< Genesis 10 >

1 Now these are the generations of the sons of Noah and of Shem, Ham, and Japheth. Sons were born to them after the flood.
Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
2 The sons of Japheth: Gomer, Magog, Madai, Javan, Tubal, Meshech, and Tiras.
Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
3 The sons of Gomer: Ashkenaz, Riphath, and Togarmah.
Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
4 The sons of Javan: Elishah, Tarshish, Kittim, and Rodanim.
Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
5 From these, the coastlands of the nations separated into their territories, every one according to its language, according to their families, in their nations.
(Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
6 The sons of Ham: Cush, Mizraim, Put, and Canaan.
Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
7 The sons of Cush: Seba, Havilah, Sabtah, Raamah, and Sabteca. The sons of Raamah: Sheba and Dedan.
Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
8 Cush became the father of Nimrod. He began to be a mighty one on the earth.
Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
9 He was a mighty hunter before God. Therefore it is said, "Like Nimrod, a mighty hunter before God."
Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
10 And the beginning of his kingdom was Babel, and Erech, and Akkad, and Calneh, in the land of Shinar.
Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
11 Out of that land he went forth into Assyria, and built Nineveh, and Rehoboth Ir, and Calah,
Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
12 and Resen, between Nineveh and the great city of Calah.
ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
13 And Mizraim became the father of Ludim, and Anamim, and Lehabim, and Naphtuhim,
Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
14 And Pathrusim, and Casluhim, which the Philistines descended from, and Caphtorim.
Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
15 And Canaan became the father of Sidon, his firstborn, and Heth,
Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
16 and the Jebusites, and the Amorites, and the Girgashites,
Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
17 and the Hivites, and the Arkites, and the Sinites,
Ahivi, Aariki, Asini,
18 and the Arvadites, and the Zemarites, and the Hamathites. Afterward the families of the Canaanites were spread abroad.
Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
19 And the border of the Canaanites was from Sidon, as you go toward Gerar, to Gaza; as you go toward Sodom, and Gomorrah, and Admah, and Zeboiim, to Lasha.
mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
20 These are the sons of Ham, after their families, after their languages, in their lands, in their nations.
Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
21 To Shem, the father of all the children of Eber, the elder brother of Japheth, to him also were children born.
Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
22 The sons of Shem: Elam, and Asshur, and Arpachshad, and Lud, and Aram.
Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
23 The sons of Aram: Uz, and Hul, and Gether, and Mash.
Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
24 And Arpachshad became the father of Kenan. And Kenan became the father of Shelah. And Shelah became the father of Eber.
Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
25 To Eber were born two sons. The name of the one was Peleg, for in his days the earth was divided. His brother's name was Joktan.
A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
26 And Joktan became the father of Almodad, and Sheleph, and Hazarmaveth, and Jerah,
Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
27 and Hadoram, and Uzal, and Diklah,
Hadoramu, Uzali, Dikila,
28 and Obal, and Abimael, and Sheba,
Obali, Abimaeli, Seba,
29 and Ophir, and Havilah, and Jobab. All these were the sons of Joktan.
Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
30 Their dwelling was from Mesha, as you go toward Sephar, the mountain of the east.
Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
31 These are the sons of Shem, after their families, after their languages, in their lands, after their nations.
Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
32 These are the families of the sons of Noah, after their generations, in their nations, and from these the nations branched out on the earth after the flood.
Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.

< Genesis 10 >