhoza kumwa vinyo.
21 "This is the law of the Nazirite who vows, and of his offering to the LORD for his separation, besides that which he is able to get. According to his vow which he vows, so he must do after the law of his separation."
“Ili ndi lamulo la Mnaziri yemwe walonjeza kudzipereka kwa Yehova podzipatula yekha kuphatikiza pa zomwe angathe kukwaniritsa. Ayenera kukwaniritsa lonjezo lomwe wachitalo potsata lamulo la Mnaziri.”
22 The LORD spoke to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
23 "Speak to Aaron and to his sons, saying, 'This is how you shall bless the children of Israel.' You shall tell them,
“Uza Aaroni ndi ana ake aamuna kuti, ‘Umu ndi mmene muzidalitsira Aisraeli. Muzinena kuti,
24 'The LORD bless you, and keep you.
“‘Yehova akudalitse ndi kukusunga;
25 The LORD make his face to shine on you, and be gracious to you.
Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitira chisomo;
26 The LORD lift up his face toward you, and give you peace.'
Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.’”
27 "So they shall put my name on the children of Israel; and I will bless them."
Choncho akadzatchula dzina langa podalitsa Aisraeli, Ine ndidzawadalitsadi.

< Numbers 6 >