< James 4 >

1 From whence are warres and contentions among you? are they not hence, euen of your pleasures, that fight in your members?
Nʼchiyani chimene chimayambitsa ndewu ndi mapokoso pakati panu? Kodi sizichokera ku zilakolako zimene zimalimbana mʼkati mwanu?
2 Ye lust, and haue not: ye enuie, and desire immoderately, and cannot obtaine: ye fight and warre, and get nothing, because ye aske not.
Mumalakalaka zinthu koma simuzipeza, choncho mumapha. Mumasirira zinthu koma simutha kuzipeza zimene mukufuna, choncho mumakangana ndi kumenyana. Mulibe zinthuzo chifukwa simupempha kwa Mulungu.
3 Ye aske, and receiue not, because ye aske amisse, that ye might lay the same out on your pleasures.
Koma ngakhale mumapempha simulandira, chifukwa mumapempha ndi zolinga zoyipa. Mumapempha kuti muzigwiritse ntchito pa zokusangalatsani nokha.
4 Ye adulterers and adulteresses, knowe ye not that the amitie of the world is the enimitie of God? Whosoeuer therefore will be a friend of the world, maketh himselfe the enemie of God.
Inu anthu achigololo, kodi simukudziwa kuti kuchita ubwenzi ndi dziko lapansi ndi kudana ndi Mulungu? Choncho, aliyense wosankha kukhala bwenzi la dziko lapansi amasanduka mdani wa Mulungu.
5 Doe ye thinke that the Scripture sayeth in vaine, The spirit that dwelleth in vs, lusteth after enuie?
Kapena mukuganiza kuti Malemba amanena popanda chifukwa kuti Mulungu amafunitsitsa mwansanje mzimu umene Iye anayika kuti uzikhala mwa ife?
6 But the Scripture offereth more grace, and therefore sayth, God resisteth the proude, and giueth grace to the humble.
Koma amatipatsa chisomo chochuluka. Nʼchifukwa chake Malemba amati, “Mulungu amatsutsa odzikuza, koma apereka chisomo kwa odzichepetsa.”
7 Submit your selues to God: resist the deuill, and he will flee from you.
Dziperekeni nokha kwa Mulungu. Mukaneni Mdierekezi ndipo adzakuthawani.
8 Drawe neere to God, and he will drawe neere to you. Clense your handes, ye sinners, and purge your hearts, ye double minded.
Sendezani kufupi ndi Mulungu ndipo Iye adzasendeza kwa inu. Sambani mʼmanja mwanu, inu anthu ochimwa. Yeretsani mitima yanu, inu anthu okayikira.
9 Suffer afflictions, and sorrowe ye, and weepe: let your laughter be turned into mourning, and your ioy into heauinesse.
Chitani chisoni chifukwa cha zimene mwachita, lirani misozi. Kuseka kwanu kusanduke kulira, ndipo chimwemwe chanu chisanduke chisoni.
10 Cast downe your selues before the Lord, and he will lift you vp.
Dzichepetseni pamaso pa Ambuye ndipo Iye adzakukwezani.
11 Speake not euill one of another, brethren. He that speaketh euill of his brother, or he that condemneth his brother, speaketh euill of ye Law, and condemneth the Lawe: and if thou condemnest the Lawe, thou art not an obseruer of the Lawe, but a iudge.
Abale musamanenane. Aliyense wonenera zoyipa mʼbale wake kapena kumuweruza, akusinjirira ndi kuweruza Malamulo. Pamene muweruza malamulo, ndiye kuti simukusunga malamulowo, koma mukuwaweruza.
12 There is one Lawgiuer, which is able to saue, and to destroy. Who art thou that iudgest another man?
Pali mmodzi yekha Wopereka Malamulo ndi Woweruza. Ndiye amene akhoza kupulumutsa ndi kuwononga. Kodi ndiwe yani kuti uziweruza mnzako?
13 Goe to now ye that say, To day or to morowe we will goe into such a citie, and continue there a yeere, and bye and sell, and get gaine,
Tsono tamverani, inu amene mumati, “Lero kapena mawa tipita ku mzinda wakutiwakuti, tikatha chaka chimodzi tikuchita malonda ndi kupanga ndalama.”
14 (And yet ye cannot tell what shalbe to morowe. For what is your life? It is euen a vapour that appeareth for a litle time, and afterward vanisheth away)
Chifukwa chiyani mukutero? Inu simukudziwa zimene ziti zichitike mawa. Kodi moyo wanu ndi wotani? Inu muli ngati nkhungu imene imangooneka kwa kanthawi kochepa ndipo kenaka ndikuzimirira.
15 For that ye ought to say, If the Lord will, and, if we liue, we will doe this or that.
Koma inuyo muyenera kunena kuti, “Ambuye akalola, tikadzakhala ndi moyo, tidzachita zakutizakuti.”
16 But now ye reioyce in your boastings: all such reioycing is euill.
Koma mmene zililimu mumangodzitama ndi kudzikuza. Kudzitama konse kotereku ndi koyipa.
17 Therefore, to him that knoweth how to doe well, and doeth it not, to him it is sinne.
Aliyense amene amadziwa zabwino zimene amayenera kuchita koma osazichita, ndiye kuti wachimwa.

< James 4 >