< Deuteronomy 18 >

1 The cohanim the Levites, all the tribe of Levi, shall have no portion nor inheritance with Israel: they shall eat the offerings of the LORD made by fire, and his inheritance.
Ansembe Achilevi amene ndi fuko lonse la Alevi, asapatsidwe malo kapena cholowa pakati pa Aisraeli. Iwowa azidzadya zoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe, popeza zimenezo ndiye cholowa chawo.
2 They shall have no inheritance among their brothers: the LORD is their inheritance, as he has spoken to them.
Iwowa sadzakhala ndi cholowa pakati pa abale awo pakuti Yehova ndiye cholowa chawo monga anawalonjezera.
3 This shall be the cohanim' due from the people, from those who offer a sacrifice, whether it be ox or sheep, that they shall give to the cohen the shoulder, and the two cheeks, and the maw.
Anthu amene abwera kudzapereka nsembe ya ngʼombe kapena nkhosa, azipereka kwa wansembe gawo lake motere: mwendo wakutsogolo, nyama yamʼmasaya ndi zamʼkati.
4 The first fruits of your grain, of your new wine, and of your oil, and the first of the fleece of your sheep, you shall give him.
Muziwapatsa zamasika zoyamba za tirigu wanu, vinyo watsopano ndi mafuta, ndi ubweya woyamba pometa nkhosa zanu,
5 For the LORD your God has chosen him out of all your tribes, to stand to minister in the name of the LORD, him and his sons for ever.
pakuti Yehova Mulungu wanu wawasankha iwowa ndi ana awo pakati pa mafuko anu onse kuti aziyimirira ndi kutumikira mʼdzina la Yehova nthawi zonse.
6 If a Levite comes from any of your gates out of all Israel, where he lives as a foreigner, and comes with all the desire of his soul to the place which the LORD shall choose;
Ngati Mlevi asuntha achoka ku mzinda wake ndi kupita kumalo kwina kumene Yehova wasankha mu Israeli momwemo ndi mtima wake wonse,
7 then he shall minister in the name of the LORD his God, as all his brothers the Levites do, who stand there before the LORD.
kumeneko akhoza kukatumikirako mʼdzina la Yehova Mulungu wake monga Alevi anzake onse amene akutumikira pamaso pa Yehova.
8 They shall have like portions to eat, besides that which comes of the sale of his patrimony.
Iye ayenera kulandira zogawana zawo mofanana ndi anzakewo ngakhale kuti iye anagulitsa kale cholowa cha pa banja pawo.
9 When you have come into the land which the LORD your God gives you, you shall not learn to do after the abominations of those nations.
Mukafika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musakaphunzire makhalidwe onyansa a anthu a mʼdzikolo.
10 There shall not be found among you anyone who makes his son or his daughter to pass through the fire, one who practices divination, or tells fortunes, or interprets omens, or a sorcerer,
Pasapezeke pakati panu munthu wootcha pa moto mwana wake wamwamuna kapena wamkazi ngati nsembe. Asapezekenso pakati panu munthu wowombeza kapena wochita mawula, wolosera, wochita za ufiti,
11 or who casts spells, or consults a medium or a familiar spirit, or inquires of the dead.
wolodza, kapena woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndi kumafunsira nzeru kwa anthu akufawo.
12 For whoever does these things is an abomination to the LORD. And because of these abominations the LORD your God is driving them out from before you.
Aliyense wochita zinthu zotere ndi wonyansa pamaso pa Yehova, ndipo chifukwa cha zonyansa zimenezi Yehova adzakupirikitsirani mitundu ya anthu imeneyi.
13 You shall be blameless before the LORD your God.
Muzikhala angwiro pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
14 For these nations, that you shall dispossess, listen to those who practice sorcery, and to diviners; but as for you, the LORD your God has not allowed you so to do.
Mitundu ya anthu imene mudzayipirikitseyo imamvera anyanga kapena owombeza mawula. Koma inu Yehova Mulungu wanu sanakuvomerezeni kutero.
15 The LORD your God will raise up to you a prophet from the midst of you, of your brothers, like me. You shall listen to him.
Yehova Mulungu wanu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine. Muyenera kumumvera ameneyo.
16 This is according to all that you desired of the LORD your God in Horeb in the day of the assembly, saying, "Let me not hear again the voice of the LORD my God, neither let me see this great fire any more, that I not die."
Pakuti izi ndi zimene munapempha kwa Yehova Mulungu wanu ku Horebu pa tsiku la msonkhano lija pamene munati, “Ife tisamvenso mawu a Yehova Mulungu wathu kapena kuona moto woopsawu, kuopa kuti tingafe.”
17 The LORD said to me, "They have well said that which they have spoken.
Yehova anati kwa ine, “Zimene akunenazi ndi zabwino.
18 I will raise them up a prophet from among their brothers, like you; and I will put my words in his mouth, and he shall speak to them all that I shall command him.
Ndidzawawutsira mneneri ngati iwe pakati pa abale awo ndipo ndidzayika mawu anga mʼkamwa mwake ndipo adzawawuza chilichonse chimene ndidzamulamula.
19 It shall happen, that whoever will not listen to my words which he shall speak in my name, I will call him to account.
Ine mwini ndidzaweruza aliyense amene sadzamvera mawu anga amene mneneriyo adzayankhula mʼdzina langa.
20 But the prophet, who shall speak a word presumptuously in my name, which I have not commanded him to speak, or who shall speak in the name of other gods, that same prophet shall die."
Koma mneneri wonena zinthu mʼdzina langa ndisanamulamulire kutero, kapena mneneri wonenera mʼdzina la milungu ina, ayenera kuphedwa.”
21 If you say in your heart, "How shall we know the word which the LORD has not spoken?"
Mwina mukhoza kumadzifunsa kuti, “Kodi tingadziwe bwanji kuti uthengawu sanayankhule ndi Yehova?”
22 When a prophet speaks in the name of the LORD, if the thing doesn't follow, nor happen, that is the thing which the LORD has not spoken: the prophet has spoken it presumptuously, you shall not be afraid of him.
Ngati zimene mneneriyo wanenera mʼdzina la Yehova sizinachitike kapena kukwaniritsidwa, ndiye kuti umenewo si uthenga umene Yehova wayankhula. Mneneri ameneyo amangoyankhula za mʼmutu mwake ndiye musadzidzimuke naye.

< Deuteronomy 18 >