< Exodus 24 >

1 He said to Moses, "Come up to the LORD, you, and Aaron, Nadab, and Abihu, and seventy of the elders of Israel; and worship from a distance.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Bwera ku phiri kuno kwa Yehova, iwe pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu a Israeli makumi asanu ndi awiri. Enanu mundipembedze muli chapatali.
2 Moses alone shall come near to God, but they shall not come near, neither shall the people go up with him."
Koma Mose yekha ayandikire Yehova, ndipo enawo asayandikire. Komanso anthu ena onse asakwere nawe ku phiri kuno.”
3 Moses came and told the people all the words of God, and all the ordinances; and all the people answered with one voice, and said, "All the words which the LORD has spoken will we do."
Tsono Mose anapita kukawuza anthu mawu onse a Yehova ndi malamulo onse, ndipo anthu onse anayankha mogwirizana kuti, “Tidzachita zonse zimene Yehova wanena.”
4 Moses wrote all the words of the LORD, and rose up early in the morning, and built an altar under the mountain, and twelve pillars for the twelve tribes of Israel.
Ndipo Mose analemba zonse zimene Yehova ananena. Mmawa mwake Mose anadzuka nayamba kumanga guwa lansembe mʼmunsi mwa phirilo ndipo anayimika miyala khumi ndi iwiri ngati zipilala kuyimira mafuko khumi ndi awiri a Israeli.
5 He sent young men of the children of Israel, who offered burnt offerings and sacrificed peace offerings of cattle to God.
Kenaka Mose anatuma Aisraeli achinyamata kuti aphe ndi kukapereka kwa Yehova nsembe zopsereza zachiyanjano.
6 Moses took half of the blood and put it in basins, and half of the blood he sprinkled on the altar.
Mose anatenga theka la magazi ndi kuyika mʼmbale, ndipo theka linalo analiwaza pa guwa lansembe.
7 He took the book of the covenant and read it in the hearing of the people, and they said, "All that the LORD has spoken will we do, and be obedient."
Anatenganso Buku la Chipangano ndi kuwerengera anthu. Anthuwo anayankha kuti, “Zonse zimene Yehova wanena tamva, ndipo tidzazichita.”
8 Moses took the blood, and sprinkled it on the people, and said, "This is the blood of the covenant, which God has commanded you concerning all these words."
Kenaka Mose anatenga magazi, nawaza anthuwo ndipo anati, “Awa ndi magazi a pangano limene Yehova wapanga ndi inu molingana ndi mawu ake onsewa.”
9 Then Moses, Aaron, Nadab, Abihu, and seventy of the elders of Israel went up.
Kenaka Mose pamodzi ndi Aaroni, Nadabu, Abihu ndi akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Israeli aja anakwera ku phiri,
10 They saw the God of Israel. Under his feet was like a paved work of sapphire stone, like the skies for clearness.
ndipo anaona Mulungu wa Israeli. Pansi pa mapazi ake panali njira yoyendamo yopangidwa ndi mwala wa safiro woyalidwa bwino wa maonekedwe owala ngati thambo.
11 He did not lay his hand on the nobles of the children of Israel. They saw God, and ate and drank.
Ngakhale anaona Yehova koma sanafe, mʼmalo mwake anadya ndi kumwa.
12 The LORD said to Moses, "Come up to me on the mountain, and stay here, and I will give you the tablets of stone with the law and the commands that I have written, that you may teach them."
Yehova anati kwa Mose, “Bwera kwa ine ku phiri kuno, ndipo udikire konkuno. Ndidzakupatsa miyala imene ndalembapo malemba kuti ndiwaphunzitse.”
13 Moses rose up with Joshua, his servant, and Moses went up onto God's Mountain.
Ndipo anayamba ulendo wopita ku phiri la Mulungu pamodzi ndi womuthandiza wake Yoswa.
14 He said to the elders, "Wait here for us, until we come again to you. Look, Aaron and Hur are with you. Whoever is involved in a dispute can go to them."
Apa nʼkuti Mose atawawuza akuluakulu aja kuti, “Mudikire pano mpaka titabweranso. Aaroni ndi Huri ali nanu, aliyense amene ali ndi milandu apite kwa iwo.”
15 Moses went up on the mountain, and the cloud covered the mountain.
Mose atakwera ku phiri kuja mtambo unaphimba phirilo.
16 The glory of God settled on Mount Sinai, and the cloud covered it six days. The seventh day he called to Moses out of the midst of the cloud.
Ulemerero wa Yehova unakhala pa phiri la Sinai, ndipo mtambo unaphimba phirilo kwa masiku asanu ndi limodzi. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Yehova anayitana Mose kuchokera mu mtambowo.
17 The appearance of the glory of the LORD was like devouring fire on the top of the mountain in the eyes of the children of Israel.
Ulemerero wa Yehova uja unkaoneka ngati malawi a moto pamwamba pa phirilo.
18 Moses entered into the midst of the cloud, and went up on the mountain; and Moses was on the mountain forty days and forty nights.
Ndipo Mose analowa mʼmitambo nakwera phiri. Iye anakhala ku phiriko 40 usana ndi usiku.

< Exodus 24 >