< 2 Samuel 3 >

1 Now there was a long war between the house of Saul and the house of David. But David grew stronger and stronger, while the house of Saul grew weaker and weaker.
Nkhondo ya pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide inachitika nthawi yayitali. Mphamvu za Davide zinkakulirakulirabe, pamene banja la Sauli mphamvu zake zimapita zicheperachepera.
2 Now sons were born to David in Hebron. And his firstborn was Amnon, of Ahinoam of Jezreel;
Ana aamuna a Davide amene anabadwira ku Hebroni anali awa: Woyamba anali Amnoni, amayi ake anali Ahinoamu wa ku Yezireeli.
3 and his second, Daluiah, of Abigail of Carmel; and the third, Absalom the son of Maacah the daughter of Talmai king of Geshur;
Mwana wachiwiri anali Kileabu, amayi ake anali Abigayeli mkazi wamasiye wa Nabala wa ku Karimeli. Wachitatu anali Abisalomu, amayi ake anali Maaka mwana wa Talimai mfumu ya Gesuri;
4 and the fourth, Adonijah the son of Haggith; and the fifth, Shephatiah, of Abital;
wachinayi anali Adoniya, amayi ake anali Hagiti; wachisanu, Sefatiya amayi ake anali Abitali;
5 and the sixth, Ithream, of Eglah, David's wife. These were born to David in Hebron.
ndipo wachisanu ndi chimodzi anali Itireamu, amayi ake anali Egila, mkazi wa Davide. Ana awa a Davide anabadwira ku Hebroni.
6 And it came about while there was war between the house of Saul and the house of David, that Abner was gaining power in the house of Saul.
Pamene kunali nkhondo pakati pa banja la Sauli ndi banja la Davide, Abineri anayamba kudzipatsa yekha mphamvu pakati pa banja la Sauli.
7 Now Saul had a secondary wife, Rizpah, the daughter of Aiah. And Ishbaal son of Saul said to Abner, "Why have you gone in to my father's secondary wife?"
Sauli anali ndi mzikazi dzina lake Rizipa mwana wa Ayiwa. Ndipo Isiboseti anati kwa Abineri, “Nʼchifukwa chiyani unagona ndi mzikazi wa abambo anga?”
8 Then Abner was very angry over the words of Ishbaal, and said, "Am I a dog's head? Until today, is it for myself that I have been doing all these things, showing loyalty to the house of Saul your father, to his brothers, and to his friends, and have not delivered you into the hand of David? And yet you charge me this day with a fault concerning this woman.
Abineri anakwiya kwambiri chifukwa cha zimene Isi-Boseti ananena ndipo anamuyankha kuti “Kodi ukuyesa ndine mutu wagalu umene ali mbali ya Ayuda? Lero lino ndine wokhulupirika ku nyumba ya abambo ako, Sauli ndi banja lake ndi anzake. Ine sindinakupereke kwa Davide, koma tsopano ukundinena pa cholakwa chimene ndachita pa mkazi uyu!
9 God do so to Abner, and more also, if, as the LORD has sworn to David, I do not do even so to him;
Mulungu andilange ine Abineri, andilange kwambiri, ngati sindichitira Davide zimene Yehova anamulonjeza iye mwa lumbiro.
10 to transfer the kingdom from the house of Saul, and to set up the throne of David over Israel and over Judah, from Dan even to Beersheba."
Ndidzachotsa ufumu ku nyumba ya Sauli ndi kukhazikitsa ufumu wa Davide pa Aisraeli onse ndi Yuda kuchokera ku Dani mpaka ku Beeriseba.”
11 And Ishbaal could not answer Abner another word, because he feared him.
Isiboseti sanayerekezenso kunena mawu ena kwa Abineri, chifukwa ankamuopa.
12 Abner sent messengers to David on his behalf, saying, "Whose is the land?" and saying, "Make an agreement with me, and look, my hand shall be with you, to bring all Israel around to you."
Kenaka Abineri anatuma amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Kodi dzikoli ndi la yani? Uchite mgwirizano ndi ine ndipo ndidzakuthandiza kuti Aisraeli onse azikutsatira.”
13 He said, "Good. I will make a covenant with you, but one thing I require of you. That is, you shall not see my face unless you first bring Mikal, Saul's daughter, when you come to see my face."
Davide anati, “Chabwino. Ine ndichita mgwirizano ndi iwe. Koma ndikukupempha chinthu chimodzi: Usabwere pamaso panga pokhapokha utabweretsa Mikala mwana wamkazi wa Sauli, ukamabwera kudzandiona.”
14 David sent messengers to Ishbaal, Saul's son, saying, "Give me my wife Mikal, whom I betrothed to myself for one hundred foreskins of the Philistines."
Ndipo Davide anatuma amithenga kwa Isi-Boseti mwana wa Sauli, kumulamula kuti, “Patse mkazi wanga Mikala, amene ndinamukwatira ndi makungu 100 a msonga za mavalo a Afilisti.”
15 Ishbaal sent and took her from her husband Paltiel the son of Laish.
Kotero Isi-Boseti analamulira ndipo anakamutenga kwa mwamuna wake Palitieli mwana wa Laisi.
16 But her husband went with her, weeping behind her, as far as Bahurim. Then Abner said to him, "Go back." So he went back.
Koma mwamuna wake anapita naye akulira pambuyo pake njira yonse mpaka ku Bahurimu. Kenaka Abineri anati kwa iye, “Bwerera kwanu!” Ndipo anabwerera kwawo.
17 Abner advised the elders of Israel, saying, "For some time you have wanted David to be king over you.
Abineri anakambirana ndi akuluakulu a Israeli ndipo anati, “Kwa kanthawi mwakhala mukufuna kulonga Davide kuti akhale mfumu yanu.
18 Now then do it, for the LORD has spoken of David, saying, 'By the hand of my servant David, I will save my people Israel out of the hand of the Philistines, and out of the hand of all their enemies.'"
Tsopano chitani zimenezo! Pakuti Yehova analonjeza Davide kuti, ‘Kudzera mwa mtumiki wanga Davide ndidzapulumutsa anthu anga Aisraeli mʼdzanja la Afilisti ndi kuwachotsa mʼmanja mwa adani awo.’”
19 And Abner also spoke privately to the sons of Benjamin. And Abner also spoke privately to David in Hebron all that seemed good to Israel, and to the whole house of Benjamin.
Abineri anayankhulanso nawo yekha anthu a fuko la Benjamini. Kenaka anapita ku Hebroni kukamuwuza Davide zonse zimene Aisraeli ndi fuko lonse la Benjamini amafuna kuchita.
20 So Abner came to David to Hebron, and twenty men with him. David made Abner and the men who were with him a feast.
Abineri, amene anali ndi anthu makumi awiri, atafika kwa Davide ku Hebroni, Davide anamukonzera phwando pamodzi ndi anthu ake.
21 Abner said to David, "I will arise and go, and will gather all Israel to my lord the king, that they may make a covenant with you, and that you may reign over all that your soul desires." David sent Abner away; and he left in peace.
Ndipo Abineri anawuza Davide kuti, “Loleni kuti ndipite msanga kukasonkhanitsa Aisraeli onse kuti abwere kwa inu kuno, mbuye wanga mfumu, kuti adzachite nanu pangano, ndipo kuti muzilamulira kulikonse kumene mtima wanu ufuna.” Kotero Davide analola Abineri kuti apite, ndipo anapita mwamtendere.
22 Look, the servants of David and Joab were returning from a raid, and brought in a great spoil with them. But Abner was not with David in Hebron, for he had sent him away, and he left in peace.
Nthawi yomweyo ankhondo a Davide ndi Yowabu anafika kuchokera kumene anakathira nkhondo ndipo anabweretsa katundu wambiri wolanda ku nkhondo. Koma Abineri sanalinso ndi Davide ku Hebroni, chifukwa Davide anamulola kuti apite, ndipo anapita mu mtendere.
23 When Joab and all the army who was with him had come, they told Joab, saying, "Abner the son of Ner came to David, and he has sent him away, and he left in peace."
Yowabu ndi asilikali onse amene anali naye atafika, anawuzidwa kuti Abineri mwana wa Neri anabwera kwa mfumu ndipo kuti mfumu yamulola kuti apite ndi kuti wapita ndi mtendere.
24 Then Joab came to the king, and said, "What have you done? Look, Abner came to you. Why is it that you have sent him away? Now he has gone.
Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anati, “Mwachita chiyani? Taonani, Abineri anabwera kwa inu. Nʼchifukwa chiyani mwamulola kuti apite? Tsopanotu wapitadi!
25 Don't you know the evil ways of Abner the son of Ner? He came to deceive you and to observe your movements and to learn everything that you are doing."
Inu mukumudziwa bwino Abineri mwana wa Neri. Iye anabwera kudzakunamizani ndi kudzaona mayendedwe anu ndiponso kudzaona zonse zimene mukuchita.”
26 When Joab had left David, he sent messengers after Abner, and they brought him back from the well of Sirah; but David did not know it.
Kenaka Yowabu anachoka pamaso pa Davide ndipo anatumiza amithenga kutsatira Abineri, ndipo anabwera naye kuchokera ku chitsime cha Sira. Koma Davide sanadziwe zimenezi.
27 When Abner returned to Hebron, Joab took him aside into the midst of the gate to speak with him quietly, and struck him there in the abdomen, so that he died, for the blood of Asahel his brother.
Tsono Abineri atabwerera ku Hebroni, Yowabu anamutengera pambali ku chipata, kukhala ngati akufuna kuyankhula naye mwamseri. Ndipo kumeneko pobwezera imfa ya mʼbale wake Asaheli, Yowabu analasa iyeyo mʼmimba, ndipo anafa.
28 Afterward, when David heard it, he said, "I and my kingdom are guiltless before the LORD now and forever of the blood of Abner the son of Ner.
Patapita nthawi, Davide atamva zimenezi anati, “Ine ndi ufumu wanga tidzakhala osalakwa pamaso pa Yehova pa imfa ya Abineri mwana wa Neri.
29 May it whirl over the head of Joab, and on all his father's house. Let there not fail from the house of Joab one who has an issue, or who is a leper, or who leans on a staff, or who falls by the sword, or who lacks bread."
Mlandu umenewu ukhala pa Yowabu ndi banja lonse la abambo ake! Mʼbanja la Yowabu musadzasowe munthu wodwala matenda a chizonono kapena khate, kapena wolumala woyendera ndodo kapena wophedwa ndi lupanga, kapena wosowa chakudya.”
30 So Joab and Abishai his brother killed Abner, because he had killed their brother Asahel at Gibeon in the battle.
(Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anapha Abineri chifukwa iye anapha mʼbale wawo Asaheli ku nkhondo ku Gibiyoni).
31 David said to Joab, and to all the people who were with him, "Tear your clothes, and clothe yourselves with sackcloth, and mourn before Abner." And King David followed the coffin.
Ndipo Davide anati kwa Yowabu ndi anthu onse amene anali nawo, “Ngʼambani zovala zanu ndipo muvale ziguduli, muyende mukulira patsogolo pa Abineri.” Mfumu Davide mwini anayenda motsatira chitandacho.
32 They buried Abner in Hebron: and the king lifted up his voice, and wept at the grave of Abner; and all the people wept.
Iwo anamuyika Abineri mʼmanda ku Hebroni ndipo mfumu inalira mokweza pa manda a Abineri. Ndipo anthu onse analiranso.
33 The king lamented for Abner, and said, "Should Abner die as a fool dies?
Mfumu inayimba nyimbo iyi ya maliro a Abineri: “Abineri nʼkufa motere monga mmene chimafera chitsiru.
34 Your hands were not bound in chains, your feet were not put into fetters. As a man falls before the ruthless, so you fell." All the people wept again over him.
Manja ako anali osamanga, mapazi ako anali osakulungidwa. Iwe wafa monga mmene amafera anthu pamaso pa anthu oyipa.” Ndipo anthu onse analiranso kulirira Abineri.
35 Then all the people came to persuade David to eat bread while it was yet day; but David swore, saying, "God do so to me, and more also, if I taste bread, or anything else, until the sun goes down."
Kenaka onse anabwera kwa Davide kumuwumiriza kuti adye kusanade. Koma Davide analumbira kuti, “Mulungu andilange ine, andilange kwambiri, ngati ndilawe buledi kapena chilichonse dzuwa lisanalowe!”
36 And all the people took notice of it, and it pleased them; just as everything the king did pleased the people.
Anthu onse anadziwa zimenezi ndipo zinawakondweretsa ndithu. Zonse zimene mfumu inachita zinawakondweretsa.
37 So all the people and all Israel understood that day that it was not of the king to kill Abner the son of Ner.
Kotero tsiku limeneli anthu onse ndi Aisraeli onse anadziwa kuti sikunali kufuna kwa mfumu kuti Abineri mwana wa Neri aphedwe.
38 The king said to his servants, "Do you not realize that a leader and a great man has fallen this day in Israel?
Ndipo mfumu inati kwa ankhondo ake, “Kodi inu simukudziwa kuti lero mu Israeli mwagwa kalonga ndi munthu wamkulu?
39 I am this day weak, though anointed king. And these men, the sons of Zeruiah, are too brutal for me. May the LORD reward the evildoer according to his wickedness."
Ndipo lero, ngakhale ine ndine mfumu yodzozedwa, ndilibe mphamvu ndipo ana awa a Zeruya ndi amphamvu kwa ine. Yehova abwezere woyipa molingana ndi zoyipa zake!”

< 2 Samuel 3 >