< Job 40 >
1 And the Lord addressed Job, and said,
Yehova anati kwa Yobu:
2 Will he that contendeth with the Almighty yet find fault? him that reproveth God answer this.
“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse? Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”
3 Then answered Job the Lord, and said,
Pamenepo Yobu anayankha Yehova:
4 Behold, I am too vile: what shall I answer thee? my hand do I place on my mouth.
“Ine sindili kanthu konse, kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.
5 Once have I spoken; but I will not answer: yea, twice; but I will not repeat it again.
Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho, ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”
6 Then answered the Lord unto Job out of the storm-wind, and said,
Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,
7 Do but gird up like a mighty man thy loins: I will ask thee, and do thou inform me.
“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna; ndikufunsa mafunso ndipo iwe undiyankhe.
8 Wilt thou indeed annul my decree? wilt thou condemn me, in order that thou mayest appear righteous?
“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama? Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?
9 But if thou hast an arm like God, or if thou canst thunder loudly like him:
Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu, ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?
10 Then do deck thyself with excellence and greatness, and clothe thyself in majesty and glory.
Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola, ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.
11 Scatter abroad the ragings of thy wrath, and look on every proud one, and humble him.
Tsanula ukali wako wosefukirawo, uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,
12 Look on every proud one, and bend him low; and tread down the wicked in their place.
Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse, uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.
13 Hide them in the dust altogether: bind up their faces in concealment.
Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi; ukulunge nkhope zawo mʼmanda.
14 Then will I also myself praise thee, when thy own right hand hath helped thee.
Ukatero Ine ndidzakuvomereza kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.
15 Only behold Behemoth, which I made near thee: grass he eateth like the ox.
“Taganiza za mvuwu, imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe, ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.
16 Only see, [how great] is his strength in his loins, and his force, in the muscles of his belly.
Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri, thupi lake ndi lanyonga kwambiri!
17 He stretcheth out his tail like a cedar: the sinews of his loins are closely wrapped together.
Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza; mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.
18 His bones are like pipes of brass: his frame is like bars of iron.
Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa, nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.
19 He is the first in rank of the works of God: he that made him can alone bring his sword near unto him.
Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu, komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.
20 But truly the mountains bear for him his food, and all the beasts of the field play there.
Imapeza chakudya chake ku mtunda ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.
21 Under shady trees he lieth down, in the covert of the reeds, and swamp.
Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta, imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.
22 Shady trees cover him as his shadow: willows of the brook encompass him about.
Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta; imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.
23 Behold, a river sweepeth violently along, but he hasteneth not away: he remaineth quiet, though a Jordan rusheth up to his mouth.
Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha, iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.
24 Can one catch him before his eyes? pierce his nose by means of snares?—
Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza kapena kuyikola mu msampha?