< Isaiah 10 >
1 Woe unto those that decree decrees of unrighteousness, and the writers who write down wrongful things;
Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo, kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,
2 To turn aside from judgment the needy, and to rob the just due of the poor of my people, that widows may be their prey, and [that] they may plunder the fatherless!
kuwalanda anthu osauka ufulu wawo ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga, amalanda zinthu za akazi amasiye ndi kubera ana amasiye.
3 And what will ye do on the day of the visitation, and at the desolation which will come from afar? to whom will ye flee for help? and where will ye leave your glory?
Kodi mudzatani pa tsiku la chilango, pofika chiwonongeko chochokera kutali? Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni? Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?
4 Without me they shall kneel down under the prisoners, and under the slain shall they fall. For all this his anger is not turned away, but his hand still remaineth stretched out.
Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa kapena kufa pamodzi ndi ophedwa. Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
5 Woe over Asshur, the rod of my anger; and a staff is in their hand my indignation.
“Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga, iye ndiye ndodo ya mkwiyo wanga!
6 Against a hypocritical nation will I send him, and against the people of my fury will I give him a charge, to take the spoil, and to carry off the prey, and to render them trodden down like the mire of the streets.
Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu, ndidzamutumiza kukalimbana ndi anthu amene amandikwiyitsa Ine, kukafunkha ndi kulanda chuma, ndi kuwapondereza pansi ngati matope a mʼmisewu.
7 But he deemeth it not so, and his heart doth not think so; but to destroy is in his heart, and to cut off nations not a few.
Koma izi si zimene akufuna kukachita, izi si zimene zili mʼmaganizo mwake; cholinga chake ndi kukawononga, kukapulula mitundu yambiri ya anthu.
8 For he saith, “Are not my princes altogether kings?
Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’
9 Is not Calno like Karkemish? is not Chamath like Arpad? is not Samaria like Damascus?
‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi? Kodi Hamati sali ngati Aripadi, nanga Samariya sali ngati Damasiko?
10 As my hand hath reached the kingdoms of the idols, whose graven images exceeded in number those of Jerusalem and of Samaria:
Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano, mafumu amene mafano awo ndi aakulu kupambana Yerusalemu ndi Samariya;
11 Shall I not, as I have done unto Samaria and her idols, do so unto Jerusalem and unto her idols?”
nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake monga ndinakanthira Samariya pamodzi ndi mafano ake?’”
12 Wherefore shall it come to pass, that when the Lord hath completed all his work on mount Zion and in Jerusalem, I will punish the fruit of the haughtiness of the king of Asshur, and the vain-glory of his proud looks.
Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake.
13 For he hath said, “By the strength of my hand have I done it, and by my wisdom, for I have intelligence; and I have removed the boundaries of nations, and their laid-up treasures have I plundered, and brought down low those that were powerfully seated.
Pakuti mfumuyo ikuti, “‘Ndachita zimenezi ndi dzanja langa, ndiponso ndi nzeru zanga, chifukwa ndine wozindikira zinthu. Ndinachotsa malire a mitundu ya anthu, ndinafunkha chuma chawo; ndinagonjetsa mafumu awo monga munthu wamphamvu.
14 And my hand hath reached, as a bird's nest, the wealth of the people: and as one gathereth up eggs that are forsaken, have I myself gathered up all the earth: and there was not one that moved the wing, or opened the mouth, or chirped.”
Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu ngati momwe munthu amagwirira chisa cha mbalame, ngati momwe anthu amatolera mazira osiyidwa, motero inenso ndinasonkhanitsa mayiko onse; palibe mbalame imene inakupiza mapiko ake, kapena kuyasama kukamwa kuti ilire.’”
15 Shall the axe boast itself over him that heweth therewith? or shall the saw magnify itself against him that swingeth it? as if the rod should swing about those that lift it up, or as if the staff should lift up him who is no wood.
Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito, kapena macheka angathe kudzikuza kupambana wowagwiritsa ntchito? Ndiye kukhala ngati kuti chikwapu chikuzunguza munthu amene wachinyamula, kapena ngati kuti ndodo ikuopseza amene wayinyamula!
16 Therefore will the Lord, the Eternal of hosts, send forth among his fat ones leanness; and under his glory shall be kindled a burning like the burning of a fire.
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzatumiza matenda owondetsa kwa ankhondo amphamvu; kunyada kwa mfumuyo kudzapsa ndi moto wosazima.
17 And the light of Israel shall become a fire, and his Holy One a flame; and it shall burn and devour his thorns and his briers on one day.
Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto, Woyera uja wa Israeli adzakhala ngati malawi a moto. Motowo udzawatentha ndi kuwapsereza ngati minga ndi mkandankhuku pa tsiku limodzi.
18 And the glory of his forest, and of his fruitful field, both soul and body, will he destroy: and he shall be as [a tree] eaten to powder by the worms.
Ankhondo ake adzawonongedwa ngati nkhalango yayikulu ndi ngati nthaka yachonde.
19 And the rest of the trees of his forest shall be few in number, so that a boy may write them down.
Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri, yoti ndi mwana yemwe ndi kuyiwerenga.
20 And it shall come to pass on that day, that the remnant of Israel, and such as are escaped of the house of Jacob, shall not farther lean for support upon him that smiteth them; but they shall lean upon the Lord, the Holy one of Israel, in truth.
Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli, opulumuka a nyumba ya Yakobo, sadzadaliranso anthu amene anawakantha, koma adzadalira Yehova, Woyerayo wa Israeli.
21 The remnant shall return, the remnant of Jacob, unto the mighty God.
Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo adzabwerera kwa Mulungu Wamphamvu.
22 For though thy people Israel should be as the sand of the sea, [yet] a remnant [only] of them shall return: destruction is decreed, it overfloweth with righteousness.
Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja, otsala okha ndiwo adzabwerere. Chiwonongeko chalamulidwa, chidzaonetsa chilungamo chosefukira.
23 For it is completed and decreed: the Lord, the Eternal of hosts will do it in the midst of all the land.
Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse monga momwe analamulira.
24 Therefore thus hath said the Lord the Eternal of hosts, Be not afraid, O my people that dwellest in Zion, of Asshur, who will smite thee with the rod, and lift up his staff against thee, after the manner of Egypt.
Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, “Inu anthu anga okhala mu Ziyoni, musawaope Asiriya, amene amakukanthani ndi ndodo nakumenyani ndi zibonga monga mmene Igupto anachitira.
25 For yet but a very little while more, and the indignation shall cease, and my anger shall be for their destruction.
Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu ndipo ndidzaonetsa ukali wanga pa iwo mpaka kuwawononga.”
26 And the Lord shall lift up a scourge over him like [at] the smiting of Midian at the rock of 'Oreb: and as his staff was lifted over the sea, so will he carry him off after the manner of Egypt.
Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu, monga momwe anakwapulira Amidiyani ku thanthwe la Orebu; ndipo adzatukula ndodo yake pa madzi ndikuwalanga monga analangira Igupto pa nyanja.
27 And it shall come to pass in that day, that his burden shall be removed from off thy shoulder, and his yoke from off thy neck, and the yoke shall be broken because of the fatness.
Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu, goli lawo lidzachoka mʼkhosi mwanu; golilo lidzathyoka chifukwa cha kunenepa kwambiri.
28 He cometh to 'Ayath, he passeth on to Migron; at Michmash he layeth up his baggage;
Adani alowa mu Ayati apyola ku Migironi; asunga katundu wawo ku Mikimasi.
29 They go through the pass; they take up their lodging at Geba'; Ramah trembleth; Gib'ah of Saul fleeth.
Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti, “Tikagona ku Geba” Rama akunjenjemera; Gibeya, mzinda wa Saulo ukuthawa.
30 Let thy voice resound, O daughter of Gallim; listen Layshah; O poor 'Anathoth!
Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu! Tchera khutu, iwe Laisa! Iwe Anatoti wosauka!
31 Madmenah is in motion; the inhabitants of Gebim are assembled to flee.
Anthu a ku Madimena akuthawa; anthu a ku Gebimu bisalani.
32 As yet today will he remain at Nob: then will he swing his hand against the mount of the daughter of Zion, the hill of Jerusalem.
Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu; adzagwedeza mikono yawo, kuopseza anthu a ku Ziyoni, pa phiri la Yerusalemu.
33 Behold, the Lord, the Eternal of hosts, will lop off the fruitful bough with terrific might: and those of towering growth shall be hewn down, and the high shall be laid low.
Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, adzadula mwamphamvu nthambi za mitengo, mitengo yodzikweza idzadulidwa, mitengo yayitali idzagwetsedwa.
34 And he will cut down the thickets of the forests with iron, and the Lebanon shall fall by [means of] a mighty one.
Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira; Lebanoni adzagwa pamaso pa Wamphamvu.