< John 7 >

1 After these things, Iesus walked in Galile, and woulde not walke in Iudea: for the Iewes sought to kill him.
Zitatha izi Yesu anayendayenda mu Galileya, ndi cholinga chakuti asafike ku Yudeya chifukwa Ayuda kumeneko amadikira kuti amuphe.
2 Nowe the Iewes feast of the Tabernacles was at hande.
Koma phwando la Ayuda lamisasa litayandikira,
3 His brethren therefore sayde vnto him, Depart hence, and goe into Iudea, that thy disciples may see thy woorkes that thou doest.
abale a Yesu anati kwa Iye, “Inu muyenera kuchoka kuno ndi kupita ku Yudeya, kuti ophunzira anu akaone zodabwitsa zomwe mumachita.
4 For there is no man that doeth any thing secretely, and hee himselfe seeketh to be famous. If thou doest these things, shewe thy selfe to the worlde.
Palibe wina aliyense amene amafuna kukhala wodziwika amachita zinthu mseri. Popeza Inu mukuchita zinthu izi, mudzionetsere nokha ku dziko la pansi.”
5 For as yet his brethren beleeued not in him.
Pakuti ngakhale abale ake omwe sanamukhulupirire.
6 Then Iesus saide vnto them, My time is not yet come: but your time is alway readie.
Choncho Yesu anawawuza iwo kuti, “Nthawi yanga yoyenera sinafike; kwa inu nthawi ina iliyonse ndi yoyenera.
7 The world can not hate you: but me it hateth, because I testifie of it, that the workes thereof are euill.
Dziko lapansi silingakudeni inu, koma limandida Ine chifukwa Ine ndimachitira umboni kuti zomwe limachita ndi zoyipa.
8 Go ye vp vnto this feast: I wil not go vp yet vnto this feast: for my time is not yet fulfilled.
Inu pitani kuphwando. Ine sindipita tsopano kuphwando ili chifukwa kwa Ine nthawi yoyenera sinafike.”
9 These things he sayde vnto them, and abode still in Galile.
Atanena izi, Iye anakhalabe mu Galileya.
10 But assoone as his brethren were gone vp, then went hee also vp vnto the feast, not openly, but as it were priuilie.
Komabe, abale ake atanyamuka kupita kuphwando, Iye anapitanso, osati moonekera, koma mseri.
11 Then the Iewes sought him at the feast, and saide, Where is hee?
Tsopano kuphwandoko Ayuda anakamufunafuna ndi kumafunsana kuti, “Kodi munthu ameneyu ali kuti?”
12 And much murmuring was there of him among the people. Some said, He is a good man: other sayd, Nay: but he deceiueth the people.
Pakuti pa chigulu cha anthu panali kunongʼona ponseponse za Iye. Ena ankanena kuti, “Iye ndi munthu wabwino.” Ena ankayankha kuti, “Ayi, Iye amanamiza anthu.”
13 Howbeit no man spake openly of him for feare of the Iewes.
Koma panalibe amene ankanena kalikonse poyera za Iye chifukwa choopa Ayuda.
14 Nowe when halfe the feast was done, Iesus went vp into the Temple and taught.
Phwando lili pakatikati, Yesu anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kuphunzitsa.
15 And the Iewes marueiled, saving, Howe knoweth this man the Scriptures, seeing that hee neuer learned!
Ayuda anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu nzeru izi anazitenga kuti popanda kuphunzira?”
16 Iesus answered them, and saide, My doctrine is not mine, but his that sent me.
Yesu anayankha kuti, “Chiphunzitso changa si cha Ine ndekha. Chimachokera kwa Iye amene anandituma.
17 If any man will doe his will, he shall knowe of the doctrine, whether it be of God, or whether I speake of my selfe.
Ngati munthu asankha kuchita chifuniro cha Mulungu, adzazindikira ngati chiphunzitso changa nʼchochokera kwa Mulungu kapena ngati ndi mwa Ine ndekha.
18 Hee that speaketh of himselfe, seeketh his owne glorie: but hee that seeketh his glory that sent him, the same is true, and no vnrighteousnes is in him.
Iye amene amayankhula za Iye mwini amatero kuti adzipezere ulemu, koma amene amagwira ntchito kuti amene anamutuma alandire ulemu, ameneyo ndiye munthu woona; mu mtima mwake mulibe chinyengo chilichonse.
19 Did not Moses giue you a Law, and yet none of you keepeth the lawe? Why goe ye about to kill me?
Kodi Mose sanakupatseni lamulo? Komatu palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene akusunga lamulo. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kundipha Ine?”
20 The people answered, and said, Thou hast a deuil: who goeth about to kill thee?
Gulu la anthu linayankha kuti, “Iwe ndiye wagwidwa ndi ziwanda. Ndani akufuna kukupha?”
21 Iesus answered, and saide to them, I haue done one worke, and ye all maruaile.
Yesu anawawuza kuti, “Ine ndinachita chodabwitsa chimodzi ndipo inu mwadabwa.
22 Moses therefore gaue vnto you circumcision, (not because it is of Moses, but of the fathers) and ye on the Sabbath day circumcise a man.
Koma, chifukwa chakuti Mose anakulamulani kuti muzichita mdulidwe (ngakhale kuti sunachokere kwa Mose, koma kwa makolo anu), inuyo mumachita mdulidwe mwana tsiku la Sabata.
23 If a man on the Sabbath receiue circumcision, that the Lawe of Moses should not be broken, be ye angrie with me, because I haue made a man euery whit whole on the Sabbath day?
Tsopano ngati mwana angachite mdulidwe pa Sabata kuti lamulo la Mose lisaswedwe, nʼchifukwa chiyani mukundipsera mtima chifukwa chochiritsa munthu pa Sabata?
24 Iudge not according to the appearance, but iudge righteous iudgement.
Musamaweruze potengera maonekedwe chabe, koma weruzani molungama.”
25 Then saide some of them of Hierusalem, Is not this he, whom they goe about to kill?
Pa nthawi imeneyi anthu ena a ku Yerusalemu anayamba kufunsana kuti, “Kodi uyu si munthu uja akufuna kumuphayu?
26 And beholde, he speaketh openly, and they say nothing to him: doe the rulers know in deede that this is in deede that Christ?
Uyu ali apa, kuyankhula poyera, ndipo iwo sakunena kanthu kwa Iye. Kodi olamulira atsimikizadi kuti Iye ndi Khristu?
27 Howbeit we know this man whence he is: but when that Christ commeth, no man shall knowe whence he is.
Koma ife tikudziwa kumene achokera munthuyu; pamene Khristu adzabwere, palibe amene adzadziwa kumene akuchokera.”
28 Then cried Iesus in the Temple as hee taught, saying, Ye both knowe mee, and knowe whence I am: yet am I not come of my selfe, but he that sent me, is true, whome ye knowe not.
Kenaka Yesu, akuphunzitsabe mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafuwula kuti, “Zoona, mukundidziwa Ine, ndipo mukudziwa kumene ndikuchokera. Ine sindili pano mwa Ine ndekha, koma Iye amene anandituma Ine ndi woona. Inu simukumudziwa,
29 But I knowe him: for I am of him, and he hath sent me.
koma Ine ndikumudziwa chifukwa ndichokera kwa Iyeyo ndipo ndiye amene anandituma Ine.”
30 Then they sought to take him, but no man layde handes on him, because his houre was not yet come.
Chifukwa cha izi iwo anayesa kumugwira Iye, koma palibe aliyense amene anayika dzanja lake pa Iye, chifukwa nthawi yake inali isanafike.
31 Now many of the people beleeued in him, and said, When that Christ commeth, will he doe moe miracles then this man hath done?
Komabe, ambiri a mʼchigulucho anamukhulupirira Iye. Iwo anati, “Kodi pamene Khristu abwera, adzachita zizindikiro zodabwitsa zambiri kuposa munthu uyu?”
32 The Pharises heard that the people murmured these thinges of him, and the Pharises, and high Priestes sent officers to take him.
Afarisi anamva chigulucho chikunongʼona zinthu zotere za Iye. Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anatumiza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu kuti akamumange Iye.
33 Then saide Iesus vnto them, Yet am I a little while with you, and then goe I vnto him that sent mee.
Yesu anati, “Ine ndili ndi inu kwa kanthawi kochepa chabe, ndipo kenaka ndizipita kwa Iye amene anandituma Ine.
34 Ye shall seeke me, and shall not finde me, and where I am, can ye not come.
Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza; ndipo kumene Ine ndili inu simungathe kubwera.”
35 Then saide the Iewes amongs themselues, Whither will he goe, that we shall not finde him? Will he goe vnto them that are dispersed among the Grecians, and teache the Grecians?
Ayuda anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi munthu uyu akuganizira zoti apite kuti kumene ife sitingathe kumupeza Iye? Kodi Iye adzapita kumene anthu amakhala mobalalikana pakati pa Agriki, ndi kuphunzitsa Agriki?
36 What saying is this that hee saide, Ye shall seeke mee, and shall not finde mee? and where I am, cannot ye come?
Kodi Iye amatanthauza chiyani pamene anati, ‘Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza,’ ndi ‘Kumene Ine ndili, inu simungathe kubwera?’”
37 Nowe in the last and great day of the feast, Iesus stoode and cried, saying, If any man thirst, let him come vnto me, and drinke.
Pa tsiku lomaliza ndi lalikulu kwambiri laphwando, Yesu anayimirira nafuwula nati, “Ngati munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe.
38 Hee that beleeueth in mee, as saith the Scripture, out of his bellie shall flowe riuers of water of life.
Malemba kuti ‘Aliyense amene akhulupirira Ine, mitsinje yamadzi amoyo idzatuluka kuchokera mʼkati mwake.’”
39 (This spake hee of the Spirite which they that beleeued in him, should receiue: for the holy Ghost was not yet giuen, because that Iesus was not yet glorified.)
Ponena izi Iye amatanthauza Mzimu Woyera, amene adzalandire amene amakhulupirira Iye. Pa nthawiyi nʼkuti Mzimu Woyera asanaperekedwe, pakuti Yesu anali asanalemekezedwe.
40 So many of the people, when they heard this saying, said, Of a trueth this is that Prophet.
Pakumva mawu ake, ena a anthuwo anati, “Zoonadi munthu uyu ndi mneneri.”
41 Other saide, This is that Christ: and some said, But shall that Christ come out of Galile?
Ena anati, “Iye ndiye Khristu.” Komanso ena anafunsa kuti, “Kodi Khristu angachokere bwanji ku Galileya?
42 Saith not the Scripture that that Christ shall come of the seede of Dauid, and out of the towne of Beth-leem, where Dauid was?
Kodi Malemba samanena kuti Khristu adzachokera mʼbanja la Davide, ndi ku Betelehemu mu mzinda umene Davide anakhalamo?”
43 So was there dissension among the people for him.
Kotero anthu anagawikana chifukwa cha Yesu.
44 And some of them would haue taken him, but no man layde handes on him.
Ena anafuna kumugwira Iye, koma palibe amene anayika dzanja pa Iye.
45 Then came the officers to the hie Priests and Pharises, and they said vnto them, Why haue ye not brought him?
Pomaliza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu anabwerera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi amene anawafunsa iwo kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani simunamugwire Iye?”
46 The officers answered, Neuer man spake like this man.
Asilikali aja anati, “Palibe wina amene anayankhula ngati Munthu ameneyo nʼkale lonse.”
47 Then answered them the Pharises, Are yee also deceiued?
Afarisi anawadzudzula nati, “Kodi mukutanthauza kuti Iye anakunamizani inunso?”
48 Doeth any of the rulers, or of the Pharises beleeue in him?
“Kodi alipo ena a olamulira kapena a Afarisi, anamukhulupirira Iye?
49 But this people, which know not the Law, are cursed.
Ayi! Koma gulu limene silidziwa malamulo ndi lotembereredwa.”
50 Nicodemus said vnto them, (he that came to Iesus by night, and was one of them.)
Nekodimo, amene anapita kwa Yesu poyamba paja ndipo anali mmodzi wa iwo, anafunsa kuti,
51 Doth our Law iudge a man before it heare him, and knowe what he hath done?
“Kodi lamulo lathu limatsutsa munthu popanda kumva mbali yake kuti tipeze chimene wachita?”
52 They answered, and said vnto him, Art thou also of Galile? Searche and looke: for out of Galile ariseth no Prophet.
Iwo anayankha kuti, “Kodi ndiwenso wochokera ku Galileya? Tayangʼananso, ndipo udzapeza kuti mneneri sachokera ku Galileya.”
53 And euery man wet vnto his owne house.
Kenaka onse anachoka, napita kwawo.

< John 7 >