< Isaiah 13 >
1 The burden of Babel, which Isaiah the sonne of Amoz did see.
Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:
2 Lift vp a standard vpon the hie mountaine: lift vp the voyce vnto them: wagge the hand, that they may goe into the gates of the nobles.
Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see, muwafuwulire ankhondo; muwakodole kuti adzalowe pa zipata za anthu olemekezeka.
3 I haue commanded them, that I haue sanctified: and I haue called ye mightie to my wrath, and them that reioyce in my glorie.
Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga; ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira amene amadzikuza ndi chipambano changa.
4 The noyse of a multitude is in the mountaines, like a great people: a tumultuous voyce of the kingdomes of the nations gathered together: the Lord of hostes nombreth the hoste of the battell.
Tamvani phokoso ku mapiri, likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu! Tamvani phokoso pakati pa maufumu, ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi! Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera kuchita nkhondo.
5 They come from a farre countrey, from the end of the heauen: euen the Lord with the weapons of his wrath to destroy the whole land.
Iwo akuchokera ku mayiko akutali, kuchokera kumalekezero a dziko Yehova ali ndi zida zake za nkhondo kuti adzawononge dziko la Babuloni.
6 Howle you, for the day of the Lord is at hande: it shall come as a destroier from the Almightie.
Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
7 Therefore shall all hands be weakened, and all mens hearts shall melt,
Zimenezi zinafowoketsa manja onse, mtima wa munthu aliyense udzachokamo.
8 And they shalbe afraid: anguish and sorowe shall take them, and they shall haue paine, as a woman that trauaileth: euery one shall be amased at his neighbour, and their faces shalbe like flames of fire.
Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu, zowawa ndi masautso zidzawagwera; adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka. Adzayangʼanana mwamantha, nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.
9 Beholde, the day of the Lord commeth, cruel, with wrath and fierce anger to lay the land wast: and he shall destroy the sinners out of it.
Taonani, tsiku la Yehova likubwera, tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo; kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.
10 For the starres of heauen and the planets thereof shall not giue their light: the sunne shalbe darkened in his going foorth, and the moone shall not cause her light to shine.
Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga sizidzaonetsa kuwala kwawo. Dzuwa lidzada potuluka, ndipo mwezi sudzawala konse.
11 And I will visite the wickednes vpon the worlde, and their iniquitie vpon the wicked, and I wil cause the arrogancie of the proud to cease, and will cast downe the pride of tyrants.
Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake, anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo. Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza, ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.
12 I will make a man more precious then fine golde, euen a man aboue the wedge of golde of Ophir.
Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino. Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.
13 Therefore I will shake the heauen, and the earth shall remooue out of her place in the wrath of the Lord of hostes, and in the day of his fierce anger.
Tsono ndidzagwedeza miyamba ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake. Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.
14 And it shall be as a chased doe, and as a sheepe that no man taketh vp. euery man shall turne to his owne people, and flee eche one to his owne lande.
Ngati mbawala zosakidwa, ngati nkhosa zopanda wozikusa, munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo, aliyense adzathawira ku dziko lake.
15 Euery one that is founde, shall be striken through: and whosoeuer ioyneth himselfe, shall fal by the sworde.
Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa adzaphedwa momubaya ndi lupanga.
16 Their children also shall be broken in pieces before their eyes: their houses shall be spoiled, and their wiues rauished.
Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona; nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.
17 Beholde, I will stirre vp the Medes against them, which shall not regarde siluer, nor be desirous of golde.
Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva ndipo sasangalatsidwa ndi golide, kuti amenyane ndi Ababuloni.
18 With bowes also shall they destroy ye children, and shall haue no compassion vpon the fruit of the wombe, and their eies shall not spare the children.
Adzapha anyamata ndi mauta awo; sadzachitira chifundo ana ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.
19 And Babel the glorie of kingdomes, the beautie and pride of the Chaldeans, shall be as the destruction of God in Sodom and Gomorah.
Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse. Anthu ake amawunyadira. Koma Yehova adzawuwononga ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.
20 It shall not bee inhabited for euer, neither shall it be dwelled in from generation to generation: neither shall the Arabian pitch his tents there, neither shall the shepheardes make their foldes there.
Anthu sadzakhalamonso kapena kukhazikikamo pa mibado yonse; palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake, palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.
21 But Ziim shall lodge there, and their houses shall be ful of Ohim: Ostriches shall dwel there, and the Satyrs shall dance there.
Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko, nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe; mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi, ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.
22 And Iim shall crie in their palaces, and dragons in their pleasant palaces: and the time thereof is readie to come, and the daies thereof shall not be prolonged.
Mu nsanja zake muzidzalira afisi, mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe. Nthawi yake yayandikira ndipo masiku ake ali pafupi kutha.