< Mark 6 >
1 And he departed thence, and came into his owne countrey, and his disciples followed him.
Yesu anachoka kumeneko napita ku mudzi kwawo, pamodzi ndi ophunzira ake.
2 And when the Sabbath was come, he began to teach in the Synagogue, and many that heard him, were astonied, and sayd, From whence hath this man these things? and what wisdome is this that is giuen vnto him, that euen such great workes are done by his hands?
Tsiku la Sabata litafika, anayamba kuphunzitsa mʼsunagoge, ndipo ambiri amene anamumva anadabwa. Iwo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu anazitenga kuti zimenezi? Kodi ndi nzeru yotani imene munthu ameneyu wapatsidwa, kuti Iye akuchitanso zodabwitsa!
3 Is not this that carpenter Maries sonne, the brother of Iames and Ioses, and of Iuda and Simon? and are not his sisters here with vs? And they were offended in him.
Kodi uyu si mpalamatabwa uja? Kodi uyu si mwana wa Mariya ndi mʼbale wa Yakobo, Yose, Yudasi ndi Simoni? Kodi alongo ake si ali ndi ife?” Ndipo anakhumudwa naye.
4 Then Iesus sayd vnto them, A Prophet is not without honour, but in his owne countrey, and among his owne kindred, and in his own house.
Yesu anawawuza kuti, “Mneneri amalemekezedwa kulikonse kupatula kwawo, ndi pakati pa abale ake ndi a mʼbanja mwake.”
5 And he could there doe no great workes, saue that hee layd his hands vpon a fewe sicke folke, and healed them,
Sanachite zodabwitsa kumeneko, koma anangosanjika manja pa odwala ochepa ndi kuwachiritsa.
6 And he marueiled at their vnbeliefe, and went about by ye townes on euery side, teaching.
Ndipo Iye anadabwa chifukwa chakusowa chikhulupiriro kwawo. Pamenepo Yesu anayenda mudzi ndi mudzi kuphunzitsa.
7 And he called vnto him the twelue, and began to send them forth two and two, and gaue them power ouer vncleane spirits,
Atayitana khumi ndi awiriwo, Iye anawatuma awiriawiri ndipo anawapatsa ulamuliro pa mizimu yoyipa.
8 And commanded them that they should take nothing for their iourney, saue a staffe onely: neither scrip, neither bread, neither money in their girdles:
Zomwe anawalangiza ndi izi: “Musatenge kanthu ka paulendo koma ndodo yokha; osatenga buledi, thumba, kapena ndalama.
9 But that they should be shod with sandals, and that they should not put on two coates.
Muvale nsapato koma osatenga malaya apadera.
10 And he sayd vnto them, Wheresoeuer ye shall enter into an house, there abide till ye depart thence.
Pamene mulowa mʼnyumba mukakhale momwemo kufikira mutachoka mʼmudzimo.
11 And whosoeuer shall not receiue you, nor heare you, when ye depart thence, shake off the dust that is vnder your feete, for a witnes vnto them. Verely I say vnto you, It shalbe easier for Sodom, or Gomorrha at the day of iudgement, then for that citie.
Ndipo ngati pa malo ena sakakulandirani kapena kukumverani, sasani fumbi la kumapazi anu pamene mukuchoka, kuti ukhale umboni wowatsutsa.”
12 And they went out, and preached, that men should amend their liues.
Anatuluka kupita kukalalikira kuti anthu atembenuke mtima.
13 And they cast out many deuils: and they anointed many that were sicke, with oyle, and healed them.
Anatulutsa ziwanda zambiri ndi kudzoza mafuta odwala ambiri ndi kuwachiritsa.
14 Then King Herod heard of him (for his name was made manifest) and sayd, Iohn Baptist is risen againe from the dead, and therefore great workes are wrought by him.
Mfumu Herode anamva zimenezi, pakuti dzina la Yesu linali litadziwika kwambiri. Ena amati, “Yohane Mʼbatizi waukitsidwa kwa akufa, ndipo nʼchifukwa chake mphamvu zochita zodabwitsa zinkagwira ntchito mwa Iye.”
15 Other sayd, It is Elias, and some sayd, It is a Prophet, or as one of those Prophets.
Ena anati, “Iye ndi Eliya.” Enanso anati, “Ndi mneneri, ofanana ndi mmodzi wa aneneri akale.”
16 So when Herod heard it, he said, It is Iohn whom I beheaded: he is risen from the dead.
Koma Herode atamva zimenezi anati, “Yohane, munthu amene ndinamudula mutu, waukitsidwa kuchokera kwa akufa.”
17 For Herod him selfe had sent forth, and had taken Iohn, and bound him in prison for Herodias sake, which was his brother Philippes wife, because he had maried her.
Pakuti Herode iye mwini analamula kuti amumange Yohane ndi kumuyika mʼndende. Anachita izi chifukwa cha Herodia, mkazi wa mʼbale wake Filipo, amene iye anamukwatira.
18 For Iohn sayd vnto Herod, It is not lawfull for thee to haue thy brothers wife.
Pakuti Yohane ankanena kwa Herode kuti, “Sikololedwa kwa inu kuti mukwatire mkazi wa mʼbale wanu.”
19 Therefore Herodias layd waite against him, and would haue killed him, but she could not:
Ndipo Herodia anamusungira Yohane chidani ndipo anafuna kumupha, koma sanathe kutero,
20 For Herod feared Iohn, knowing that hee was a iust man, and an holy, and reuerenced him, and when he heard him, he did many things, and heard him gladly.
chifukwa Herode anaopa Yohane ndipo anamuteteza, podziwa kuti iye anali munthu wolungama ndi woyera mtima. Herode akamamva Yohane, ankathedwa nzeru; komabe amakonda kumumvetsera.
21 But the time being conuenient, when Herod on his birth day made a banket to his princes and captaines, and chiefe estates of Galile:
Pomaliza mpata unapezeka. Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwake, Herode anakonzera phwando akuluakulu ake, akulu a ankhondo ndi anthu odziwika a mu Galileya.
22 And the daughter of the same Herodias came in, and daunced, and pleased Herod, and them that sate at table together, the King sayd vnto the mayde, Aske of me what thou wilt, and I will giue it thee.
Mwana wamkazi wa Herodia atabwera ndi kudzavina, anakondweretsa Herode ndi alendo ake a pa mphwandopo. Mfumu inati kwa mtsikanayo, “Undipemphe chilichonse chimene ukuchifuna, ndipo ndidzakupatsa.”
23 And he sware vnto her, Whatsoeuer thou shalt aske of me, I will giue it thee, euen vnto the halfe of my kingdome.
Ndipo analonjeza ndi lumbiriro kuti, “Chilichonse chimene upempha ndidzakupatsa, ngakhale theka la ufumu wanga.”
24 So she went forth, and said to her mother, What shall I aske? And she said, Iohn Baptists head.
Iye anatuluka nati kwa amayi ake, “Kodi ndikapemphe chiyani?” Iye anamuyankha kuti, “Mutu wa Yohane Mʼbatizi.”
25 Then she came in straightway with haste vnto the King, and asked, saying, I would that thou shouldest giue me euen now in a charger the head of Iohn Baptist.
Nthawi yomweyo mtsikana uja anafulumira kupita komwe kunali mfumu ndi pempho lake: “Ndikufuna kuti mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.”
26 Then the King was very sory: yet for his othes sake, and for their sakes which sate at table with him, he would not refuse her.
Mfumu inamva chisoni chachikulu, koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo ake a pa mphwandolo, sanafune kumukaniza.
27 And immediatly the King sent the hangman, and gaue charge that his head shoulde be brought in. So he went and beheaded him in the prison,
Nthawi yomweyo iye anatumiza yemwe anali ndi ulamuliro wonyonga anthu kuti abweretse mutu wa Yohane. Munthuyo anapita, nakadula mutu wa Yohane mʼndende,
28 And brought his head in a charger, and gaue it to the maide, and the maide gaue it to her mother.
nabweretsa mutuwo mʼmbale. Anawupereka kwa mtsikanayo, ndipo iye anakapereka kwa amayi ake.
29 And when his disciples heard it, they came and tooke vp his body, and put it in a tombe.
Atamva izi, ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo ndi kukawuyika mʼmanda.
30 And the Apostles gathered themselues together to Iesus, and tolde him all things, both what they had done, and what they had taught.
Atumwi anasonkhana mozungulira Yesu namufotokozera zonse zomwe anachita ndi kuphunzitsa.
31 And he sayd vnto them, Come ye apart into the wildernes, and rest a while: for there were many commers and goers, that they had not leasure to eate.
Popeza kuti panali anthu ambiri amene amabwera ndi kumapita, analibe mpata wakuti adye, ndipo Iye anawawuza kuti, “Tiyeni kuno kumalo achete kuti tikapume.”
32 So they went by ship out of the way into a desart place.
Ndipo anachoka okha pa bwato napita kumalo a okhaokha.
33 But the people sawe them when they departed, and many knewe him, and ran a foote thither out of all cities, and came thither before them, and assembled vnto him.
Koma ambiri amene anawaona akuchoka anawazindikira ndipo anathamanga wapansi kuchokera mʼmidzi yonse nakayambirira kufika.
34 Then Iesus went out, and sawe a great multitude, and had compassion on them, because they were like sheepe which had no shepheard: and he began to teach them many things.
Yesu atafika ku mtunda ndi kuona gulu lalikulu la anthu, anamva nawo chisoni chifukwa anali ngati nkhosa zopanda mʼbusa. Ndipo anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambiri.
35 And when the day was nowe farre spent, his disciples came vnto him, saying, This is a desart place, and nowe the day is farre passed.
Pa nthawi iyi nʼkuti dzuwa litapendeka, ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kuthengo, ndipo ano ndi madzulo.
36 Let them depart, that they may goe into the countrey and townes about, and buy them bread: for they haue nothing to eate.
Awuzeni anthuwa azipita ku midzi ndi madera ozungulira, kuti akadzigulire kanthu kakuti adye.”
37 But he answered, and said vnto them, Giue yee them to eate. And they said vnto him, Shall we goe, and buy two hundreth peny worth of bread, and giue them to eate?
Koma Iye anayankha kuti, “Apatseni kanthu koti adye.” Iwo anati kwa Iye, “Apa pafunika ndalama za miyezi isanu ndi itatu zomwe munthu amalandira! Kodi tipite kukagwiritsa ntchito ndalama zotere kugulira buledi kuti tiwapatse adye?”
38 Then he sayde vnto them, Howe many loaues haue ye? goe and looke. And when they knewe it, they sayd, Fiue, and two fishes.
Iye anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati? Pitani mukaone.” Ataona anati kwa Iye, “Asanu ndi nsomba ziwiri.”
39 So he commanded them to make them all sit downe by companies vpon the greene grasse.
Pamenepo Yesu anawalamulira kuti awakhazike anthu pansi mʼmagulu pa msipu obiriwira.
40 Then they sate downe by rowes, by hundreds, and by fifties.
Ndipo anakhala pansi mʼmagulu a anthu 100 ndi gulu la anthu makumi asanu.
41 And he tooke the fiue loaues, and the two fishes, and looked vp to heauen, and gaue thanks, and brake the loaues, and gaue them to his disciples to set before them, and the two fishes he deuided among them all.
Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri, nayangʼana kumwamba, Iye anayamika nagawa malofu a bulediwo. Kenaka anawapatsa ophunzira ake kuti awapatse anthu. Ndipo anagawanso nsomba ziwirizo kwa onse.
42 So they did all eate, and were satisfied.
Onse anadya ndipo anakhuta,
43 And they tooke vp twelue baskets full of the fragments, and of the fishes.
ndipo ophunzira ake anatola buledi ndi nsomba zotsalira zokwanira madengu khumi ndi awiri.
44 And they that had eaten, were about fiue thousand men.
Chiwerengero cha amuna amene anadya chinali 5,000.
45 And straightway he caused his disciples to goe into the ship, and to goe before vnto the other side vnto Bethsaida, while he sent away the people.
Nthawi yomweyo Yesu anawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita ku Betisaida, pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita.
46 Then assoone as he had sent them away, he departed into a mountaine to pray.
Atawasiya, Iye anakwera ku phiri kukapemphera.
47 And when euen was come, the ship was in the mids of the sea, and he alone on the land.
Pofika madzulo, bwato linali pakati pa nyanja, ndipo Iye anali yekha pa mtunda.
48 And he saw them troubled in rowing, (for the winde was contrary vnto them) and about the fourth watch of the night, hee came vnto them, walking vpon the sea, and would haue passed by them.
Iye anaona ophunzira ake akuvutika popalasa bwato, chifukwa mphepo imawomba mokumana nawo. Pa nthawi ya mʼbandakucha Iye anafika kwa iwo akuyenda pa nyanja. Anali pafupi kuwapitirira,
49 And when they saw him walking vpon the sea, they supposed it had bene a spirit, and cried out.
koma atamuona Iye akuyenda pa nyanja, anaganiza kuti anali mzukwa. Iwo anafuwula,
50 For they all saw him, and were sore afrayd: but anon he talked with them, and said vnto them, Be ye of good comfort: it is I, be not afrayd.
pakuti onse anamuona ndipo anachita mantha. Nthawi yomweyo Iye anawayankhula nati, “Limbani mtima! Ndine. Musachite mantha.”
51 Then he went vp vnto them into the ship, and the winde ceased, and they were much more amased in them selues, and marueiled.
Ndipo Iye anakwera mʼbwato pamodzi nawo, ndipo mphepo inaleka. Iwo anadabwa kwambiri,
52 For they had not considered the matter of the loaues, because their hearts were hardened.
popeza sanazindikire zimene zinachitika pa malofu a buledi; pakuti mitima yawo inali yowuma.
53 And they came ouer, and went into the land of Gennesaret, and arriued.
Atawoloka, anafika ku Genesareti nayima pa dooko.
54 So when they were come out of the ship, straightway they knewe him,
Atangotuluka mʼbwato, anthu anamuzindikira Yesu.
55 And ran about throughout all that region round about, and began to cary hither and thither in couches all that were sicke, where they heard that he was.
Anathamanga uku ndi uko mʼdera lonse nakanyamula odwala pa machira kupita nawo kulikonse kumene anamva kuti kuli Iye.
56 And whithersoeuer he entred into townes, or cities, or villages, they laide their sicke in the streetes, and prayed him that they might touch at the least the edge of his garment. And as many as touched him, were made whole.
Ndipo kulikonse kumene anapita, ku midzi, mʼmizinda ndi madera a ku midzi, iwo anayika odwala mʼmalo a mʼmisika. Iwo anamupempha kuti awalole kuti akhudze ngakhale mphonje za mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachira.