< John 4 >

1 Nowe when the Lord knew, how the Pharises had heard, that Iesus made and baptized moe disciples then Iohn,
Yesu atazindikira kuti Afarisi amva zoti Iye ankapeza ndi kubatiza ophunzira ambiri kupambana Yohane,
2 (Though Iesus himselfe baptized not: but his disciples)
(ngakhale kuti Yesuyo sankabatiza, koma ophunzira ake).
3 Hee left Iudea, and departed againe into Galile.
Iye anachoka ku Yudeya ndi kubwereranso ku Galileya.
4 And he must needes goe through Samaria.
Ndipo Iye anayenera kudutsa mu Samariya.
5 Then came hee to a citie of Samaria called Sychar, neere vnto the possession that Iacob gaue to his sonne Ioseph.
Iye anafika mʼmudzi wa Asamariya wotchedwa Sukari, pafupi ndi malo amene Yakobo anapatsa mwana wake Yosefe.
6 And there was Iacobs well. Iesus then wearied in the iourney, sate thus on the well: it was about the sixt houre.
Chitsime cha Yakobo chinali pamenepo ndipo Yesu atatopa ndi ulendo anakhala pansi pambali pa chitsimecho. Nthawi inali pafupifupi ora lachisanu ndi chimodzi masana.
7 There came a woman of Samaria to drawe water. Iesus sayd vnto her, Giue me drinke.
Mayi wa Chisamariya atabwera kudzatunga madzi, Yesu anati kwa iye, “Kodi ungandipatse madzi akumwa.”
8 For his disciples were gone away into the citie, to buy meate.
(Ophunzira ake nʼkuti atapita mʼmudzi kukagula chakudya).
9 Then sayde the woman of Samaria vnto him, Howe is it, that thou being a Iewe, askest drinke of me, which am a woman of Samaria? For the Iewes meddle not with the Samaritans.
Mayiyo anati kwa Iye, “Inu ndinu Myuda ndipo ine ndine Msamariya. Bwanji mukundipempha madzi akumwa?” (Popeza Ayuda ndi Asamariya sankayanjana).
10 Iesus answered and saide vnto her, If thou knewest that gift of God, and who it is that saieth to thee, Giue mee drinke, thou wouldest haue asked of him, and hee woulde haue giuen thee, water of life.
Yesu anamuyankha kuti, “Koma iwe ukanadziwa mphatso ya Mulungu ndi Iye amene akukupempha madzi akumwa, ukanamupempha ndipo akanakupatsa madzi amoyo.”
11 The woman saide vnto him, Sir, thou hast nothing to drawe with, and the well is deepe: from whence then hast thou that water of life?
Mayiyo anati, “Ambuye, Inu mulibe kanthu kotungira madzi ndipo chitsime ndi chakuya. Kodi madzi amoyowo mungawatenge kuti?
12 Art thou greater then our father Iacob, which gaue vs the well, and hee himselfe dranke thereof, and his sonnes, and his cattell?
Kodi Inu ndinu wamkulu kuposa kholo lathu Yakobo, amene anatipatsa chitsimechi ndipo iye ankamwanso monga anachita ana ake ndi ziweto zake?”
13 Iesus answered, and said vnto her, Whosoeuer drinketh of this water, shall thirst againe:
Yesu anayankha kuti, “Aliyense amene amamwa madzi awa amamvanso ludzu,
14 But whosoeuer drinketh of the water that I shall giue him, shall neuer be more a thirst: but the water that I shall giue him, shalbe in him a well of water, springing vp into euerlasting life. (aiōn g165, aiōnios g166)
koma aliyense amene adzamwa madzi amene Ine ndidzamupatsa sadzamvanso ludzu. Ndithudi, madzi amene ndidzamupatsa adzakhala kasupe wamadzi wotumphukira ku moyo wosatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
15 The woman said vnto him, Syr, giue me of that water, that I may not thirst, neither come hither to drawe.
Mayiyo anati kwa Iye, “Ambuye, patseni madzi amenewo kuti ndisadzamvenso ludzu ndi kumabwerabe kuno kudzatunga madzi.”
16 Iesus said vnto her, Go, call thine husband, and come hither.
Iye anamuwuza kuti, “Pita kayitane mwamuna wako ndipo ubwere naye.”
17 The woman answered, and saide, I haue no husband. Iesus said vnto her, Thou hast well said, I haue no husband.
Iye anayankha kuti, “Ine ndilibe mwamuna.” Yesu anati kwa iye, “Wakhoza ponena kuti ulibe mwamuna.
18 For thou hast had fiue husbands, and he whom thou nowe hast, is not thine husband: that saidest thou truely.
Zoona nʼzakuti iwe wakhala pa banja ndi amuna asanu, ndipo mwamuna amene uli naye tsopano si wako. Zimene wanenazi ndi zoona.”
19 The woman saide vnto him, Sir, I see that thou art a Prophet.
Mayiyo anati, “Ambuye, ine ndazindikira kuti Inu ndinu mneneri.
20 Our fathers worshipped in this mountaine, and ye say, that in Ierusalem is the place where men ought to worship.
Makolo athu ankapembedza mʼphiri ili koma inu Ayuda mumati malo amene tiyenera kupembedzera ali ku Yerusalemu.”
21 Iesus saide vnto her, Woman, beleeue me, the houre commeth, when ye shall neither in this mountaine, nor at Hierusalem worship ye Father.
Yesu anati, “Mayi inu khulupirira Ine. Nthawi ikubwera pamene inu simudzapembedza Atate mʼphiri ili kapena mu Yerusalemu.
22 Ye worship that which ye knowe not: we worship that which we knowe: for saluation is of the Iewes.
Inu Asamariya mumapembedza chimene simukuchidziwa. Ife timapembedza chimene tikuchidziwa, pakuti chipulumutso nʼchochokera kwa Ayuda.
23 But the houre commeth, and nowe is, when the true worshippers shall worship the Father in spirit, and trueth: for the Father requireth euen such to worship him.
Koma nthawi ikubwera ndipo yafika kale tsopano pamene opembedza woona adzapembedza Atate mu mzimu ndi mʼchoonadi, pakuti opembedza otere ndiwo amene Atate akuwafuna.
24 God is a Spirite, and they that worship him, must worship him in spirit and trueth.
Mulungu ndi Mzimu, ndipo omupembedza Iye ayenera kumupembedza mu mzimu ndi mʼchoonadi.”
25 The woman said vnto him, I knowe well that Messias shall come which is called Christ: when he is come, he will tell vs all things.
Mayiyo anati, “Ine ndikudziwa kuti Mesiya (wotchedwa Khristu) akubwera. Akabwera, Iye adzafotokoza zonse kwa ife.”
26 Iesus said vnto her, I am he, that speake vnto thee.
Ndipo Yesu anamuwuza kuti, “Amene ndikukuyankhulane, ndine amene.”
27 And vpon that, came his disciples, and marueiled that he talked with a woman: yet no man said vnto him, What askest thou? or why talkest thou with her?
Pa nthawi yomweyo ophunzira ake anabwerera ndipo anadabwa kupeza Iye akuyankhula ndi mayi. Koma palibe amene anamufunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” kapena, “Nʼchifukwa chiyani mukuyankhula naye?”
28 The woman then left her waterpot, and went her way into the citie, and said to the men,
Kenaka mayiyo anasiya mtsuko wamadzi, nabwerera ku mzinda ndipo anati kwa anthu,
29 Come, see a man which hath tolde me all things that euer I did: is not he that Christ?
“Tiyeni mukaone munthu amene wandiwuza ine zilizonse zimene ndinazichita. Kodi ameneyu sangakhale Khristu?”
30 Then they went out of the citie, and came vnto him.
Iwo anatuluka mʼmudziwo ndi kupita kumene kunali Iye.
31 In the meane while, the disciples prayed him, saying, Master, eate.
Pa nthawi imeneyi ndi kuti ophunzira ake akumukakamiza kuti, “Rabi idyani.”
32 But he said vnto them, I haue meate to eate that ye know not of.
Koma Iye anawawuza kuti, “Ine ndili ndi chakudya choti ndidye chimene inu simukuchidziwa.”
33 Then said ye disciples betweene themselues, Hath any man brought him meate?
Ndipo ophunzira ake anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi alipo wina amene anamubweretsera Iye chakudya?”
34 Iesus saide vnto them, My meate is that I may doe the will of him that sent me, and finish his worke.
Yesu anati, “Chakudya changa ndikuchita chifuniro cha Iye amene anandituma Ine ndi kumaliza ntchito yake.
35 Say not ye, There are yet foure moneths, and then commeth haruest? Beholde, I say vnto you, Lift vp your eyes, and looke on the regions: for they are white alreadie vnto haruest.
Kodi inu simunena kuti, ‘Kwatsala miyezi inayi ndipo kenaka kukolola?’ Ine ndikukuwuzani kuti, tsekulani maso anu ndipo muyangʼane mʼminda! Mbewu zacha kale kuti zikololedwe.
36 And he that reapeth, receiueth rewarde, and gathereth fruite vnto life eternall, that both he that soweth, and he that reapeth, might reioyce together. (aiōnios g166)
Ngakhale tsopano amene akukolola akulandira malipiro ake, ndipo akututa mbewu ku moyo wosatha kuti wofesa ndi wokolola asangalale pamodzi. (aiōnios g166)
37 For herein is the saying true, that one soweth, and an other reapeth.
Nʼchifukwa chake mawu akuti, ‘Wina amafesa ndipo wina amakolola’ ndi woona.
38 I sent you to reape that, whereon ye bestowed no labour: other men laboured, and ye are entred into their labours.
Ine ndinakutumani kukakolola zimene simunagwirire ntchito. Ena anagwira ntchito yolemetsa ndipo inu mwatuta phindu la ntchito yawo.”
39 Nowe many of the Samaritans of that citie beleeued in him, for the saying of the woman which testified, He hath tolde me all things that euer I did.
Asamariya ambiri ochokera mʼmudziwo anakhulupirira Iye chifukwa cha umboni wa mayiyo wakuti, “Iye anandiwuza ine zonse ndinazichita.”
40 Then when the Samaritans were come vnto him, they besought him, that he woulde tarie with them: and he abode there two dayes.
Choncho Asamariya atabwera kwa Iye, anamuwumiriza Iye kuti akhale nawo, ndipo Iye anakhala nawo masiku awiri.
41 And many moe beleeued because of his owne word.
Ndipo chifukwa cha mawu ake, ena ambiri anakhulupirira.
42 And they said vnto the woman, Nowe we beleeue, not because of thy saying: for we haue heard him our selues, and knowe that this is in deede that Christ the Sauiour of the world.
Iwo anati kwa mayiyo, “Ife sitikukhulupirira chifukwa cha mawu ako okha, koma tsopano ife tadzimvera tokha, ndipo tikudziwa kuti munthu uyu ndithu ndi Mpulumutsi wa dziko lapansi.”
43 So two dayes after he departed thence, and went into Galile.
Patatha masiku awiri Iye anachoka napita ku Galileya.
44 For Iesus himselfe had testified, that a Prophet hath none honour in his owne countrey.
(Tsopano Yesu mwini ananena kale kuti mneneri salandira ulemu mʼdziko lake).
45 Then when he was come into Galile, the Galileans receiued him, which had seene all the things that he did at Hierusalem at the feast: for they went also vnto the feast.
Iye atafika ku Galileya, Agalileya anamulandira. Iwo anali ataona zonse zimene anazichita mu Yerusalemu pa phwando la Paska, pakuti iwonso anali komweko.
46 And Iesus came againe into Cana a towne of Galile, where he had made of water, wine. And there was a certaine ruler, whose sonne was sicke at Capernaum.
Iye anakafikanso ku Kana wa ku Galileya, kumene anasanduliza madzi kukhala vinyo. Ndipo kumeneko kunali nduna ina ya mfumu imene mwana wake wamwamuna anali chigonere akudwala ku Kaperenawo.
47 When he heard that Iesus was come out of Iudea into Galile, he went vnto him, and besought him that he would goe downe, and heale his sonne: for he was euen ready to die.
Munthu uyu atamva kuti Yesu wafika ku Galileya kuchokera ku Yudeya, anapita kwa Iye, namupempha kuti apite akachiritse mwana wakeyo, amene anali pafupi kufa.
48 Then saide Iesus vnto him, Except ye see signes and wonders, ye will not beleeue.
Yesu anawawuza iwo kuti, “Anthu inu pokhapokha mutaona zizindikiro zodabwitsa, simudzakhulupirira.”
49 The ruler said vnto him, Syr, goe downe before my sonne dye.
Nduna ya mfumuyo inati, “Ambuye tiyeni mwana wanga asanafe.”
50 Iesus said vnto him, Go thy way, thy sonne liueth: and the man beleeued the worde that Iesus had spoken vnto him, and went his way.
Yesu anayankha kuti, “Pita. Mwana wako adzakhala ndi moyo.” Munthuyo anakhulupirira mawu a Yesu ndipo ananyamuka.
51 And as he was nowe going downe, his seruants met him, saying, Thy sonne liueth.
Iye ali pa njira, antchito ake anakumana naye, namuwuza kuti mwana wanu uja wachira.
52 Then enquired he of them the houre when he began to amend. And they said vnto him, Yesterday the seuenth houre the feuer left him.
Iye atafunsa kuti ndi nthawi yanji imene mwana wake anapeza bwino, iwo anati kwa iye, “Malungo anamusiya iye dzulo pa ora lachisanu ndi chiwiri.”
53 Then the father knew, that it was the same houre in the which Iesus had said vnto him, Thy sonne liueth. And he beleeued, and all his houshold.
Ndipo bamboyo anazindikira kuti iyi inali nthawi yomweyo imene Yesu anati kwa iye, “Mwana wako adzakhala ndi moyo.” Choncho iye ndi onse a pa banja lake anakhulupirira.
54 This second miracle did Iesus againe, after he was come out of Iudea into Galile.
Ichi ndiye chinali chizindikiro chodabwitsa chachiwiri chimene Yesu anachita atafika ku Galileya kuchokera ku Yudeya.

< John 4 >