< Galatians 6 >
1 Brethren, if a man be suddenly taken in any offence, ye which are spirituall, restore such one with the spirit of meekenes, considering thy selfe, least thou also be tempted.
Abale, ngati munthu agwa mʼtchimo lililonse, inu amene Mzimu amakutsogolerani, mumuthandize munthuyo ndi mtima wofatsa kuti akonzekenso. Koma mukhale maso kuti inu nomwe mungayesedwe.
2 Beare ye one anothers burden, and so fulfill the Lawe of Christ.
Thandizanani kusenza zolemetsa zanu, ndipo mʼnjira imeneyi mudzakwanitsa lamulo la Khristu.
3 For if any man seeme to himselfe, that he is somewhat, when he is nothing, hee deceiueth himselfe in his imagination.
Ngati wina adziyesa kanthu pamene iyeyo sali kanthu konse, akudzinamiza yekha.
4 But let euery man prooue his owne worke: and then shall he haue reioycing in himselfe onely and not in another.
Munthu aliyense aziyesa yekha ntchito zake mmene zilili. Ngati zili bwino, adzatha kunyadira chifukwa cha ntchito zake zokhazo, iyeyo asadzifanizire ndi munthu wina wake,
5 For euery man shall beare his owne burden.
pakuti aliyense ayenera kusenza katundu wake.
6 Let him that is taught in the worde, make him that hath taught him, partaker of all his goods.
Koma munthu amene akuphunzira mawu, agawireko mphunzitsi wake zinthu zonse zabwino zimene iye ali nazo.
7 Be not deceiued: God is not mocked: for whatsoeuer a man soweth, that shall hee also reape.
Musanamizidwe: nʼkosatheka kupusitsa Mulungu. Munthu amakolola zimene wafesa.
8 For hee that soweth to his flesh, shall of the flesh reape corruption: but hee that soweth to the spirit, shall of the spirit reape life euerlasting. (aiōnios )
Pakuti amene amafesa zokondweretsa thupi lake la uchimo, kuchokera ku khalidwe limenelo adzakolola chiwonongeko; amene amafesa zokondweretsa Mzimu, kuchokera kwa Mzimu adzakolola moyo wosatha. (aiōnios )
9 Let vs not therefore be weary of well doing: for in due season we shall reape, if we faint not.
Tisatope nʼkuchita zabwino, pakuti pa nthawi yoyenera tidzakolola ngati sititopa.
10 While we haue therefore time, let vs doe good vnto all men, but specially vnto them, which are of the housholde of faith.
Nʼchifukwa chake ngati tapeza mpata, tiyenera kuchitira zabwino anthu onse, makamaka amene ndi a banja la okhulupirira.
11 Ye see how large a letter I haue written vnto you with mine owne hand.
Onani zilembo zazikulu zimene ine ndikulemba ndi dzanja langa.
12 As many as desire to make a faire shewe in the flesh, they constraine you to be circumcised, onely because they would not suffer persecution for the crosse of Christ.
Onse amene akufuna kuoneka abwino pamaso pa anthu akukukakamizani kuti muchite mdulidwe. Akuchita izi ndi cholinga chimodzi chokha, chakuti apewe kuzunzidwa chifukwa cha mtanda wa Khristu.
13 For they themselues which are circumcised keepe not the law, but desire to haue you circumcised, that they might reioyce in your flesh.
Pakuti ngakhale iwowa amene anachita mdulidwe satsata Malamulo, komabe akufuna kuti muchite mdulidwe kuti anyadire mdulidwe wanuwo.
14 But God forbid that I should reioyce, but in ye crosse of our Lord Iesus Christ, whereby the world is crucified vnto me, and I vnto ye world.
Ine sindingathe kunyadira kanthu kena koma mtanda wa Ambuye athu Yesu Khristu, kudzera mwa mtandawo dziko lapansi linapachikidwa kwa ine ndi ine ku dziko lapansi.
15 For in Christ Iesus neither circumcision auaileth any thing, nor vncircumcision, but a newe creature.
Pakuti kaya mdulidwe kapena kusachita mdulidwe, sizitanthauza kanthu; chofunika ndi kulengedwa mwatsopano.
16 And as many as walke according to this rule, peace shalbe vpon them, and mercie, and vpon the Israel of God.
Mtendere ndi chifundo zikhale kwa onse amene amatsata chiphunzitso ichi, ndi pa Israeli wa Mulungu.
17 From henceforth let no man put me to busines: for I beare in my body the markes of the Lord Iesus.
Pomaliza wina asandivutitse, pakuti mʼthupi mwanga muli zizindikiro za Yesu.
18 Brethren, the grace of our Lord Iesus Christ be with your spirit, Amen. ‘Vnto the Galatians written from Rome.’
Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu zikhale ndi mzimu wanu abale. Ameni.