< Titus 1 >

1 Paul a seruaunt of God, and an Apostle of Iesus Christ, according to the faith of Gods elect, and the acknowledging of the trueth, which is according vnto godlines,
Ndine Paulo, mtumiki wa Mulungu, ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Ndinatumidwa kuti nditsogolere amene Mulungu anawasankha ku chikhulupiriro ndi ku chidziwitso cha choonadi chimene chimawafikitsa ku moyo wolemekeza Mulungu
2 Vnto the hope of eternall life, which God that cannot lie, hath promised before the world began: (aiōnios g166)
ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. (aiōnios g166)
3 But hath made his worde manifest in due time through the preaching, which is committed vnto me, according to the commandement of God our Sauiour:
Pa nthawi yake Mulungu, Mpulumutsi wathu anawulula poyera mawu ake ndipo analamula kuti ndipatsidwe udindo wolalikira uthengawu.
4 To Titus my naturall sonne according to the common faith, Grace, mercie and peace from God the Father, and from the Lord Iesus Christ our Sauiour.
Kwa Tito, mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro cha ife tonse: Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.
5 For this cause left I thee in Creta, that thou shouldest continue to redresse the thinges that remaine, and shouldest ordeine Elders in euery citie, as I appointed thee,
Ndinakusiya ku Krete kuti ulongosole zonse zimene ndinazisiya zisanathe ndiponso usankhe akulu ampingo mʼmizinda yonse, monga momwe ndinakulamulira.
6 If any be vnreproueable, the husband of one wife, hauing faithfull children, which are not slandered of riot, neither are disobedient.
Mkulu wampingo akhale munthu wopanda cholakwa, akhale wa mkazi mmodzi yekha, munthu amene ana ake ndi okhulupirira, osati amakhalidwe oyipa ndi osamvera.
7 For a Bishop must bee vnreproueable, as Gods steward, not froward, not angrie, not giuen to wine, no striker, not giuen to filthie lucre,
Popeza mkulu wa mpingo amayendetsa ntchito za banja la Mulungu, ayenera kukhala wopanda cholakwa, asakhale womva zayekha, kapena wopsa mtima msanga, kapena womwa zoledzeretsa, kapena wandewu, kapena wopeza phindu mwachinyengo.
8 But harberous, one that loueth goodnesse, wise, righteous, holy, temperate,
Koma akhale wosamala bwino alendo, wokonda zabwino, wodziretsa, wolungama, woyera mtima ndi wosunga mwambo.
9 Holding fast that faithfull worde according to doctrine, that he also may bee able to exhort with wholesome doctrine, and conuince them that say against it.
Iye ayenera kugwiritsa mawu okhulupirika monga tinaphunzitsira, kuti athe kulimbikitsa ena ndi chiphunzitso choona ndiponso kugonjetsa amene atsutsana nacho.
10 For there are many disobedient and vaine talkers and deceiuers of mindes, chiefly they of the Circumcision,
Paja pali anthu ambiri osaweruzika, makamaka mʼgulu la anthu a mdulidwe, oyankhula nkhani zopanda pake ndi kusocheretsa anzawo.
11 Whose mouthes must bee stopped, which subuert whole houses, teaching things, which they ought not, for filthie lucres sake.
Ayenera kuletsedwa kuyankhula chifukwa akusokoneza mabanja athunthu pophunzitsa zinthu zomwe sayenera kuwaphunzitsa. Iwo amachita izi kuti apeze ndalama mwachinyengo.
12 One of themselues, euen one of their owne prophets said, The Cretians are alwaies liars, euill beastes, slowe bellies.
Mneneri wina, mmodzi wa iwo omwewo anati, “Akrete nthawi zonse ndi amabodza, akhalidwe loyipitsitsa ndiponso alesi adyera.”
13 This witnesse is true: wherefore conuince them sharply, that they may be sound in ye faith,
Mawu amenewa ndi woona. Nʼchifukwa chake, uwadzudzule mwamphamvu, kuti akhale ndi chikhulupiriro choona,
14 And not taking heede to Iewish fables and commandements of men, that turne away from the trueth.
kuti asasamalenso nthano za Chiyuda, ndi malamulo a anthu amene akukana choonadi.
15 Vnto the pure are all things pure, but vnto them that are defiled, and vnbeleeuing, is nothing pure, but euen their mindes and consciences are defiled.
Kwa oyera mtima, zinthu zonse ndi zoyera, koma kwa amene ndi odetsedwa ndi osakhulupirira, palibe kanthu koyera. Kunena zoona, mitima yawo ndi chikumbumtima chawo, zonse nʼzodetsedwa.
16 They professe that they know God, but by works they deny him, and are abominable and disobedient, and vnto euery good worke reprobate.
Iwo amati amadziwa Mulungu, pamene ndi zochita zawo amamukana. Ndi anthu onyansa ndi osamvera, ndi osayenera kuchita kalikonse kabwino.

< Titus 1 >